< 1 Mbiri 15 >

1 Davide atadzimangira nyumba zina mu Mzinda wa Davide, iye anakonza malo a Bokosi la Mulungu ndipo analimangira tenti.
And David made for him houses in the city of David. And he prepared a place for the ark of God, and pitched a tent for it.
2 Pamenepo Davide anati, “Palibe wina ati anyamule Bokosi la Mulungu koma Alevi chifukwa Yehova anawasankha kuti azinyamula Bokosi la Yehova ndi kumatumikira pamaso pake nthawi zonse.”
Then David said, None ought to carry the ark of God but the Levites, for Jehovah has them chosen to carry the ark of God, and to minister to him forever.
3 Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse mu Yerusalemu kuti abweretse Bokosi la Yehova ku malo amene analikonzera.
And David assembled all Israel at Jerusalem to bring up the ark of Jehovah to its place, which he had prepared for it.
4 Iye anayitanitsa pamodzi zidzukulu za Aaroni ndi Alevi:
And David gathered together the sons of Aaron, and the Levites:
5 kuchokera ku banja la Kohati, mtsogoleri Urieli ndi abale ake 120.
of the sons of Kohath, Uriel the chief, and his brothers a hundred and twenty;
6 Kuchokera ku banja la Merari, mtsogoleri Asaya ndi abale ake 220;
of the sons of Merari, Asaiah the chief, and his brothers two hundred and twenty;
7 kuchokera ku banja la Geresomu, mtsogoleri Yoweli ndi abale ake 130;
of the sons of Gershom, Joel the chief, and his brothers a hundred and thirty;
8 kuchokera ku banja la Elizafani, mtsogoleri Semaya ndi abale ake 200;
of the sons of Elizaphan, Shemaiah the chief, and his brothers two hundred;
9 kuchokera ku banja la Hebroni, mtsogoleri Elieli ndi abale ake 80;
of the sons of Hebron, Eliel the chief, and his brothers eighty;
10 kuchokera ku banja la Uzieli, mtsogoleri Aminadabu ndi abale ake 112.
of the sons of Uzziel, Amminadab the chief, and his brothers a hundred and twelve.
11 Kenaka Davide anayitanitsa ansembe Zadoki ndi Abiatara, ndi Alevi awa, Urieli, Asaya, Yoweli, Semaya, Elieli ndi Aminadabu.
And David called for Zadok and Abiathar the priests, and for the Levites, for Uriel, Asaiah, and Joel, Shemaiah, and Eliel, and Amminadab.
12 Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu atsogoleri a mabanja a Alevi ndipo inu ndi abale anu Alevi mudziyeretse nokha ndi kubweretsa Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli ku malo amene ine ndalikonzera.
And said to them, Ye are the heads of the fathers of the Levites. Sanctify yourselves, both ye and your brothers, that ye may bring up the ark of Jehovah, the God of Israel, to the place that I have prepared for it.
13 Popeza kuti inu Alevi simunalinyamule poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anatikantha. Sitinafunse momwe tikanachitira monga mmene Iyeyo anafotokozera.”
For because ye did not at the first, Jehovah our God made a breach upon us, because we did not seek him according to the ordinance.
14 Kotero ansembe ndi Alevi anadziyeretsa ndi cholinga chakuti akatenge Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli.
So the priests and the Levites sanctified themselves to bring up the ark of Jehovah, the God of Israel.
15 Ndipo Alevi ananyamula Bokosi la Mulungu pa mapewa awo pa mitengo yake yonyamulira monga momwe Mose analamulira molingana ndi mawu a Yehova.
And the sons of the Levites bore the ark of God upon their shoulders with the staves thereon, as Moses commanded according to the word of Jehovah.
16 Davide anawuza atsogoleri a Alevi kuti asankhe abale awo kuti akhale oyimba nyimbo zachisangalalo, zoyimba ndi zida: azeze, apangwe ndi ziwaya za malipenga.
And David spoke to the chief of the Levites to appoint their brothers the singers, with instruments of music, psalteries and harps and cymbals, sounding aloud and lifting up the voice with joy.
17 Kotero Alevi anasankha Hemani mwana wa Yoweli; ndipo mwa abale ake anasankha Asafu mwana wa Berekiya; ndipo mwa ana a Merari, abale awo, anasankha Etani mwana wa Kusaya;
So the Levites appointed Heman the son of Joel. And of his brothers, Asaph the son of Berechiah. And of the sons of Merari their brothers, Ethan the son of Kushaiah.
