< Eksodo 24 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Bwera ku phiri kuno kwa Yehova, iwe pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu a Israeli makumi asanu ndi awiri. Enanu mundipembedze muli chapatali.
And he said to Moses, Come up to Jehovah, thou, and Aaron, Nadab, and Abihu, and seventy of the elders of Israel, and worship ye afar off.
2 Koma Mose yekha ayandikire Yehova, ndipo enawo asayandikire. Komanso anthu ena onse asakwere nawe ku phiri kuno.”
And Moses alone shall come near to Jehovah, but they shall not come near, neither shall the people go up with him.
3 Tsono Mose anapita kukawuza anthu mawu onse a Yehova ndi malamulo onse, ndipo anthu onse anayankha mogwirizana kuti, “Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.”
And Moses came and told the people all the words of Jehovah, and all the ordinances. And all the people answered with one voice, and said, All the words which Jehovah has spoken will we do.
4 Ndipo Mose analemba zonse zimene Yehova ananena. Mmawa mwake Mose anadzuka nayamba kumanga guwa lansembe mʼmunsi mwa phirilo ndipo anayimika miyala khumi ndi iwiri ngati zipilala kuyimira mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
And Moses wrote all the words of Jehovah, and rose up early in the morning, and built an altar below the mount, and twelve pillars, according to the twelve tribes of Israel.
5 Kenaka Mose anatuma Aisraeli achinyamata kuti aphe ndi kukapereka kwa Yehova nsembe zopsereza zachiyanjano.
And he sent young men of the sons of Israel, who offered burnt offerings, and sacrificed peace offerings of oxen to Jehovah.
6 Mose anatenga theka la magazi ndi kuyika mʼmbale, ndipo theka linalo analiwaza pa guwa lansembe.
And Moses took half of the blood, and put it in basins, and half of the blood he sprinkled on the altar.
7 Anatenganso Buku la Chipangano ndi kuwerengera anthu. Anthuwo anayankha kuti, “Zonse zimene Yehova wanena tamva, ndipo tidzazichita.”
And he took the book of the covenant, and read in the audience of the people. And they said, All that Jehovah has spoken will we do, and be obedient.
8 Kenaka Mose anatenga magazi, nawaza anthuwo ndipo anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Yehova wapanga ndi inu molingana ndi mawu ake onsewa.”
And Moses took the blood, and sprinkled it on the people, and said, Behold the blood of the covenant that Jehovah has made with you concerning all these words.
9 Kenaka Mose pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Israeli aja anakwera ku phiri,
Then Moses, and Aaron, Nadab, and Abihu, and seventy of the elders of Israel went up.
10 ndipo anaona Mulungu wa Israeli. Pansi pa mapazi ake panali njira yoyendamo yopangidwa ndi mwala wa safiro woyalidwa bwino wa maonekedwe owala ngati thambo.
And they saw the God of Israel. And there was under his feet as it were a paved work of sapphire stone, and as it were the very heaven for clearness.
11 Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.
And he laid not his hand upon the nobles of the sons of Israel. And they beheld God, and ate and drank.
12 Yehova anati kwa Mose, “Bwera kwa ine ku phiri kuno, ndipo udikire konkuno. Ndidzakupatsa miyala imene ndalembapo malemba kuti ndiwaphunzitse.”
And Jehovah said to Moses, Come up to me onto the mount, and be there, and I will give thee the tablets of stone, and the law and the commandment, which I have written, that thou may teach them.
13 Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa.
And Moses rose up, and Joshua his minister, and Moses went up onto the mount of God.
14 Apa nʼkuti Mose atawawuza akuluakulu aja kuti, “Mudikire pano mpaka titabweranso. Aaroni ndi Huri ali nanu, aliyense amene ali ndi milandu apite kwa iwo.”
And he said to the elders, Tarry ye here for us, until we come again to you. And, behold, Aaron and Hur are with you; whoever has a case, let him come near to them.
15 Mose atakwera ku phiri kuja mtambo unaphimba phirilo.
And Moses went up onto the mount, and the cloud covered the mount.
16 Ulemerero wa Yehova unakhala pa phiri la Sinai, ndipo mtambo unaphimba phirilo kwa masiku asanu ndi limodzi. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Yehova anayitana Mose kuchokera mu mtambowo.
And the glory of Jehovah abode upon mount Sinai, and the cloud covered it six days. And the seventh day he called to Moses out of the midst of the cloud.
17 Ulemerero wa Yehova uja unkaoneka ngati malawi a moto pamwamba pa phirilo.
And the appearance of the glory of Jehovah was like devouring fire on the top of the mount in the eyes of the sons of Israel.
18 Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku.
And Moses entered into the midst of the cloud, and went up onto the mount. And Moses was on the mount forty days and forty nights.

< Eksodo 24 >