< Deuteronomo 32 >

1 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
Give ear, ye heavens, and I will speak, and let the earth hear the words of my mouth.
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
My doctrine shall drop as the rain. My speech shall distil as the dew, as the small rain upon the tender grass, and as the showers upon the herb.
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
For I will proclaim the name of Jehovah. Ascribe ye greatness to our God.
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
The Rock, his work is perfect, for all his ways are justice, a God of faithfulness and without iniquity, just and right is he.
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
They have dealt corruptly with him. They are not his sons, it is their blemish, a perverse and crooked generation.
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
Do ye thus requite Jehovah, O foolish people and unwise? Is not he thy father who has bought thee? He has made thee, and established thee.
7 Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
Remember the days of old. Consider the years of many generations. Ask thy father, and he will show thee, thine elders, and they will tell thee.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
When the Most High gave to the nations their inheritance, when he separated the sons of men, he set the bounds of the peoples according to the number of the sons of Israel.
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
For Jehovah's portion is his people. Jacob is the lot of his inheritance.
10 Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
He found him in a desert land, and in the waste howling wilderness. He compassed him about. He cared for him. He kept him as the apple of his eye.
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
As an eagle that stirs up her nest, that flutters over her young, he spread abroad his wings. He took them. He bore them on his pinions.
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
Jehovah alone led him, and there was no foreign god with him.
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
He made him ride on the high places of the earth, and he ate the increase of the field, and he made him to suck honey out of the rock, and oil out of the flinty rock,
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
butter of the herd, and milk of the flock, with fat of lambs, and rams of the breed of Bashan, and goats, with the finest of the wheat, and of the blood of the grape thou drank wine.
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
But Jeshurun grew fat, and kicked. Thou have grown fat. Thou have grown thick. Thou have become sleek. Then he forsook God who made him, and lightly esteemed the Rock of his salvation.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
They moved him to jealousy with strange gods. With abominations they provoked him to anger.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
They sacrificed to demons, not God, to gods that they knew not, to new gods that came up of late, which your fathers did not dread.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
Thou are unmindful of the Rock that begot thee, and have forgotten God who gave thee birth.
19 Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
And Jehovah saw, and abhorred, because of the provocation of his sons and his daughters.
20 Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
And he said, I will hide my face from them. I will see what their end shall be. For they are a very perverse generation, sons in whom is no faithfulness.
21 Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
They have moved me to jealousy with that which is not God. They have provoked me to anger with their vanities, and I will move them to jealousy with a non-nation. I will provoke them to anger with a foolish nation.
22 Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol h7585)
For a fire is kindled in my anger, and burns to the lowest Sheol, and devours the earth with its increase, and sets on fire the foundations of the mountains. (Sheol h7585)
23 “Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
I will heap evils upon them. I will spend my arrows upon them,
24 Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
to be wasted with hunger, and devoured with burning heat and bitter destruction. And I will send upon them the teeth of beasts, with the poison of crawling things of the dust.
25 Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
Outside the sword shall bereave, and in the chambers terror, to both young man and virgin, the suckling with the man of gray hairs.
26 Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
I said, I would scatter them afar, I would make the remembrance of them to cease from among men,
27 koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
were it not that I feared the provocation of the enemy, lest their adversaries should judge amiss, lest they should say, Our hand is exalted, and Jehovah has not done all this.
28 Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
For they are a nation void of counsel, and there is no understanding in them.
29 Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
Oh that they were wise, that they understood this, that they would consider their latter end!
30 Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
How should one chase a thousand, and two put ten thousand to flight unless their Rock had sold them, and Jehovah had delivered them up?
31 Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
For their rock is not as our Rock, even our enemies themselves being judges.
32 Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
For their vine is of the vine of Sodom, and of the fields of Gomorrah. Their grapes are grapes of gall, their clusters are bitter.
33 Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
Their wine is the poison of serpents, and the cruel venom of asps.
34 “Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
Is not this laid up in store with me, sealed up among my treasures?
35 Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
Vengeance is for me, and recompense at the time when their foot shall slide. For the day of their calamity is at hand, and the things that are to come upon them shall make haste.
36 Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
For Jehovah will judge his people, and regrets for his servants, when he sees that their power is gone, and there is none remaining, shut up or left at large.
37 Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
And he will say, Where are their gods, the rock in which they took refuge,
38 milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
which ate the fat of their sacrifices, and drank the wine of their drink offering? Let them rise up and help you, let them be your protection.
39 “Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
See now that I, even I, am he, and there is no god with me. I kill, and I make alive. I wound, and I heal. And there is none that can deliver out of my hand.
40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
For I lift up my hand to heaven, and say, As I live forever,
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
if I whet my glittering sword, and my hand takes hold on judgment, I will render vengeance to my adversaries, and will recompense those who hate me.
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
I will make my arrows drunk with blood, and my sword shall devour flesh, with the blood of the slain and the captives, from the head of the leaders of the enemy.
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
Rejoice, O ye Gentiles, with his people. For he will avenge the blood of his servants, and will render vengeance to his adversaries, and will recompense those who hate him, and will make expiation for his land, for his people.
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
And Moses came and spoke all the words of this song in the ears of the people, he and Joshua the son of Nun.
45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
And Moses made an end of speaking all these words to all Israel.
46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
And he said to them, Set your heart to all the words which I testify to you this day, which ye shall command your sons to observe to do, even all the words of this law.
47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
For it is no vain thing for you, because it is your life, and through this thing ye shall prolong your days in the land where ye go over the Jordan to possess it.
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses that selfsame day, saying,
49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
Get thee up onto this mountain of Abarim, to mount Nebo, which is in the land of Moab, that is opposite Jericho, and behold the land of Canaan, which I give to the sons of Israel for a possession.
50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
And die on the mount where thou go up, and be gathered to thy people, as Aaron thy brother died in mount Hor, and was gathered to his people,
51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
because ye trespassed against me in the midst of the sons of Israel at the waters of Meribah of Kadesh, in the wilderness of Zin, because ye did not sanctify me in the midst of the sons of Israel.
52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”
For thou shall see the land before thee, but thou shall not go there into the land which I give the sons of Israel.

< Deuteronomo 32 >