< 1 Samueli 24 >

1 Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
And it came to pass, when Saul was returned from following the Philistines, that it was told him, saying, Behold, David is in the wilderness of En-gedi.
2 Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
Then Saul took three thousand chosen men out of all Israel, and went to seek David and his men upon the rocks of the wild goats.
3 Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
And he came to the sheepcotes by the way, where was a cave, and Saul went in to cover his feet. Now David and his men were abiding in the innermost parts of the cave.
4 Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
And the men of David said to him, Behold, the day of which Jehovah said to thee, Behold, I will deliver thine enemy into thy hand, and thou shall do to him as it shall seem good to thee. Then David arose, and cut off the skirt of Saul's robe secretly.
5 Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
And it came to pass afterward, that David's heart smote him, because he had cut off Saul's skirt.
6 Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
And he said to his men, Jehovah forbid that I should do this thing to my lord, Jehovah's anointed, to put forth my hand against him, since he is Jehovah's anointed.
7 Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
So David restrained his men with these words, and did not allow them to rise against Saul. And Saul rose up out of the cave, and went on his way.
8 Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
David also arose afterward, and went out of the cave, and cried after Saul, saying, My lord the king. And when Saul looked behind him, David bowed with his face to the earth, and did obeisance.
9 Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
And David said to Saul, Why do thou hearken to men's words, saying, Behold, David seeks thy hurt?
10 Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
Behold, this day thine eyes have seen how that Jehovah had delivered thee today into my hand in the cave. And some bade me kill thee, but I spared thee. And I said, I will not put forth my hand against my lord, for he is Jehovah's anointed.
11 Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
Moreover, my father, see, yea, see the skirt of thy robe in my hand, for in that I cut off the skirt of thy robe, and killed thee not. Know thou and see that there is neither evil nor transgression in my hand, and I have not sinned against thee, though thou hunt after my life to take it.
12 Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
Jehovah judge between me and thee, and Jehovah avenge me of thee, but my hand shall not be upon thee.
13 Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
As says the proverb of the ancients, Out of the wicked comes forth wickedness, but my hand shall not be upon thee.
14 “Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
After whom is the king of Israel come out? After whom do thou pursue? After a dead dog, after a flea.
15 Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
Jehovah therefore be judge, and give sentence between me and thee, and see, and plead my cause, and deliver me out of thy hand.
16 Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
And it came to pass, when David had made an end of speaking these words to Saul, that Saul said, Is this thy voice, my son David? And Saul lifted up his voice, and wept.
17 Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
And he said to David, Thou are more righteous than I, for thou have rendered to me good, whereas I have rendered to thee evil.
18 Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
And thou have declared this day how that thou have dealt well with me, inasmuch as when Jehovah had delivered me up into thy hand, thou killed me not.
19 Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
For if a man finds his enemy, will he let him go away well? Therefore Jehovah reward thee good for that which thou have done to me this day.
20 Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
And now, behold, I know that thou shall surely be king, and that the kingdom of Israel shall be established in thy hand.
21 Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
Swear now therefore to me by Jehovah, that thou will not cut off my seed after me, and that thou will not destroy my name out of my father's house.
22 Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.
And David swore to Saul. And Saul went home, but David and his men got up to the stronghold.

< 1 Samueli 24 >