< 2 Mbiri 6 >

1 Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda;
Then Solomon spoke, Jehovah has said that he would dwell in the thick darkness.
2 ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”
But I have built for thee a house of habitation, and a place for thee to dwell in forever.
3 Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa.
And the king turned his face, and blessed all the assembly of Israel. And all the assembly of Israel stood.
4 Ndipo inati, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati,
And he said, Blessed be Jehovah, the God of Israel, who spoke with his mouth to David my father, and has with his hands fulfilled it, saying,
5 ‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba kuti ndizikhalamo kapena munthu wina aliyense kuti akhale mtsogoleri wa Aisraeli anthu anga.
Since the day that I brought forth my people out of the land of Egypt, I chose no city out of all the tribes of Israel to build a house in that my name might be there. Neither did I choose any man to be ruler over my people Israel.
6 Koma tsopano ndasankha Yerusalemu kuti Dzina langa likhale kumeneko ndiponso ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’
But I have chosen Jerusalem that my name might be there. And have chosen David to be over my people Israel.
7 “Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire Nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
Now it was in the heart of David my father to build a house for the name of Jehovah, the God of Israel.
8 Koma Yehova ananena kwa abambo anga Davide kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira Nyumba dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo.
But Jehovah said to David my father, Whereas it was in thy heart to build a house for my name, thou did well that it was in thy heart.
9 Komatu si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye amene adzandimangire Nyumba.’
Nevertheless thou shall not build the house, but thy son who shall come forth out of thy loins, he shall build the house for my name.
10 “Yehova wasunga zimene analonjeza. Ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide, ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova Mulungu wa Israeli.
And Jehovah has performed his word that he spoke. For I have risen up in the place of David my father, and sit on the throne of Israel, as Jehovah promised, and have built the house for the name of Jehovah, the God of Israel.
11 Mʼmenemo ndayikamo Bokosi la Chipangano, mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi ana a Israeli.”
And there I have set the ark in which is the covenant of Jehovah, which he made with the sons of Israel.
12 Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova patsogolo pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake.
And he stood before the altar of Jehovah in the presence of all the assembly of Israel, and spread forth his hands.
13 Iyeyo anali atapanga nsanja yamkuwa, kutalika kwake kunali mamita awiri, mulifupi mwake munali mamita awiri, msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka ndipo nsanjayo anayimika pakati pa bwalo lakunja. Iye anayimirira pa nsanjapo nagwada pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba.
For Solomon had made a brazen scaffold, five cubits long, and five cubits broad, and three cubits high, and had set it in the midst of the court. And upon it he stood, and knelt down upon his knees before all the assembly of Israel, and spread forth his hands toward heaven.
14 Iye anati, “Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pa dziko. Inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse.
And he said, O Jehovah, the God of Israel, there is no God like thee, in heaven, or on earth, who keep covenant and loving kindness with thy servants, who walk before thee with all their heart,
15 Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu monga mmene tikuonera lero lino.
who have kept with thy servant David my father that which thou promised him. Yea, thou spoke with thy mouth, and have fulfilled it with thy hand, as it is this day.
16 “Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo ndi kusunga malamulo anga monga iwe wachitira.’
Now therefore, O Jehovah, the God of Israel, keep with thy servant David my father that which thou have promised him, saying, There shall not fail thee a man in my sight to sit on the throne of Israel, if only thy sons take heed to their way, to walk in my law as thou have walked before me.
17 Ndipo tsopano Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide.
Now therefore, O Jehovah, the God of Israel, let thy word be verified, which thou spoke to thy servant David.
18 “Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi ndi munthu? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga!
But will God in very deed dwell with men on the earth? Behold, heaven and the heaven of heavens cannot contain thee. How much less this house which I have built!
19 Koma Inu Yehova, Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu.
Yet have thou respect to the prayer of thy servant, and to his supplication, O Jehovah my God, to hearken to the cry and to the prayer which thy servant prays before thee,
20 Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usana ndi usiku, malo ano amene Inu munati mudzayikamo Dzina lanu, imvani pemphero la mtumiki wanu limene akupemphera pa malo ano.
that thine eyes may be open toward this house day and night, even toward the place of which thou have said that thou would put thy name there, to hearken to the prayer which thy servant shall pray toward this place.
21 Imvani mapembedzero a mtumiki wanu ndi a anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.
And hearken thou to the supplications of thy servant, and of thy people Israel, when they shall pray toward this place. Yea, hear thou from thy dwelling-place, even from heaven, and when thou hear forgive.
22 “Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino,
If a man sins against his neighbor, and an oath be laid upon him to cause him to swear, and he comes and swears before thine altar in this house,
23 imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.
then hear thou from heaven, and do, and judge thy servants, requiting the wicked, to bring his way upon his own head, and justifying the righteous, to give him according to his righteousness.
