< Estere 7 >

1 Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
So the king and Haman came to banquet with Esther the queen.
2 Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
And the king said again to Esther on the second day at the banquet of wine, What is thy petition, queen Esther? And it shall be granted thee. And what is thy request? Even to the half of the kingdom it shall be performed.
3 Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
Then Esther the queen answered and said, If I have found favor in thy sight, O king, and if it please the king, let my life be given me at my petition, and my people at my request.
4 Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
For we are sold, I and my people, to be destroyed, to be slain, and to perish. But if we had been sold for bondmen and bondwomen, I would have held my peace, although the adversary could not have compensated for the king's damage.
5 Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
Then king Ahasuerus spoke and said to Esther the queen, Who is he, and where is he, who dares presume in his heart to do so?
6 Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
And Esther said, An adversary and an enemy, even this wicked Haman. Then Haman was afraid before the king and the queen.
7 Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
And the king arose in his wrath from the banquet of wine and went into the palace garden. And Haman stood up to make request for his life to Esther the queen, for he saw that there was evil determined against him by the king.
8 Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
Then the king returned out of the palace garden into the place of the banquet of wine, and Haman was fallen upon the couch on which Esther was. Then the king said, Will he even force the queen before me in the house? As the word went out of the king's mouth, they covered Haman's face.
9 Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
Then Harbonah, one of the chamberlains who were before the king said, Behold also, the gallows fifty cubits high, which Haman has made for Mordecai, who spoke good for the king, stands in the house of Haman. And the king said, Hang him on it.
10 Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.
So they hanged Haman on the gallows that he had prepared for Mordecai. Then the king's wrath was pacified.

< Estere 7 >