< 2 Mbiri 7 >

1 Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo.
Now when Solomon had made an end of praying, the fire came down from heaven, and consumed the burnt offering and the sacrifices. And the glory of Jehovah filled the house.
2 Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova.
And the priests could not enter into the house of Jehovah, because the glory of Jehovah filled Jehovah's house.
3 Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti, “Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala chikhalire”
And all the sons of Israel looked on when the fire came down, and the glory of Jehovah was upon the house. And they bowed themselves with their faces to the ground upon the pavement, and worshiped, and gave thanks to Jehovah, saying, For he is good. For his loving kindness is forever.
4 Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.
Then the king and all the people offered sacrifice before Jehovah.
5 Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu.
And king Solomon offered a sacrifice of twenty-two thousand oxen, and a hundred and twenty thousand sheep. So the king and all the people dedicated the house of God.
6 Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.
And the priests stood according to their offices, also the Levites with instruments of music of Jehovah, which David the king had made to give thanks to Jehovah (for his loving kindness is forever) when David praised by their ministry, and the priests sounded trumpets before them. And all Israel stood.
7 Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.
Moreover Solomon hallowed the middle of the court that was before the house of Jehovah. For there he offered the burnt offerings, and the fat of the peace offerings, because the brazen altar which Solomon had made was not able to receive the burnt offering, and the meal offering, and the fat.
8 Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto.
So Solomon held the feast at that time seven days, and all Israel with him, a very great assembly, from the entrance of Hamath to the brook of Egypt.
9 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero.
And on the eighth day they held a solemn assembly. For they kept the dedication of the altar seven days, and the feast seven days.
10 Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.
And on the twenty-third day of the seventh month he sent the people away to their tents, joyful and glad of heart for the goodness that Jehovah had shown to David, and to Solomon, and to Israel his people.
11 Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu,
Thus Solomon finished the house of Jehovah, and the king's house. And all that came into Solomon's heart to make in the house of Jehovah, and in his own house, he caused to prosper.
12 Yehova anamuonekera usiku ndipo anati: “Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.
And Jehovah appeared to Solomon by night, and said to him, I have heard thy prayer, and have chosen this place to myself for a house of sacrifice.
13 “Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu,
If I shut up the heavens so that there is no rain, or if I command the locust to devour the land, or if I send pestilence among my people,
14 ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo.
if my people, who are called by my name, shall humble themselves, and pray, and seek my face, and turn from their wicked ways, then I will hear from heaven, and will forgive their sin, and will heal their land.
15 Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano.
Now my eyes shall be open, and my ears attend to the prayer that is made in this place.
16 Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.
For now I have chosen and hallowed this house, that my name may be there forever, and my eyes and my heart shall be there perpetually.
17 “Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
And as for thee, if thou will walk before me as David thy father walked, and do according to all that I have commanded thee, and will keep my statutes and mine ordinances,
18 Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’
then I will establish the throne of thy kingdom, according as I covenanted with David thy father, saying, There shall not fail thee a man to be ruler in Israel.
19 “Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
But if ye turn away, and forsake my statutes and my commandments which I have set before you, and shall go and serve other gods, and worship them,
20 pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
then I will pluck them up by the roots out of my land which I have given them. And this house, which I have hallowed for my name, I will cast out of my sight, and I will make it a proverb and a byword among all peoples.
21 Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
And this house, which is so high, everyone who passes by it shall be astonished, and shall say, Why has Jehovah done thus to this land, and to this house?
22 Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”
And they shall answer, Because they forsook Jehovah, the God of their fathers, who brought them forth out of the land of Egypt, and laid hold on other gods, and worshiped them, and served them; therefore he has brought all this evil upon them.

< 2 Mbiri 7 >