< 2 Mbiri 19 >

1 Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
And Jehoshaphat the king of Judah returned to his house in peace to Jerusalem.
2 mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
And Jehu the son of Hanani the seer went out to meet him, and said to king Jehoshaphat, Should thou help the wicked, and love those who hate Jehovah? For this thing wrath is upon thee from before Jehovah.
3 Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
Nevertheless there are good things found in thee, in that thou have put away the Asheroth out of the land, and have set thy heart to seek God.
4 Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
And Jehoshaphat dwelt at Jerusalem. And he went out again among the people from Beersheba to the hill-country of Ephraim, and brought them back to Jehovah, the God of their fathers.
5 Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
And he set judges in the land throughout all the fortified cities of Judah, city by city,
6 Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
and said to the judges, Consider what ye do. For ye judge not for man, but for Jehovah, and he is with you in the judgment.
7 Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
Now therefore let the fear of Jehovah be upon you. Take heed and do it. For there is no iniquity with Jehovah our God, nor respect of persons, nor taking of bribes.
8 Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
Moreover in Jerusalem Jehoshaphat set from the Levites and the priests, and from the heads of the fathers of Israel for the judgment of Jehovah, and for controversies. And they returned to Jerusalem.
9 Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
And he charged them, saying, Thus ye shall do in the fear of Jehovah, faithfully, and with a perfect heart.
10 Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
And whenever any controversy shall come to you from your brothers who dwell in their cities, between blood and blood, between law and commandment, statutes and ordinances, ye shall warn them, that they not be guilty towards Jehovah, and so wrath come upon you and upon your brothers. Do this, and ye shall not be guilty.
11 “Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”
And, behold, Amariah the chief priest is over you in all matters of Jehovah, and Zebadiah the son of Ishmael, the ruler of the house of Judah, in all the king's matters. The Levites shall also be officers before you. Deal courageously, and Jehovah be with the good.

< 2 Mbiri 19 >