< Eksodo 20 >

1 Ndipo Mulungu anayankhula mawu onse awa nati:
And God spoke all these words, saying,
2 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
I am Jehovah thy God, who brought thee out of the land of Egypt, out of the house of bondage.
3 “Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.”
Thou shall have no other gods before me.
4 “Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
Thou shall not make to thee a graven image, nor any likeness of anything that is in heaven above, or that is on the earth beneath, or that is in the water under the earth.
5 Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane.
Thou shall not bow down thyself to them, nor serve them, for I, Jehovah thy God, am a jealous God, visiting the iniquity of the fathers upon the sons, upon the third and upon the fourth generation of those who hate me,
6 Koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda, ndi kusunga malamulo anga.
and showing loving kindness to thousands of those who love me and keep my commandments.
7 “Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
Thou shall not take the name of Jehovah thy God in vain, for Jehovah will not hold him guiltless who takes his name in vain.
8 “Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika.
Remember the sabbath day, to keep it holy.
9 Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi.
Six days thou shall labor, and do all thy work,
10 Koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi, wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu, ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu.
but the seventh day is a sabbath to Jehovah thy God. Thou shall not do any work, thou, nor thy son, nor thy daughter, thy man-servant, nor thy maid-servant, nor thy cattle, nor thy stranger that is within thy gates,
11 Pakuti Yehova anapanga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo mʼmasiku asanu ndi limodzi. Iye anapuma pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Kotero Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale loyera.
for in six days Jehovah made heaven and earth, the sea, and all that is in them, and rested the seventh day. Therefore Jehovah blessed the sabbath day, and hallowed it.
12 “Lemekeza abambo ako ndi amayi ako kuti ukhale ndi moyo wautali mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
Honor thy father and thy mother, that thy days may be long in the land which Jehovah thy God gives thee.
13 “Usaphe.
Thou shall not murder.
14 “Usachite chigololo.
Thou shall not commit adultery.
15 “Usabe.
Thou shall not steal.
16 “Usapereke umboni womunamizira mnzako.
Thou shall not bear false witness against thy neighbor.
17 “Usasirire nyumba ya mnzako. Usasirire mkazi wa mnzako kapena wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
Thou shall not covet thy neighbor's house. Thou shall not covet thy neighbor's wife, nor his man-servant, nor his maid-servant, nor his ox, nor his donkey, nor anything that is thy neighbor's.
18 Pamene anthu ankamva mabingu ndi kuona ziphaliwali ndi kumvanso lipenga ndi kuona utsi umene umafuka mʼphiri, ananjenjemera ndi mantha. Ndipo iwo anayima patali.
And all the people perceived the thunderings, and the lightnings, and the voice of the trumpet, and the mountain smoking. And when the people saw it, they trembled, and stood afar off.
19 Ndipo anati kwa Mose, “Iwe utiyankhule ndipo tidzamvera. Koma usalole kuti Mulungu atiyankhule, tingafe.”
And they said to Moses, Speak thou with us, and we will hear, but let not God speak with us, lest we die.
20 Koma Mose anati kwa anthuwo, “Musachite mantha. Mulungu wabwera kudzakuyesani kuti mukhale ndi mtima woopa Mulungu kuti musamuchimwire.”
And Moses said to the people, Fear not, for God has come to prove you, and that his fear may be before you, that ye not sin.
21 Anthu aja anayima patali koma Mose anayandikira mtambo wakuda kumene kunali Mulungu.
And the people stood afar off, and Moses drew near to the thick darkness where God was.
22 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Awuze izi Aisraeli: ‘Inu mwaona nokha kuti Ine ndakuyankhulani kuchokera kumwamba.
And Jehovah said to Moses, Thus thou shall say to the sons of Israel, Ye yourselves have seen that I have talked with you from heaven.
23 Choncho musadzipangire milungu yasiliva kapena yagolide kuti muziyipembedza pamodzi ndi Ine.’”
Ye shall not make other gods with me; gods of silver, or gods of gold, ye shall not make to you.
24 Mundimangire guwa ladothi ndipo muziperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe zanu. Pamalo paliponse pamene Ine ndidzakonza kuti muzinditamandirapo, ndidzabwera ndi kukudalitsani.
An altar of earth thou shall make to me, and shall sacrifice on it thy burnt offerings, and thy peace offerings, thy sheep, and thine oxen. In every place where I record my name I will come to thee and I will bless thee.
25 Ngati mudzandimangira guwa lansembe lamiyala, musagwiritse ntchito miyala yosema, pakuti mudzalidetsa mukadzagwiritsa ntchito zida.
And if thou make to me an altar of stone, thou shall not build it of hewn stones, for if thou lift up thy tool upon it, thou have polluted it.
26 Musamakwere pa makwerero popita pa guwa langa lansembe kuti mungaonetse maliseche anu.
Neither shall thou go up by steps to my altar, that thy nakedness be not uncovered on it.

< Eksodo 20 >