< Danieli 6 >

1 Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
It pleased Darius to set over the kingdom a hundred and twenty satraps, who should be throughout the whole kingdom,
2 ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
and over them three presidents, of whom Daniel was one, that these satraps might give account to them, and that the king should have no damage.
3 Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
Then this Daniel was distinguished above the presidents and the satraps, because an excellent spirit was in him, and the king thought to set him over the whole realm.
4 Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
Then the presidents and the satraps sought to find occasion against Daniel concerning the kingdom, but they could find no occasion nor fault, inasmuch as he was faithful, nor was there any error or fault found in him.
5 Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
Then these men said, We shall not find any occasion against this Daniel unless we find it against him concerning the law of his God.
6 Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
Then these presidents and satraps assembled together to the king, and said thus to him: King Darius, live forever.
7 Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
All the presidents of the kingdom, the deputies and the satraps, the counselors and the governors, have consulted together to establish a royal statute, and to make a strong interdict, that whoever shall ask a petition of any god or man for thirty days, except of thee, O king, he shall be cast into the den of lions.
8 Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
Now, O king, establish the interdict, and sign the writing, that it be not changed, according to the law of the Medes and Persians, which does not alter.
9 Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
Therefore king Darius signed the writing and the interdict.
10 Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
And when Daniel knew that the writing was signed, he went into his house (now his windows were open in his chamber toward Jerusalem) and he knelt upon his knees three times a day, and prayed, and gave thanks before his God, as he did formerly.
11 Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
Then these men assembled together, and found Daniel making petition and supplication before his God.
12 Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
Then they came near, and spoke before the king concerning the king's interdict. Have thou not signed an interdict, that every man who shall make petition to any god or man within thirty days, except to thee, O king, shall be cast into the den of lions? The king answered and said, The thing is true according to the law of the Medes and Persians, which does not alter.
13 Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
Then they answered and said before the king, That Daniel, who is of the sons of the captivity of Judah, does not regard thee, O king, nor the interdict that thou have signed, but makes his petition three times a day.
14 Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
Then the king, when he heard these words, was very displeased, and set his heart on Daniel to deliver him. And he labored till the going down of the sun to rescue him.
15 Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
Then these men assembled together to the king, and said to the king, Know, O king, that it is a law of the Medes and Persians, that no interdict nor statute which the king establishes may be changed.
16 Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
Then the king commanded, and they brought Daniel, and cast him into the den of lions. Now the king spoke and said to Daniel, Thy God whom thou serve continually, he will deliver thee.
17 Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
And a stone was brought, and laid upon the mouth of the den. And the king sealed it with his own signet, and with the signet of his lords, that nothing might be changed concerning Daniel.
18 Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
Then the king went to his palace, and passed the night fasting, nor were instruments of music brought before him. And his sleep fled from him.
19 Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
Then the king arose very early in the morning, and went in haste to the den of lions.
20 Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
And when he came near to the den to Daniel, he cried with a lamentable voice. The king spoke and said to Daniel, O Daniel, servant of the living God, is thy God, whom thou serve continually, able to deliver thee from the lions?
21 Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
Then Daniel said to the king, O king, live forever.
22 Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
My God has sent his agent, and has shut the lions' mouths, and they have not hurt me, inasmuch as before him innocence was found in me. And also before thee, O king, I have done no harm.
23 Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
Then the king was exceedingly glad, and commanded that they should take Daniel up out of the den. So Daniel was taken up out of the den, and no manner of harm was found upon him, because he had trusted in his God.
24 Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
And the king commanded, and they brought those men who had accused Daniel, and they cast them into the den of lions, them, their sons, and their wives. And the lions had the mastery of them, and broke all their bones in pieces, before they came to the bottom of the den.
25 Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
Then king Darius wrote to all the peoples, nations, and languages, who dwell in all the earth: Peace be multiplied to you.
26 “Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
I make a decree, that in all the dominion of my kingdom men tremble and fear before the God of Daniel, for he is the living God, and steadfast forever. And his kingdom is that which shall not be destroyed, and his dominion shall be even to the end.
27 Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
He delivers and rescues, and he works signs and wonders in heaven and in earth, who has delivered Daniel from the power of the lions.
28 Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.
So this Daniel prospered in the reign of Darius, and in the reign of Cyrus the Persian.

< Danieli 6 >