< 1 Mafumu 14 >

1 Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
At that time Abijah the son of Jeroboam fell sick.
2 ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
And Jeroboam said to his wife, Arise, I pray thee, and disguise thyself that thou not be known to be the wife of Jeroboam, and get thee to Shiloh. Behold, there is Ahijah the prophet who spoke concerning me that I should be king over this people.
3 Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
And take with thee ten loaves, and cakes, and a cruse of honey, and go to him. He will tell thee what shall become of the child.
4 Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
And Jeroboam's wife did so, and arose, and went to Shiloh, and came to the house of Ahijah. Now Ahijah could not see, for his eyes were set because of his age.
5 Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
And Jehovah said to Ahijah, Behold, the wife of Jeroboam comes to inquire of thee concerning her son, for he is sick. Thus and thus thou shall say to her, for it will be, when she comes in, that she will feign herself to be another woman.
6 Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
And it was so, when Ahijah heard the sound of her feet, as she came in at the door, that he said, Come in, thou wife of Jeroboam. Why feign thou thyself to be another? For I am sent to thee with heavy news.
7 Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
Go, tell Jeroboam, Thus says Jehovah, the God of Israel: Forasmuch as I exalted thee from among the people, and made thee prince over my people Israel,
8 Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
and tore the kingdom away from the house of David, and gave it thee, and yet thou have not been as my servant David, who kept my commandments, and who followed me with all his heart to do only that which was right in my eyes,
9 Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
but have done evil above all who were before thee, and have gone and made thee other gods, and molten images to provoke me to anger, and have cast me behind thy back,
10 “‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
therefore, behold, I will bring evil upon the house of Jeroboam, and will cut off from Jeroboam every man-child, he who is shut up and he who is left at large in Israel, and will utterly sweep away the house of Jeroboam as a man sweeps away dung, till it be all gone.
11 Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
He who dies of Jeroboam in the city shall the dogs eat, and he who dies in the field shall the birds of the heavens eat, for Jehovah has spoken it.
12 “Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
Arise thou therefore, get thee to thy house. When thy feet enter into the city, the child shall die.
13 Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
And all Israel shall mourn for him, and bury him, for he only of Jeroboam shall come to the grave, because in him there is found some good thing toward Jehovah, the God of Israel, in the house of Jeroboam.
14 “Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
Moreover Jehovah will raise up a king for him over Israel who shall cut off the house of Jeroboam that day. But what? Even now.
15 Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
For Jehovah will smite Israel as a reed is shaken in the water. And he will root up Israel out of this good land which he gave to their fathers, and will scatter them beyond the River because they have made their Asherim, provoking Jehovah to anger.
16 Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
And he will give Israel up because of the sins of Jeroboam, which he has sinned, and with which he has made Israel to sin.
17 Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
And Jeroboam's wife arose, and departed, and came to Tirzah. As she came to the threshold of the house, the child died.
18 Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
And all Israel buried him, and mourned for him, according to the word of Jehovah, which he spoke by his servant Ahijah the prophet.
19 Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
And the rest of the acts of Jeroboam, how he warred, and how he reigned, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
20 Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And the days which Jeroboam reigned were twenty-two years, and he slept with his fathers. And Nadab his son reigned in his stead.
21 Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
And Rehoboam the son of Solomon reigned in Judah. Rehoboam was forty-one years old when he began to reign, and he reigned seventeen years in Jerusalem, the city which Jehovah had chosen out of all the tribes of Israel to put his name there. And his mother's name was Naamah the Ammonitess.
22 Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
And Judah did that which was evil in the sight of Jehovah, and they provoked him to jealousy with their sins which they committed, above all that their fathers had done.
23 Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
For they also built for them high places, and pillars, and Asherim, on every high hill, and under every green tree.
24 Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
And there were also sodomites in the land. They did according to all the abominations of the nations which Jehovah drove out before the sons of Israel.
25 Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
And it came to pass in the fifth year of king Rehoboam, that Shishak king of Egypt came up against Jerusalem.
26 Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
And he took away the treasures of the house of Jehovah, and the treasures of the king's house. He even took away all. And he took away all the shields of gold which Solomon had made.
27 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
And king Rehoboam made in their stead shields of brass, and committed them to the hands of the captains of the guard who kept the door of the king's house.
28 Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
And it was so, that, as often as the king went into the house of Jehovah, the guard bore them, and brought them back into the guard-chamber.
29 Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Now the rest of the acts of Rehoboam, and all that he did, are they not written in the book of the chronicles of the kings of Judah?
30 Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
And there was war between Rehoboam and Jeroboam continually.
31 Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
And Rehoboam slept with his fathers, and was buried with his fathers in the city of David. And his mother's name was Naamah the Ammonitess. And Abijah his son reigned in his stead.

< 1 Mafumu 14 >