< Yohani 5 >

1 Pambele uYesu akaluta kulikaaja ilya Yelusalemu ku kikulukulu ikya Vayahudi.
Patapita nthawi Yesu anakwera kupita ku Yerusalemu ku phwando la Ayuda.
2 Mu likaaja ilio pweghulyale umulyango um'baha ghuno ghukatambuluagha, mulyango ghwa ng'holo, piipi nu mulyango ughuo pwelilyale ililamba lino munjovele ija Kiebulania likatambulwagha Bethzatha, mulubale mulilamba ilio pwefilyale ifibalasa fihano ifyeleefu.
Ndipo ku Yerusalemuko pafupi ndi chipata cha Nkhosa kuli dziwe limene mʼChihebri limatchedwa Betisaida ndipo ndi lozunguliridwa ndi makumbi asanu.
3 Mu lusulua ulwa fibalasa ifio valyaghonile avatamu vinga, avabofu amaaso, avalema amaghulu, na vanya liteela. (Vingilila: Amasio agha kadebe aka 3 naghivoneka mu malembe amanofu amakuulu. “Vakaghulagha amalenga ghatimbusivue.”)
Mʼmenemo munkagonamo gulu lalikulu la anthu odwala, osaona, olumala ndi ofa ziwalo.
4 Mu uluo, juno akavisagha ghwa kwasia kukwingila pano amalenga ghatimbwike, alyale isooka inhamu jaake.
Pakuti nthawi zina mngelo wa Ambuye ankatsikira mʼdziwemo nʼkuvundula madziwo. Woyamba kulowamo madzi atavundulidwa, ankachira ngakhale akhale ndi nthenda yanji.
5 Lino palilamba pala pwealyale umuunhu jumonga juno alyale ntamu amaaka fijigho fitatu na lekelakwoni.
Mmodzi wa amene anali pamenepo anali atadwala zaka 38.
6 UYesu akamwagha umuunhu ujuo aghonile pala alyakagwile kuuti umuunhu ujuo inhamu jaake ja maaka minga, akamposia akati, “Asi ghulonda kusooka?”
Yesu atamuona ali chigonere, nadziwa kuti anakhala chotero kwa nthawi yayitali, anamufunsa iye kuti, “Kodi ukufuna kuchira?”
7 Untamu jula akamwamula akati, “Ghwe Ntwa, amalenga ghangatimbusivue, nkwale umuunhu ughwa kumbiika mu lilamba. Pano nilonda kukwingila mu lilamba ye nivonagha umuunhu ujunge anhaliile pikwingila.”
Wodwalayo anayankha kuti, “Ambuye, ndilibe wina aliyense woti angandithandize kulowa mʼdziwe pamene madzi avundulidwa. Pamene ndikuyesera kuti ndilowemo, wina amalowamo ine ndisanalowemo.”
8 Pe pano uYesu akam'buula akati, “Ima veghala iliteefu lyako vujagha.”
Ndipo Yesu anati kwa iye, “Imirira! Nyamula mphasa yako yamba kuyenda.”
9 Pala pala umuunhu jula akasooka, akaveghala iliteefu lyake, akavuuka iluta. Ikighono ikio jaale Sabato.
Nthawi yomweyo munthuyo anachiritsidwa. Iye ananyamula mphasa yake nayamba kuyenda. Tsiku limene izi zinachitika linali la Sabata.
10 Pe aVayahudi vakam'buula umuunhu jula juno asokile vakati, “Umusyughu kighono kya Sabato, indaghilo na sikwitikisia kupiinda iliteefu.”
Ndipo Ayuda anati kwa munthu amene anachiritsidwayo, “Lero ndi la Sabata; lamulo silikulola iwe kunyamula mphasa yako.”
11 Neke umuunhu jula akavamula akati, “Umuunhu juno asoosisie ghwe mwene ambulile kuuti, 'Veghala iliteefu lyako vujagha.”
Koma iye anayankha kuti, “Munthu amene wandichiritsa anati kwa ine, ‘Nyamula mphasa yako yamba kuyenda.’”
