< 1 Samueli 23 >

1 Davide atawuzidwa kuti “Onani, Afilisti akuthira nkhondo mzinda wa Keila ndi kulanda zokolola zawo za mʼnkhokwe,”
And they told David, saying, Behold, the Philistines are fighting against Keilah, and are robbing the threshing-floors.
2 anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ndikamenyane nawo Afilistiwa?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, kamenyane nawo Afilisti ndi kupulumutsa mzinda wa Keila.”
Therefore David inquired of Jehovah, saying, Shall I go and smite these Philistines? And Jehovah said to David, Go, and smite the Philistines, and save Keilah.
3 Koma anthu amene anali ndi Davide anati, “Ngati tikuchita mantha ku Yuda konkuno, nanji kupita ku Keila kukamenyana ndi ankhondo a Afilisti!”
And David's men said to him, Behold, we are afraid here in Judah. How much more then if we go to Keilah against the armies of the Philistines?
4 Davide anafunsanso Yehova, ndipo Yehova anamuyankha kuti, “Pita ku Keila pakuti ndapereka Afilisti mʼdzanja lako.”
Then David inquired of Jehovah yet again. And Jehovah answered him, and said, Arise, go down to Keilah, for I will deliver the Philistines into thy hand.
5 Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Keila kukamenyana ndi Afilisti. Anapha Afilisti ambiri ndi kutenga ziweto zawo. Choncho anapulumutsa anthu a ku Keila.
And David and his men went to Keilah, and fought with the Philistines, and brought away their cattle, and killed them with a great slaughter. So David saved the inhabitants of Keilah.
6 (Pamene Abiatara mwana wa Ahimeleki anathawira kwa Davide anabwera ndi efodi mʼmanja mwake).
And it came to pass, when Abiathar the son of Ahimelech fled to David to Keilah, that he came down with an ephod in his hand.
7 Sauli atamva kuti Davide wapita ku Keila anati, “Mulungu wamupereka kwa ine, pakuti Davide wadzitsekera yekha mʼndende polowa mu mzinda umene uli ndi zipata ndi zotsekera zake.”
And it was told Saul that David came to Keilah. And Saul said, God has delivered him into my hand, for he is shut in by entering into a town that has gates and bars.
8 Choncho Sauli anasonkhanitsa ankhondo ake nawatuma ku Keila kuti akamuzungulire Davide ndi anthu ake.
And Saul summoned all the people to war, to go down to Keilah, to besiege David and his men.
9 Davide atadziwa kuti Sauli akufuna kumuchita chiwembu, anawuza Abiatara wansembe uja kuti, “Bwera nayo efodiyo.”
And David knew that Saul was devising mischief against him, and he said to Abiathar the priest, Bring here the ephod.
10 Tsono Davide anayankhula ndi Yehova kuti, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, ine mtumiki wanu ndamva ndithu kuti Sauli akufuna kubwera ku Keila ndi kudzawononga mzindawu chifukwa cha ine.
Then said David, O Jehovah, the God of Israel, thy servant has surely heard that Saul seeks to come to Keilah to destroy the city for my sake.
11 Kodi anthu a Keila adzandipereka mʼmanja mwa Sauli? Kodi Sauli abweradi monga ndamvera ine mtumiki wanu? Inu Yehova Mulungu wa Israeli, chonde, ndiwuzeni ine mtumiki wanu.” Ndipo Yehova anati, “Sauli abweradi.”
Will the men of Keilah deliver me up into his hand? Will Saul come down as thy servant has heard? O Jehovah, the God of Israel, I beseech thee, tell thy servant. And Jehovah said, He will come down.
12 Davide anafunsanso, “Kodi anthu a ku Keila adzapereka ine ndi anthu angawa kwa Sauli?” Ndipo Yehova anayankha, “Iwo adzakuperekanidi.”
Then David said, Will the men of Keilah deliver up me and my men into the hand of Saul? And Jehovah said, They will deliver thee up.
13 Choncho Davide ndi anthu ake, omwe analipo 600, anachoka ku Keila namayenda mothawathawa. Sauli atamva kuti Davide wathawa ku Keila, sanatumizeko ankhondo ake aja.
Then David and his men, who were about six hundred, arose and departed out of Keilah, and went wherever they could go. And it was told Saul that David was escaped from Keilah, and he ceased to go forth.
14 Davide ankakhala mʼmapanga mʼdziko lamapiri ku chipululu cha Zifi. Sauli ankamufufuza tsiku ndi tsiku, koma Mulungu sanapereke Davide mʼmanja mwake.
And David abode in the wilderness in the strongholds, and remained in the hill-country in the wilderness of Ziph. And Saul sought him every day, but God did not deliver him into his hand.
