< 2 Mbiri 23 >

1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
And in the seventh year Jehoiada strengthened himself, and took the captains of hundreds, Azariah the son of Jeroham, and Ishmael the son of Jehohanan, and Azariah the son of Obed, and Maaseiah the son of Adaiah, and Elishaphat the son of Zichri, into covenant with him.
2 Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
And they went about in Judah, and gathered the Levites out of all the cities of Judah, and the heads of fathers of Israel, and they came to Jerusalem.
3 msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
And all the assembly made a covenant with the king in the house of God. And he said to them, Behold, the king's son shall reign, as Jehovah has spoken concerning the sons of David.
4 Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
This is the thing that ye shall do: A third part of you who come in on the sabbath, of the priests and of the Levites, shall be porters of the thresholds,
5 ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
and a third part shall be at the king's house, and a third part at the gate of the foundation. And all the people shall be in the courts of the house of Jehovah.
6 Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
But let none come into the house of Jehovah except the priests, and those who minister of the Levites. They shall come in for they are holy, but all the people shall keep the charge of Jehovah.
7 Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
And the Levites shall encompass the king round about, every man with his weapons in his hand. And whoever comes into the house, let him be slain. And be ye with the king when he comes in, and when he goes out.
8 Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
So the Levites and all Judah did according to all that Jehoiada the priest commanded. And they took every man his men, those who were to come in on the sabbath, with those who were to go out on the sabbath. For Jehoiada the priest did not dismiss the divisions.
9 Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
And Jehoiada the priest delivered to the captains of hundreds the spears, and bucklers, and shields, that had been king David's, which were in the house of God.
10 Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
And he set all the people, every man with his weapon in his hand, from the right side of the house to the left side of the house, along by the altar and the house, by the king round about.
11 Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
Then they brought out the king's son, and put the crown upon him, and gave him the testimony, and made him king. And Jehoiada and his sons anointed him. And they said, Live, O king.
12 Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
And when Athaliah heard the noise of the people running and praising the king, she came to the people into the house of Jehovah.
13 Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
And she looked, and, behold, the king stood by his pillar at the entrance, and the captains and the trumpets by the king. And all the people of the land rejoiced, and blew trumpets. The singers also played on instruments of music, and led the singing of praise. Then Athaliah tore her clothes, and said, Treason! treason!
14 Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
And Jehoiada the priest brought out the captains of hundreds who were set over the army, and said to them, Have her forth between the ranks. And whoever follows her, let him be slain with the sword, for the priest said, Do not slay her in the house of Jehovah.
15 choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
So they made way for her. And she went to the entrance of the horse gate to the king's house, and they killed her there.
16 Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
And Jehoiada made a covenant between himself, and all the people, and the king, that they should be Jehovah's people.
17 Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
And all the people went to the house of Baal, and broke it down, and broke his altars and his images in pieces, and killed Mattan the priest of Baal before the altars.
18 Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
And Jehoiada appointed the officers of the house of Jehovah under the hand of the priests the Levites, whom David had distributed in the house of Jehovah, to offer the burnt offerings of Jehovah, as it is written in the law of Moses, with rejoicing and with singing, according to the order of David.
19 Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
And he set the porters at the gates of the house of Jehovah that no man who was unclean in anything should enter in.
20 Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
And he took the captains of hundreds, and the mighty men, and the governors of the people, and all the people of the land, and brought down the king from the house of Jehovah. And they came through the upper gate to the king's house, and set the king upon the throne of the kingdom.
21 ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.
So all the people of the land rejoiced, and the city was quiet. And they had slain Athaliah with the sword.

< 2 Mbiri 23 >