< 1 Mbiri 18 >

1 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.
And after this it came to pass, that David smote the Philistines, and subdued them, and took Gath and its towns out of the hand of the Philistines.
2 Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.
And he smote Moab, and the Moabites became servants to David, and brought tribute.
3 Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
And David smote Hadarezer king of Zobah to Hamath, as he went to establish his dominion by the river Euphrates.
4 Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
And David took from him a thousand chariots, and seven thousand horsemen, and twenty thousand footmen. And David hocked all the chariot horses, but reserved from them for a hundred chariots.
5 Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
And when the Syrians of Damascus came to aid Hadarezer king of Zobah, David smote of the Syrians twenty-two thousand men.
6 Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
Then David put garrisons in Syria of Damascus. And the Syrians became servants to David, and brought tribute. And Jehovah gave victory to David wherever he went.
7 Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
And David took the shields of gold that were on the servants of Hadarezer, and brought them to Jerusalem.
8 Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.
And from Tibhath and from Cun, cities of Hadarezer, David took very much brass, with which Solomon made the brazen sea, and the pillars, and the vessels of brass.
9 Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba,
And when Tou king of Hamath heard that David had smitten all the army of Hadarezer king of Zobah,
10 anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.
he sent Hadoram his son to king David, to salute him, and to bless him, because he had fought against Hadarezer and smitten him (for Hadarezer had wars with Tou), and he had with him all manner of vessels of gold and silver and brass.
11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.
These also king David dedicated to Jehovah, with the silver and the gold that he carried away from all the nations: from Edom, and from Moab, and from the sons of Ammon, and from the Philistines, and from Amalek.
12 Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
Moreover Abishai the son of Zeruiah smote eighteen thousand of the Edomites in the Valley of Salt.
13 Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
And he put garrisons in Edom, and all the Edomites became servants to David. And Jehovah gave victory to David wherever he went.
14 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
And David reigned over all Israel, and he executed justice and righteousness to all his people.
15 Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika;
And Joab the son of Zeruiah was over the army, and Jehoshaphat the son of Ahilud was recorder,
16 Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi;
and Zadok the son of Ahitub, and Abimelech the son of Abiathar, were priests, and Shavsha was scribe,
17 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.
and Benaiah the son of Jehoiada was over the Cherethites and the Pelethites, and the sons of David were chief about the king.

< 1 Mbiri 18 >