15 Davide anaona kuti Sauli akufunafuna kuti amuphe. Nthawiyi nʼkuti Davide ali mʼchipululu cha Zifi ku Horesi.
And David saw that Saul came out to seek his life, and David was in the wilderness of Ziph in the forest.
16 Ndipo Yonatani mwana wa Sauli anapita kwa Davide ku Horesi ndipo anamulimbitsa mtima pomuwuza kuti Yehova ali naye.
And Jonathan, Saul's son, arose, and went to David into the forest, and strengthened his hand in God.
17 Iye anamuwuza kuti, “Usaope, abambo anga sadzakupha. Iwe udzakhala mfumu ya Israeli ndipo ine ndidzakhala wachiwiri wako. Ngakhale abambo anga Sauli akudziwa zimenezi.”
And he said to him, Fear not, for the hand of Saul my father shall not find thee. And thou shall be king over Israel, and I shall be next to thee. And that, Saul my father also knows.
18 Awiriwa anachita pangano pamaso pa Yehova. Ndipo Yonatani anabwerera kwawo, koma Davide anakhalabe ku Horesi.
And those two made a covenant before Jehovah. And David abode in the forest, and Jonathan went to his house.
19 Anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ku Gibeya ndipo anamuwuza kuti, “Davide akubisala kwathu, mʼmapanga a ku Horesi, mʼphiri la Hakila, kummwera kwa Yesimoni.
Then the Ziphites came up to Saul to Gibeah, saying, Does not David hide himself with us in the strongholds in the forest, in the hill of Hachilah, which is on the south of the desert?
20 Tsopano inu, mubwere nthawi iliyonse imene mukufuna, ndipo ife tidzamupereka kwa mfumu.”
Now therefore, O king, come down, according to all the desire of thy soul to come down, and our part shall be to deliver him up into the king's hand.
21 Sauli anayankha kuti, “Yehova akudalitseni pakuti mwandichitira chifundo.
And Saul said, Blessed be ye of Jehovah, for ye have had compassion on me.
22 Pitani mukatsimikizire. Mukaone kumene amakhala ndiponso mupeze munthu amene wamuona. Anthu amandiwuza kuti ndi wochenjera kwambiri.
Go, I pray you, make yet more sure, and know and see his place where his haunt is, and who has seen him there, for it is told me that he deals very shrewdly.
23 Kafufuzeni ndithu malo onse kumene amabisalako, ndipo mubwerenso kuno mudzandiwuze chenicheni. Pambuyo pake ine ndidzapita nanu. Ngatidi ali mʼderalo ndidzamusaka pakati pa mabanja onse a Yuda.”
See therefore, and take knowledge of all the lurking-places where he hides himself, and come ye again to me of a certainty. And I will go with you, and it shall come to pass, if he is in the land, that I will search him out among all the thousands of Judah.
24 Kotero iwo ananyamuka ndi kupita ku Zifi, koma Sauli asananyamuke. Nthawi imeneyi Davide ndi anthu ake anali ku chipululu cha Maoni, ku Araba kummwera kwa Yesimoni.
And they arose, and went to Ziph before Saul, but David and his men were in the wilderness of Maon, in the Arabah on the south of the desert.
25 Sauli ndi anthu ake anapita kukamufufuza Davide. Koma Davide atamva izi anathawa ndi kukabisala ku thanthwe la chipululu cha Maoni. Sauli atamva kuti Davide anathawira ku Maoni anamutsatira ku chipululu komweko.
And Saul and his men went to seek him. And they told David. Therefore he came down to the rock, and abode in the wilderness of Maon. And when Saul heard that, he pursued after David in the wilderness of Maon.
26 Sauli amayenda mbali ina ya phirilo, ndipo Davide ndi anthu ake nawonso anali mbali ina ya phirilo. Koma Davide ndi anthu ake anafulumira kumuthawa Sauli pamene Sauliyo ndi anthu ake ali pafupi kuwagwira.
And Saul went on this side of the mountain, and David and his men on that side of the mountain. And David made haste to get away for fear of Saul. For Saul and his men encompassed David and his men round about to take them.
27 Nthawi yomweyo munthu wina wamthenga anabwera kudzamuwuza Sauli kuti, “Bwerani msanga! Afilisti akuthira nkhondo dzikoli.”
But there came a messenger to Saul, saying, Hasten thee, and come, for the Philistines have made a raid upon the land.
28 Choncho Sauli analeka kuthamangitsa Davide ndipo anapita kukamenyana ndi Afilisti. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Mwala wa Malekano.
So Saul returned from pursuing after David, and went against the Philistines. Therefore they called that place Sela-hammahlekoth.
29 Ndipo Davide anachoka kumeneko ndi kukakhala ku mapanga a ku Eni Gedi.
And David went up from there, and dwelt in the strongholds of En-gedi.

< 1 Samueli 23 >