18 ndipo pamodzi ndi iwowa abale awo otsatana nawo: Zekariya, Yaazieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Benaya, Maaseya, Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli, alonda a pa chipata.
And with them their brothers of the second degree, Zechariah, Ben, and Jaaziel, and Shemiramoth, and Jehiel, and Unni, Eliab, and Benaiah, and Maaseiah, and Mattithiah, and Eliphelehu, and Mikneiah, and Obed-edom, and Jeiel, the porters.
19 Anthu oyimba aja Hemani, Asafu ndi Etani ndiwo ankayimba ziwaya za malipenga zamkuwa;
So the singers, Heman, Asaph, and Ethan, were appointed with cymbals of brass to sound aloud.
20 Zekariya, Azieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Maaseya ndi Benaya ankayimba azeze a liwu lokwera;
And Zechariah, and Aziel, and Shemiramoth, and Jehiel, and Unni, and Eliab, and Maaseiah, and Benaiah, with psalteries set to Alamoth.
21 ndipo Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu, Yeiyeli ndi Azaziya ankayimba apangwe a liwu lotsika.
And Mattithiah, and Eliphelehu, and Mikneiah, and Obed-edom, and Jeiel, and Azaziah, with harps set to the Sheminith, to lead.
22 Kenaniya, mtsogoleri wa Alevi anali woyangʼanira mayimbidwe; uwu ndiye unali udindo wake pakuti anali waluso pa zimenezi.
And Chenaniah, chief of the Levites, was over the song. He instructed about the song because he was skilful.
23 Berekiya ndi Elikana anali olondera pa khomo la bokosilo.
And Berechiah and Elkanah were porters for the ark.
24 Ansembe awa; Sebaniya, Yehosafati, Netaneli, Amasai, Zekariya, Benaya ndi Eliezara ndiwo ankayimba malipenga patsogolo pa Bokosi la Mulungu. Obedi-Edomu ndi Yehiya analinso alonda a pa khomo la bokosilo.
And Shebaniah, and Joshaphat, and Nethanel, and Amasai, and Zechariah, and Benaiah, and Eliezer, the priests, blew the trumpets before the ark of God. And Obed-edom and Jehiah were porters for the ark.
25 Choncho Davide pamodzi ndi akuluakulu a Israeli ndiponso asilikali olamulira magulu a anthu 1,000, anapita kukatenga Bokosi la Chipangano la Yehova ku nyumba ya Obedi-Edomu akukondwera.
So David, and the elders of Israel, and the captains over thousands, went to bring up the ark of the covenant of Jehovah out of the house of Obed-edom with joy.
26 Popeza Mulungu anathandiza Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, anapereka nsembe ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndiponso nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.
And it came to pass, when God helped the Levites who bore the ark of the covenant of Jehovah, that they sacrificed seven bullocks and seven rams.
27 Ndipo Davide anali atavala mkanjo wa nsalu yofewa yosalala, monga anavalira Alevi onse amene ananyamula bokosi pamodzi anthu oyimba, ndiponso Kenaniya, amene anali woyangʼanira magulu oyimba. Davide anavalanso efodi ya nsalu yofewa yosalala.
And David was clothed with a robe of fine linen, and all the Levites who bore the ark, and the singers, and Chenaniah the master of the song with the singers. And David had upon him an ephod of linen.
28 Kotero Aisraeli onse anabweretsa Bokosi la Chipangano la Yehova ndi mfuwu, ndiponso akuyimba zitoliro zanyanga zankhosa zazimuna, malipenga ndi maseche ndiponso akuyimba azeze ndi apangwe.
Thus all Israel brought up the ark of the covenant of Jehovah with shouting, and with sound of the cornet, and with trumpets, and with cymbals, sounding aloud with psalteries and harps.
29 Bokosi la Chipangano la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikuvina ndi kukondwera, iye ananyoza Davideyo mu mtima mwake.
And it came to pass, as the ark of the covenant of Jehovah came to the city of David, that Michal the daughter of Saul looked out at the window, and saw king David dancing and playing. And she despised him in her heart.

< 1 Mbiri 15 >