< 2 Mbiri 20 >

1 Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
And it came to pass after this, that the sons of Moab, and the sons of Ammon, and with them some of the Minaeans, came against Jehoshaphat to battle.
2 Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
Then there came some who told Jehoshaphat, saying, There comes a great multitude against thee from beyond the sea from Syria. And, behold, they are in Hazazon-tamar (the same is En-gedi).
3 Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
And Jehoshaphat was afraid, and set himself to seek for Jehovah. And he proclaimed a fast throughout all Judah.
4 Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
And Judah gathered themselves together, to seek help from Jehovah, even out of all the cities of Judah they came to seek Jehovah.
5 Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
And Jehoshaphat stood in the assembly of Judah and Jerusalem in the house of Jehovah before the new court.
6 ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
And he said, O Jehovah, the God of our fathers, are thou not God in heaven? And are thou not ruler over all the kingdoms of the nations? And in thy hand is power and might, so that none is able to withstand thee.
7 Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
Did thou not, O our God, drive out the inhabitants of this land before thy people Israel, and give it to the seed of Abraham thy friend forever?
8 Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
And they dwelt therein, and have built for thee a sanctuary in it for thy name, saying,
9 ‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
If evil comes upon us, the sword, judgment, or pestilence, or famine, we will stand before this house, and before thee, (for thy name is in this house, ) and cry out to thee in our affliction, and thou will hear and save.
10 “Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
And now, behold, the sons of Ammon and Moab and mount Seir (whom thou would not let Israel invade when they came out of the land of Egypt, but they turned aside from them, and did not destroy them),
11 Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
behold, how they reward us, to come to cast us out of thy possession, which thou have given us to inherit.
12 Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
O our God, will thou not judge them? For we have no might against this great company that comes against us. Neither do we know what to do, but our eyes are upon thee.
13 Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
And all Judah stood before Jehovah, with their little ones, their wives, and their sons.
14 Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
Then upon Jahaziel the son of Zechariah, the son of Benaiah, the son of Jeiel, the son of Mattaniah, the Levite, of the sons of Asaph, came the Spirit of Jehovah in the midst of the assembly.
15 Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
And he said, Hearken ye, all Judah, and ye inhabitants of Jerusalem, and thou king Jehoshaphat. Thus says Jehovah to you, Fear ye not, neither be dismayed because of this great multitude. For the battle is not yours, but God's.
16 Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
Tomorrow go ye down against them. Behold, they come up by the ascent of Ziz. And ye shall find them at the end of the valley, before the wilderness of Jeruel.
17 Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
Ye shall not need to fight in this battle. Set yourselves, stand ye still, and see the salvation of Jehovah with you, O Judah and Jerusalem. Fear not, nor be dismayed. Tomorrow go out against them, for Jehovah is with you.
18 Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
And Jehoshaphat bowed his head with his face to the ground. And all Judah and the inhabitants of Jerusalem fell down before Jehovah, worshiping Jehovah.
19 Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
And the Levites, of the sons of the Kohathites and of the sons of the Korahites, stood up to praise Jehovah, the God of Israel, with an exceedingly loud voice.
20 Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
And they rose early in the morning, and went forth into the wilderness of Tekoa. And as they went forth, Jehoshaphat stood and said, Hear me, O Judah, and ye inhabitants of Jerusalem. Believe in Jehovah your God, so shall ye be established. Believe his prophets, so shall ye prosper.
21 Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
And when he had taken counsel with the people, he appointed those who should sing to Jehovah, and give praise in holy array, as they went out before the army, and say, Give thanks to Jehovah. For his loving kindness is forever.
22 Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
And when they began to sing and to praise, Jehovah set an ambushment against the sons of Ammon, Moab, and mount Seir who came against Judah, and they were smitten.
23 Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
For the sons of Ammon and Moab stood up against the inhabitants of mount Seir, to slay and destroy them utterly. And when they had made an end of the inhabitants of Seir, every one helped to destroy another of themselves.
24 Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
And when Judah came to the watch-tower of the wilderness, they looked upon the multitude. And, behold, they were dead bodies fallen to the earth, and there were none who escaped.
25 Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
And when Jehoshaphat and his people came to take the spoil of them, they found among them in abundance both riches and dead bodies, and precious jewels, which they stripped off for themselves, more than they could carry away. And they were three days in taking the spoil, it was so much.
26 Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
And on the fourth day they assembled themselves in the valley of Beracah, for there they blessed Jehovah. Therefore the name of that place was called The valley of Beracah to this day.
27 Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
Then they returned, every man of Judah and Jerusalem, and Jehoshaphat in the forefront of them, to go again to Jerusalem with joy. For Jehovah had made them to rejoice over their enemies.
28 Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
And they came to Jerusalem with psalteries and harps and trumpets to the house of Jehovah.
29 Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
And the fear of God was on all the kingdoms of the countries, when they heard that Jehovah fought against the enemies of Israel.
30 Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
So the realm of Jehoshaphat was quiet. For his God gave him rest round about.
31 Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
And Jehoshaphat reigned over Judah. He was thirty-five years old when he began to reign. And he reigned twenty-five years in Jerusalem. And his mother's name was Azubah the daughter of Shilhi.
32 Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
And he walked in the way of Asa his father, and did not turn aside from it, doing that which was right in the eyes of Jehovah.
33 Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
However the high places were not taken away. Neither as yet had the people set their hearts to the God of their fathers.
34 Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Now the rest of the acts of Jehoshaphat, first and last, behold, they are written in the history of Jehu the son of Hanani, which is inserted in the book of the kings of Israel.
35 Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
And after this Jehoshaphat king of Judah joined himself with Ahaziah king of Israel. The same did very wickedly.
36 Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
And he joined himself with him to make ships to go to Tarshish. And they made the ships in Ezion-geber.
37 Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.
Then Eliezer the son of Dodavahu of Mareshah prophesied against Jehoshaphat, saying, Because thou have joined thyself with Ahaziah, Jehovah has destroyed thy works. And the ships were broken, so that they were not able to go to Tarshish.

< 2 Mbiri 20 >