< Eksodo 8 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
And Jehovah spoke to Moses, Go in to Pharaoh, and say to him, Thus says Jehovah, Let my people go, that they may serve me.
2 Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
And if thou refuse to let them go, behold, I will smite all thy borders with frogs.
3 Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
And the river shall swarm with frogs, which shall go up and come into thy house, and into thy bedchamber, and upon thy bed, and into the house of thy servants, and upon thy people, and into thine ovens, and into thy kneading-troughs.
4 Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
And the frogs shall come up both upon thee, and upon thy people, and upon all thy servants.
5 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
And Jehovah said to Moses, Say to Aaron, Stretch forth thy hand with thy rod over the rivers, over the streams, and over the pools, and cause frogs to come up upon the land of Egypt.
6 Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
And Aaron stretched out his hand over the waters of Egypt, and the frogs came up, and covered the land of Egypt.
7 Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
And the magicians did in like manner with their enchantments, and brought up frogs upon the land of Egypt.
8 Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
Then Pharaoh called for Moses and Aaron, and said, Entreat Jehovah, that he take away the frogs from me, and from my people, and I will let the people go, that they may sacrifice to Jehovah.
9 Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
And Moses said to Pharaoh, Have this honor over me: When shall I entreat for thee, and for thy servants, and for thy people, that the frogs be destroyed from thee and thy houses, and remain in the river only?
10 Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
And he said, Tomorrow. And he said, Be it according to thy word, that thou may know that there is none like Jehovah our God.
11 Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
And the frogs shall depart from thee, and from thy houses, and from thy servants, and from thy people, they shall remain in the river only.
12 Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
And Moses and Aaron went out from Pharaoh. And Moses cried to Jehovah concerning the frogs which he had brought upon Pharaoh.
13 Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
And Jehovah did according to the word of Moses. And the frogs died out of the houses, out of the courts, and out of the fields.
14 Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
And they gathered them together in heaps, and the land stank.
15 Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
But when Pharaoh saw that there was relief, he hardened his heart, and did not hearken to them, as Jehovah had spoken.
16 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
And Jehovah said to Moses, Say to Aaron, Stretch out thy rod, and smite the dust of the earth, that it may become lice throughout all the land of Egypt.
17 Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
And they did so. And Aaron stretched out his hand with his rod, and smote the dust of the earth. And there were lice upon man, and upon beast; all the dust of the earth became lice throughout all the land of Egypt.
18 Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
And the magicians did so with their enchantments to bring forth lice, but they could not. And there were lice upon man, and upon beast.
19 Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
Then the magicians said to Pharaoh, This is the finger of God. And Pharaoh's heart was hardened, and he did not hearken to them, as Jehovah had spoken.
20 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
And Jehovah said to Moses, Rise up early in the morning, and stand before Pharaoh. Lo, he comes forth to the water. And say to him, Thus says Jehovah, Let my people go, that they may serve me.
21 Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
Else, if thou will not let my people go, behold, I will send swarms of flies upon thee, and upon they servants, and upon thy people, and into thy houses. And the houses of the Egyptians shall be full of swarms of flies, and also the ground on which they are.
22 “Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
And in that day I will set apart the land of Goshen, in which my people dwell, that no swarms of flies shall be there, to the end thou may know that I am Jehovah in the midst of the earth.
23 Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
And I will put a division between my people and thy people. This sign shall be by tomorrow.
24 Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
And Jehovah did so, and there came grievous swarms of flies into the house of Pharaoh, and into his servants' houses. And in all the land of Egypt the land was corrupted because of the swarms of flies.
25 Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
And Pharaoh called for Moses and for Aaron, and said, Go ye, sacrifice to your God in the land.
26 Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
And Moses said, It is not right to do so, for we shall sacrifice the abomination of the Egyptians to Jehovah our God. Lo, shall we sacrifice the abomination of the Egyptians before their eyes, and will they not stone us?
27 Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
We will go three days' journey into the wilderness, and sacrifice to Jehovah our God, as he shall command us.
28 Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
And Pharaoh said, I will let you go, that ye may sacrifice to Jehovah your God in the wilderness, only ye shall not go very far away. Entreat for me.
29 Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
And Moses said, Behold, I go out from thee, and I will entreat Jehovah that the swarms of flies may depart from Pharaoh, from his servants, and from his people, tomorrow. Only let not Pharaoh deal deceitfully any more in not letting the people go to sacrifice to Jehovah.
30 Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
And Moses went out from Pharaoh, and entreated Jehovah.
31 Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
And Jehovah did according to the word of Moses, and he removed the swarms of flies from Pharaoh, from his servants, and from his people; there remained not one.
32 Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.
And Pharaoh hardened his heart this time also, and he did not let the people go.

< Eksodo 8 >