< Eksodo 27 >

1 “Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
And thou shall make the altar of acacia wood, five cubits long, and five cubits broad (the altar shall be foursquare), and the height of it shall be three cubits.
2 Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
And thou shall make the horns of it upon the four corners of it. The horns of it shall be of one piece with it, and thou shall overlay it with brass.
3 Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
And thou shall make its pots to take away its ashes, and its shovels, and its basins, and its flesh-hooks, and its firepans; all the vessels of it thou shall make of brass.
4 Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
And thou shall make for it a grating of network of brass, and upon the network thou shall make four brazen rings in the four corners of it.
5 Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
And thou shall put it under the ledge round the altar beneath, that the network may reach halfway up the altar.
6 Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
And thou shall make staves for the altar, staves of acacia wood, and overlay them with brass.
7 Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
And the staves of it shall be put into the rings, and the staves shall be upon the two sides of the altar, in bearing it.
8 Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
Thou shall make it hollow with planks. As it has been shown thee on the mount, so shall they make it.
9 “Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
And thou shall make the court of the tabernacle. For the south side southward there shall be hangings for the court of fine twined linen a hundred cubits long for one side.
10 Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
And the pillars of it shall be twenty, and their sockets twenty, of brass. The hooks of the pillars and their bands shall be of silver.
11 Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
And likewise for the north side in length there shall be hangings a hundred cubits long, and the pillars of it twenty, and their sockets twenty, of brass, the hooks of the pillars and their bands, of silver.
12 “Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
And for the breadth of the court on the west side shall be hangings of fifty cubits, their pillars ten, and their sockets ten.
13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
And the breadth of the court on the east side eastward shall be fifty cubits.
14 Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
The hangings for the one side of the gate shall be fifteen cubits, their pillars three, and their sockets three.
15 Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
And for the other side shall be hangings of fifteen cubits, their pillars three, and their sockets three.
16 “Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
And for the gate of the court shall be a screen of twenty cubits, of blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen, the work of the embroiderer, their pillars four, and their sockets four.
17 Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
All the pillars of the court round about shall be banded with silver, their hooks of silver, and their sockets of brass.
18 Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
The length of the court shall be a hundred cubits, and the breadth fifty everywhere, and the height five cubits, of fine twined linen, and their sockets of brass.
19 Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
All the instruments of the tabernacle in all the service of it, and all the pegs of it, and all the pegs of the court, shall be of brass.
20 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
And thou shall command the sons of Israel, that they bring to thee pure beaten olive oil for the light, to cause a lamp to burn continually
21 Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”
in the tent of meeting, outside the veil which is before the testimony. Aaron and his sons shall keep it in order from evening to morning before Jehovah. It shall be a statute forever throughout their generations on the behalf of the sons of Israel.

< Eksodo 27 >