< 1 Mbiri 14 >

1 Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu.
And Hiram king of Tyre sent messengers to David, and cedar trees, and masons, and carpenters, to build for him a house.
2 Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
And David perceived that Jehovah had established him king over Israel, for his kingdom was exalted on high for his people Israel's sake.
3 Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
And David took more wives at Jerusalem, and David begot more sons and daughters.
4 Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
And these are the names of the children whom he had in Jerusalem: Shammua, and Shobab, Nathan, and Solomon,
5 Ibihari, Elisua, Elipeleti,
and Ibhar, and Elishua, and Elpelet,
6 Noga, Nefegi, Yafiya,
and Nogah, and Nepheg, and Japhia,
7 Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.
and Elishama, and Beeliada, and Eliphelet.
8 Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo.
And when the Philistines heard that David was anointed king over all Israel, all the Philistines went up to seek David. And David heard of it, and went out against them.
9 Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu.
Now the Philistines had come and made a raid in the valley of Rephaim.
10 Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”
And David inquired of God, saying, Shall I go up against the Philistines? And will thou deliver them into my hand? And Jehovah said to him, Go up, for I will deliver them into thy hand.
11 Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu.
So they came up to Baal-perazim, and David smote them there. And David said, God has broken my enemies by my hand like the breach of waters. Therefore they called the name of that place Baal-perazim.
12 Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.
And they left their gods there. And David gave commandment, and they were burned with fire.
13 Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo.
And the Philistines yet again made a raid in the valley.
14 Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
And David inquired again of God. And God said to him, Thou shall not go up after them. Turn away from them, and come upon them opposite the mulberry trees.
15 Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
And it shall be, when thou hear the sound of marching in the tops of the mulberry trees, that then thou shall go out to battle. For God has gone out before thee to smite the army of the Philistines.
16 Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.
And David did as God commanded him, and they smote the army of the Philistines from Gibeon even to Gezer.
17 Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.
And the fame of David went out into all lands. And Jehovah brought the fear of him upon all nations.

< 1 Mbiri 14 >