12 Vakamposia kange vakati, “Ghwe veeni juno akuvulile kuuti 'Veghala iliteefu lyako vujagha?”
Pamenepo anamufunsa iye kuti, “Kodi munthu ameneyo ndani amene wakuwuza kuti, ‘Nyamula mphasa yako ndipo yenda?’”
13 Neke umuunhu jula naalyammanyile juno ansosisie ulwakuva uYesu alyavukile kisyefu. Ulwakuva avaanu valyale vinga.
Munthu amene anachiritsidwayo sanadziwe kuti anali ndani, pakuti Yesu anangolowera mʼgulu la anthu ndi kupita.
14 Pambele uYesu akamwagha umuunhu jula munyumba inyimike ija kufunyila, akambuula akati, “Lolagha lino usokile! “Nungavombaghe inyivi kange nave ghuvomba lukukwagha ulutalamu ulukome kukila ulwa kwanda.”
Patapita nthawi Yesu anamupeza ku Nyumba ya Mulungu ndipo anati kwa iye, “Taona uli bwino tsopano. Usakachimwenso kuti choyipa choposa ichi chingakugwere.”
15 Umuunhu jula akavuuka pala akaluta kukuvavuula aVayahudi kuuti juno ansosisie ghwe Yesu.
Munthu uja anachoka ndi kukawawuza Ayuda kuti anali Yesu amene anamuchiritsa iye.
16 Pepano, vwimila amasio aghuo aVayahudi vakampumwisie uYesu, ulwakuva alyavombile isio mu kighono ikya Sabato.
Ndipo popeza Yesu amachita zinthu izi tsiku la Sabata, Ayuda anayamba kumulondalonda.
17 Neke uYesu akavavuula akati, “UNhaata ghwango ivomba imbombo ifighono fyoni, na juune nivomba imbombo ifighono fyoni.”
Yesu anawawuza kuti, “Atate anga amagwira ntchito nthawi zonse mpaka lero lino, ndipo Inenso ndili pa ntchito.”
18 Vwimila uluo aVayahudi vakava vighina kulonda isila ija kum'buda uYesu vakalonda kukum'buda ulwakuva vakatisagha adenyile ululaghilo lwa kighono ikya Sabati, kange ijova kuuti, uNguluve ghwe viise, kange ikuviika kuuti aling'hiine nu Nguluve.
Chifukwa cha ichi Ayuda anawirikiza kufuna kumupha; osati chifukwa chakuswa Sabata kokha komanso chifukwa ankanena kuti Mulungu ndi Atate ake, nadziyesa Iye wofanana ndi Mulungu.
19 UYesu akavavuula akati, “Kyang'haani nikuvavuula une ne mwanaake nanivomba lumonga vwimila amasaaghe ghango, looli nivomba si sino nikumwagha uNhaata ivomba, nijova uluo, ulwakuva sino ivomba uNhaata se sino najune ne mwanaake nivoomba.
Yesu anawapatsa yankho ili: “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Mwana sangathe kuchita kanthu pa Iye yekha. Iye amachita zokhazo zimene amaona Atate ake akuchita, chifukwa chilichonse chimene Atate amachita Mwana amachitanso.
20 UNhaata anganile une ne mwanaake, ikuhofia sooni sino ivomba umwene, kange ilikuhufia une imbombo sino ilonda nivombe, imbombo imbaha kukila isio, kuuti pe mudeghe fiijo.
Pakuti Atate amakonda Mwana, amamuonetsa zonse zimene Iwo amachita. Inde, Atate adzamuonetsa zinthu zazikulu kuposa zimenezi ndipo mudzadabwa.
21 Ndavule uNhaata vule ikuvasyusia avafue na kukuvapeela uvwumi, fye enendiiki na juune nikuvapeela uvwumi, vano nilonda kukuvapeela.
Pakuti monga Atate amaukitsa akufa nawapatsa moyo, momwemonso Mwana amapereka moyo kwa amene Iye akufuna.
