< 1 Mbiri 24 >

1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Men Aarons barnas ordning var denna: Aarons barn voro Nadab, Abihu, Eleazar och Ithamar.
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
Men Nadab och Abihu blefvo döde inför deras fader, och hade inga barn; och Eleazar och Ithamar vordo Prester.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
Och David skickade dem alltså, Zadok af Eleazars barn, och Ahimelech af Ithamars barn, efter deras tal och ämbete.
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
Och vordo Eleazars barn flere funne till yppersta starka män än Ithamars barn. Och han skickade dem alltså; nämliga sexton utaf Eleazars barn, till öfverstar ibland deras fäders hus; och åtta af Ithamars barn ibland deras fäders hus.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
Och han skifte dem efter lott, derföre, att både af Eleazars och Ithamars barn voro öfverstar i helgedomenom, och öfverstar för Gud.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
Och skrifvaren Semaja, Nethaneels son, utaf Leviterna, beskref dem för Konungenom, och för öfverstarna, och för Zadok Prestenom, och för Ahimelech, AbJathars son, och för öfversta fäderna ibland Presterna och Leviterna; nämliga ett fadershus för Eleazar, och det andra för Ithamar.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
Och förste lotten föll uppå Jojarib, den andre uppå Jedaja;
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
Den tredje på Harim, den fjerde på Seorim;
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
Den femte på Malchija, den sjette på Mijamin;
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
Den sjunde på Hakkoz, den åttonde på Abia;
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
Den nionde på Jesua, den tionde på Sechania;
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
Den ellofte på EljaSib, den tolfte på Jakim;
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
Den trettonde på Huppa, den fjortonde på Jesebeab;
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
Den femtonde på Bilga, den sextonde på Immer;
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
Den sjuttonde på Hesir, den adertonde på Happizez;
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
Den nittonde på Petahja, den tjugonde på Jeheskel;
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
Den förste och tjugonde på Jachin, den andre och tjugonde på Gamul;
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
Den tredje och tjugonde på Delaja, den fjerde och tjugonde på Mahasia.
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
Detta är ordningen efter deras ämbeten, till att gå i Herrans hus efter deras sätt, under deras fader Aaron, såsom Herren Israels Gud dem budit hade.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
Men utaf de andra Levi barn, af Amrams barn var Subael. Af Subaels barn var Jehdeja.
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
Af Rehabia barn var den förste Jissija.
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
Men af de Jizeariter var Selomoth. Af Selomoths barn var Jahath.
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
( Hebrons ) barn voro: Jeria den förste, Amaria den andre, Jahasiel den tredje, Jekameam den fjerde.
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
Ussiels barn voro: Micha. Utaf Micha barn var Samir.
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
Micha broder var Jissija. Utaf Jissija barn var Zacharia.
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
Merari barn voro: Maheli och Musi; hans son var Jaasia.
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
Merari barn, af Jaasia, hans son, voro: Soham, Saccur och Ibri.
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
Men Maheli hade Eleazar, och Eleazar hade inga söner.
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
Af Kis: Kis barn voro: Jerahmeel.
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
Musi barn voro: Maheli, Eder och Jerimoth. Detta äro de Leviters barn, i deras faders hus.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
Och man kastade också för dem lott, bredovid deras bröder Aarons barn, inför Konung David och Zadok, och Ahimelech, och inför de öfversta fäderna af Prestomen och Levitomen, dem minsta brodrenom så väl som dem öfversta af fäderna.

< 1 Mbiri 24 >