< Ezekieli 12 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
The word of Jehovah also came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
Son of man, thou dwell in the midst of the rebellious house, that have eyes to see, and see not, that have ears to hear, and hear not, for they are a rebellious house.
3 “Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
Therefore, thou son of man, prepare thee stuff for moving, and move by day in their sight. And thou shall move from thy place to another place in their sight. It may be they will consider, though they are a rebellious house.
4 Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
And thou shall bring forth thy stuff by day in their sight, as stuff for moving. And thou shall go forth thyself at evening in their sight, as when men go forth into exile.
5 Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
Dig thou through the wall in their sight, and carry out by that.
6 Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
Thou shall bear it upon thy shoulder in their sight, and carry it forth in the dark. Thou shall cover thy face, that thou not see the land. For I have set thee for a sign to the house of Israel.
7 Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
And I did so as I was commanded. I brought forth my stuff by day, as stuff for moving, and in the evening I dug through the wall with my hand. I brought it forth in the dark, and bore it upon my shoulder in their sight.
8 Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
And in the morning the word of Jehovah came to me, saying,
9 “Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
Son of man, has not the house of Israel, the rebellious house, said to thee, What are thou doing?
10 “Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
Say thou to them, Thus says the lord Jehovah: This burden concerns the ruler in Jerusalem, and all the house of Israel among whom they are.
11 Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
Say, I am your sign. Just as I have done, so shall it be done to them. They shall go into exile, into captivity.
12 “Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
And the ruler who is among them shall bear upon his shoulder in the dark, and shall go forth. They shall dig through the wall to carry out by it. He shall cover his face, because he shall not see the land with his eyes.
13 Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
I will also spread my net upon him, and he shall be taken in my snare. And I will bring him to Babylon to the land of the Chaldeans, yet he shall not see it, though he shall die there.
14 Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
And I will scatter toward every wind all who are round about him to help him, and all his groups. And I will draw out the sword after them.
15 “Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
And they shall know that I am Jehovah, when I shall disperse them among the nations, and scatter them through the countries.
16 Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
But I will leave a few men of them from the sword, from the famine, and from the pestilence, that they may declare all their abominations among the nations where they come. And they shall know that I am Jehovah.
17 Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
Moreover the word of Jehovah came to me, saying,
18 “Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
Son of man, eat thy bread with quaking, and drink thy water with trembling and with fearfulness.
19 Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
And say to the people of the land, Thus says the lord Jehovah concerning the inhabitants of Jerusalem, and the land of Israel: They shall eat their bread with fearfulness, and drink their water in dismay, that her land may be desolate of all that is in it, because of the violence of all those who dwell therein.
20 Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
And the cities that are inhabited shall be laid waste, and the land shall be a desolation. And ye shall know that I am Jehovah.
21 Yehova anayankhulanso nane kuti,
And the word of Jehovah came to me, saying,
22 “Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
Son of man, what is this proverb that ye have in the land of Israel, saying, The days are prolonged, and every vision fails?
23 Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
Tell them therefore, Thus says the lord Jehovah: I will make this proverb to cease, and they shall no more use it as a proverb in Israel, but say to them, The days are at hand, and the fulfillment of every vision.
24 Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
For there shall no more be any false vision nor flattering divination within the house of Israel.
25 Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
For I am Jehovah. I will speak, and the word that I shall speak shall be performed. It shall be no more deferred. For in your days, O rebellious house, I will speak the word, and will perform it, says the lord Jehovah.
26 Yehova anandiyankhula nati:
Again the word of Jehovah came to me, saying,
27 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
Son of man, behold, those of the house of Israel say, The vision that he sees is for many day to come, and he prophesies of times that are far off.
28 “Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”
Therefore say to them, Thus says the lord Jehovah: There shall none of my words be deferred any more, but the word which I shall speak shall be performed, says the lord Jehovah.

< Ezekieli 12 >