24 “Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera pamaso panu mʼNyumba ino,
And if thy people Israel be smitten down before the enemy because they have sinned against thee, and shall turn again and confess thy name, and pray and make supplication before thee in this house,
25 pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa iwo ndi makolo awo.
then hear thou from heaven, and forgive the sin of thy people Israel, and bring them again to the land which thou gave to them and to their fathers.
26 “Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga,
When the heavens are shut up, and there is no rain, because they have sinned against thee, if they pray toward this place, and confess thy name, and turn from their sin when thou do afflict them,
27 pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera, ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.
then hear thou in heaven, and forgive the sin of thy servants, and of thy people Israel, when thou teach them the good way wherein they should walk, and send rain upon thy land, which thou have given to thy people for an inheritance.
28 “Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene adani azungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera,
If there be in the land famine, if there be pestilence, if there be blight or mildew, locust or caterpillar, if their enemies besiege them in the land of their cities, whatever plague or whatever sickness there be,
29 ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso ake ndi ululu wake, ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino,
whatever prayer and supplication be made by any man, or by all thy people Israel, who shall know every man his own plague and his own sorrow, and shall spread forth his hands toward this house,
30 pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita popeza Inu mumadziwa mtima wake, (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu),
then hear thou from heaven thy dwelling-place and forgive, and render to every man according to all his ways, whose heart thou know, (for thou, even thou only, know the hearts of the sons of men),
31 motero iwo adzakuopani ndipo adzayenda mʼnjira zanu masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.
that they may fear thee, to walk in thy ways so long as they live in the land which thou gave to our fathers.
32 “Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu lotchukali, ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino,
Moreover concerning the foreigner, who is not of thy people Israel, when he shall come from a far country for thy great name's sake, and thy mighty hand, and thine outstretched arm, when they shall come and pray toward this house,
33 pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi dzina lanu.
then hear thou from heaven, even from thy dwelling-place, and do according to all that the foreigner calls to thee for, that all the peoples of the earth may know thy name, and fear thee, as do thy people Israel, and that they may know that this house which I have built is called by thy name.
34 “Anthu akapita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo akapemphera moyangʼana mzinda uno umene mwausankha ndi Nyumba yanu imene ndakumangirani,
If thy people go out to battle against their enemies, by whatever way thou shall send them, and they pray to thee toward this city which thou have chosen, and the house which I have built for thy name,
35 pamenepo imvani kumwamba pemphero lawo ndi kupempha kwawo ndipo muwapulumutse.
then hear thou from heaven their prayer and their supplication, and maintain their cause.
36 “Pamene achimwira inu, pakuti palibe amene sachimwa, ndipo inu mwawakwiyira ndi kuwapereka kwa adani awo, amene awatenga ukapolo ku dziko lawo lakutali kapena pafupi.
If they sin against thee (for there is no man that sins not), and thou be angry with them, and deliver them to the enemy, so that they carry them away captive to a land far off or near,
37 Ngati asintha mitima yawo ku dziko limene ali akapolo ndi kulapa ndi kukudandaulirani inu mʼdziko la ukapolo wawo ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa ndipo tachita moyipa kwambiri.’
yet if they shall rethink themselves in the land where they are carried captive, and turn again, and make supplication to thee in the land of their captivity, saying, We have sinned, we have done perversely, and have dealt wickedly,
38 Ndipo ngati atembenukira kwa inu ndi mtima ndi moyo wawo wonse mʼdziko lawo la ukapolo kumene anatengedwako ndi kupemphera moyangʼana dziko limene inu munalipereka kwa makolo awo, moyangʼana Nyumba yanu imene ndakumangirani;
if they return to thee with all their heart and with all their soul in the land of their captivity where they have carried them captive, and pray toward their land, which thou gave to their fathers, and the city which thou have chosen, and toward the house which I have built for thy name,
39 pamenepo imvani kumwamba, malo anu okhala, pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwapulumutse. Ndipo mukhululukire anthu anu, amene akuchimwirani.
then hear thou from heaven, even from thy dwelling-place, their prayer and their supplications, and maintain their case, and forgive thy people who have sinned against thee.
40 “Tsono Inu Mulungu wanga, tsekulani maso anu ndi makutu anu kuti mumve mapemphero ochitikira pa malo ano.
Now, O my God, let, I beseech thee, thine eyes be open, and let thine ears be attendant to the prayer that is made in this place.
41 “Tsopano dzukani Inu Yehova Mulungu, ndipo bwerani ku malo anu ampumulo,
Now therefore arise, O Jehovah God, into thy resting-place, thou, and the ark of thy strength. Let thy priests, O Jehovah God, be clothed with salvation, and let thy sanctified rejoice in goodness.
42 Inu Yehova Mulungu musamukane wodzozedwa wanu.
O Jehovah God, do not turn away the face of thine anointed. Remember thy loving kindnesses to David thy servant.

< 2 Mbiri 6 >