< 1 Mafumu 13 >

1 Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
And, behold, there came a man of God out of Judah by the word of Jehovah to Bethel. And Jeroboam was standing by the altar to burn incense.
2 Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
And he cried against the altar by the word of Jehovah, and said, O altar, altar, thus says Jehovah: Behold, a son shall be born to the house of David, Josiah by name. And upon thee shall he sacrifice the priests of the high places that burn incense upon thee, and men's bones they shall burn upon thee.
3 Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
And he gave a sign the same day, saying, This is the sign which Jehovah has spoken: Behold, the altar shall be torn, and the ashes that are upon it shall be poured out.
4 Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
And it came to pass, when the king heard the saying of the man of God, which he cried against the altar in Bethel, that Jeroboam put forth his hand from the altar, saying, Lay hold on him. And his hand, which he put forth against him, dried up, so that he could not draw it back again to him.
5 Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
The altar also was torn, and the ashes poured out from the altar, according to the sign which the man of God had given by the word of Jehovah.
6 Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
And the king answered and said to the man of God, Entreat now the favor of Jehovah thy God, and pray for me that my hand may be restored to me again. And the man of God entreated Jehovah, and the king's hand was restored to him again, and became as it was before.
7 Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
And the king said to the man of God, Come home with me, and refresh thyself, and I will give thee a reward.
8 Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
And the man of God said to the king, If thou will give me half thy house, I will not go in with thee, neither will I eat bread nor drink water in this place;
9 Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
for so it was charged me by the word of Jehovah, saying, Thou shall eat no bread, nor drink water, neither return by the way that thou came.
10 Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
So he went another way, and returned not by the way that he came to Bethel.
11 Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
Now there dwelt an old prophet in Bethel. And one of his sons came and told him all the works that the man of God had done that day in Bethel. The words which he had spoken to the king, they also told them to their father.
12 Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
And their father said to them, What way did he go? Now his sons had seen what way the man of God went, who came from Judah.
13 Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
And he said to his sons, Saddle the donkey for me. So they saddled him the donkey, and he rode on it.
14 ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
And he went after the man of God, and found him sitting under an oak. And he said to him, Are thou the man of God who came from Judah? And he said, I am.
15 Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
Then he said to him, Come home with me, and eat bread.
16 Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
And he said, I may not return with thee, nor go in with thee. Neither will I eat bread nor drink water with thee in this place;
17 Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
for it was said to me by the word of Jehovah, Thou shall eat no bread nor drink water there, nor turn again to go by the way that thou came.
18 Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
And he said to him, I also am a prophet as thou are. And an agent spoke to me by the word of Jehovah, saying, Bring him back with thee into thy house that he may eat bread and drink water. But he lied to him.
19 Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
So he went back with him, and ate bread in his house, and drank water.
20 Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
And it came to pass, as they sat at the table, that the word of Jehovah came to the prophet who brought him back.
21 Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
And he cried out to the man of God who came from Judah, saying, Thus says Jehovah, Forasmuch as thou have been disobedient to the mouth of Jehovah, and have not kept the commandment which Jehovah thy God commanded thee,
22 Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
but came back, and have eaten bread and drunk water in the place of which he said to thee, Eat no bread, and drink no water, thy body shall not come to the sepulcher of thy fathers.
23 Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
And it came to pass, after he had eaten bread, and after he had drunk, that he saddled the donkey for him, namely, for the prophet whom he had brought back.
24 Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
And when he was gone, a lion met him by the way, and killed him. And his body was cast in the way, and the donkey stood by it. The lion also stood by the body.
25 Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
And, behold, men passed by, and saw the body cast in the way, and the lion standing by the body. And they came and told it in the city where the old prophet dwelt.
26 Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
And when the prophet who brought him back from the way heard of it, he said, It is the man of God who was disobedient to the mouth of Jehovah. Therefore Jehovah has delivered him to the lion, which has torn him, and slain him, according to the word of Jehovah which he spoke to him.
27 Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
And he spoke to his sons, saying, Saddle the donkey for me. And they saddled it.
28 Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
And he went and found his body cast in the way, and the donkey and the lion standing by the body. The lion had not eaten the body, nor torn the donkey.
29 Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
And the prophet took up the body of the man of God, and laid it upon the donkey, and brought it back. And he came to the city of the old prophet, to mourn, and to bury him.
30 Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
And he laid his body in his own grave. And they mourned over him, saying, Alas, my brother!
31 Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
And it came to pass, after he had buried him, that he spoke to his sons, saying, When I am dead, then bury me in the sepulcher in which the man of God is buried. Lay my bones beside his bones.
32 Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
For the saying which he cried by the word of Jehovah against the altar in Bethel, and against all the houses of the high places which are in the cities of Samaria, shall surely come to pass.
33 Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
After this thing Jeroboam did not return from his evil way, but again made from among all the people priests of the high places. Whoever would, he consecrated him, that there might be priests of the high places.
34 Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.
And this thing became sin to the house of Jeroboam, even to cut it off, and to destroy it from off the face of the earth.

< 1 Mafumu 13 >