< 1 Mbiri 17 >

1 Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”
And it came to pass, when David dwelt in his house, that David said to Nathan the prophet, Lo, I dwell in a house of cedar, but the ark of the covenant of Jehovah dwells under curtains.
2 Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”
And Nathan said to David, Do all that is in thy heart, for God is with thee.
3 Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,
And it came to pass the same night, that the word of God came to Nathan, saying,
4 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’
Go and tell David my servant, Thus says Jehovah, Thou shall not build for me a house to dwell in.
5 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena.
For I have not dwelt in a house since the day that I brought up Israel, to this day, but have gone from tent to tent, and from one tabernacle to another.
6 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
In all places wherein I have walked with all Israel, did I speak a word with any of the judges of Israel, whom I commanded to be shepherd of my people, saying, Why have ye not built for me a house of cedar?
7 Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli.
Now therefore thus thou shall say to my servant David, Thus says Jehovah of hosts, I took thee from the sheepfold, from following the sheep, that thou should be prince over my people Israel.
8 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
And I have been with thee wherever thou have gone, and have cut off all thine enemies from before thee. And I will make thee a name like the name of the great ones who are on the earth.
9 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja;
And I will appoint a place for my people Israel, and will plant them, that they may dwell in their own place, and be moved no more. Neither shall the sons of wickedness waste them any more, as at the first,
10 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse. “‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako.
and as from the day that I commanded judges to be over my people Israel. And I will subdue all thine enemies. Moreover I tell thee that Jehovah will build for thee a house.
11 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
And it shall come to pass, when thy days are fulfilled that thou must go to be with thy fathers, that I will set up thy seed after thee, who shall be of thy sons. And I will establish his kingdom.
12 Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
He shall build for me a house, and I will establish his throne forever.
13 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo.
I will be his father, and he shall be my son. And I will not take my loving kindness away from him as I took it from him who was before thee.
14 Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’”
But I will settle him in my house and in my kingdom forever, and his throne shall be established forever.
15 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
According to all these words, and according to all this vision, so Nathan spoke to David.
16 Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati, “Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?
Then David the king went in, and sat before Jehovah. And he said, Who am I, O Jehovah God, and what is my house, that thou have brought me thus far?
17 Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”
And this was a small thing in thine eyes, O God. But thou have spoken of thy servant's house for a great while to come, and have regarded me according to the estate of a man of high degree, O Jehovah God.
18 “Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu.
What can David say yet more to thee concerning the honor which is done to thy servant? For thou know thy servant.
19 Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.
O Jehovah, for thy servant's sake, and according to thine own heart, thou have wrought all this greatness, to make known all these great things.
20 “Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu.
O Jehovah, there is none like thee, neither is there any God besides thee, according to all that we have heard with our ears.
21 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
And what one nation on the earth is like thy people Israel, whom God went to redeem to himself for a people, to make thee a name by great and awesome things, in driving out nations from before thy people whom thou redeemed out of Egypt?
22 Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
For thy people Israel thou made thine own people forever. And thou, Jehovah, became their God.
23 “Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera,
And now, O Jehovah, let the word that thou have spoken concerning thy servant, and concerning his house, be established forever, and do as thou have spoken.
24 kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
And let thy name be established and magnified forever, saying, Jehovah of hosts is the God of Israel, even a God to Israel, and the house of David thy servant is established before thee.
25 “Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
For thou, O my God, have revealed to thy servant that thou will build him a house. Therefore thy servant has found in his heart to pray before thee.
26 Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
And now, O Jehovah, thou are God, and have promised this good thing to thy servant,
27 Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
and now it has pleased thee to bless the house of thy servant, that it may continue for ever before thee; for thou, O Jehovah, have blessed, and it is blessed forever.

< 1 Mbiri 17 >