22 Ulwakuva uNhaata naihigha muunhu, looli ampeliile umwanake uvutavulilua uvwa kuhigha,
Komanso, Atate saweruza aliyense koma wapereka kwa Mwana ulamuliro woweruzawo,
23 Kuuti avaanhu vooni vamwoghopaghe ndavule vikumwoghopa umwene. Umuunhu juno naikumwoghopa umwanake naikumwoghopa uNhata juno ansung'hile.
kuti aliyense alemekeze Mwanayo monga momwe amalemekezera Atate. Munthu amene salemekeza Mwana salemekezanso Atate amene anamutuma Mwanayo.
24 Kyang'haani nikuvavuula, umuunhu juno ipulika amasio ghango na kukumwitika uNguluve juno asung'hile ali nu vwumi uvwa fighono fyoni. Kange nailihighua. Looli ujuo akilile uvufue na kukwingila ku vwumi uvwa kuvusila kusila. (aiōnios g166)
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene amamva mawu anga ndi kukhulupirira Iye amene ananditumiza Ine, ali ndi moyo wosatha ndipo sadzaweruzidwa. Iye wachoka mu imfa ndipo walowa mʼmoyo. (aiōnios g166)
25 Kyang'haani nikuvavuula, unsiki ghukwisa, kange ghufikile, avafue vilipulika, viliiva nu vwumi uvwa kuvusila kusila.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti nthawi ikubwera ndipo yafika kale tsopano, pamene akufa adzamva mawu a Mwana wa Mulungu ndipo iwo amene amva adzakhala ndi moyo.
26 Nijo uluo ulwakuva ndavule uNhaata vule ali ni ngufu isa kumpeela umuunhu uvwumi uvwa kuvisila kusila, najuune amheliile ingufu isa kuvapeela avaanhu uvwumi uvuo.
Pakuti monga Atate ali gwero la moyo, momwemonso anapereka mphamvu zopereka moyo mwa Mwana.
27 Kange, amheliile uvtavulilua uvwa kuhigha avaanhu, ulwakuva une nili, Mwana ghwa Muunhu.
Ndipo wamupatsa Iye ulamuliro woweruza chifukwa ndi Mwana wa Munthu.
28 Namungadeghaghe amasio aghuo, ulwakuva ghukwisa unsiki ghuno avafue vooni vilipulika ing'hemeelo jaango.
“Musadabwe ndi zimenezi. Pakuti nthawi ikubwera pamene onse amene ali mʼmanda adzamva mawu ake
29 Avafue vilisyuka: vano vavombagha inofu viiva nu vwumi uvwa fighono fyoni, vano vavombagha uvuhosi vilihighua.
ndi kutuluka. Iwo amene anachita zabwino adzauka ndi kupita ku moyo wosatha ndipo amene anachita zoyipa adzauka ndi kupita ku chilango chamuyaya.
30 UYesu akafijovagha akati une nanivomba kimonga vwimila amasaaghe ghango, une nihigha avaanhu ndavule ikumbuula uNhata. Nihigha mu vwakyang'haani, ulwakuva nanivomba muvughane vwango, looli mu vughane vwa Nguluve juno asung'hile.
Pakuti sindingathe kuchita kena kalikonse pa ndekha. Ine ndimaweruza molingana ndi zomwe Mulungu wandiwuza ndipo kuweruza kwanga ndi kolungama. Ine sindifuna kudzikondweretsa ndekha koma Iye amene anandituma.
31 Nave une nikujoleka juune, uvwolesi vwango navwale vuuva vwa kyang'haani.
“Ngati ndidzichitira umboni ndekha, umboni wanga si woona.
32 Looli kwale ujunge juno ikwoleka imhola sango na juune nikagwile kuuti sino ikwoleka vwimila une sa kyang'haani.
Alipo wina amene amandichitira umboni wabwino. Ine ndikudziwa kuti umboni wake wonena za Ine ndi woona.
33 Umue mulyasung'hile avaanhu kwa Yohani umwofughi, ghwope alyavoliike isa kyang'haani vwimila une.
“Inu munatumiza amithenga kwa Yohane ndipo iye anachitira umboni choona.
34 Neke une nanihuviila sino vikwoleka avaanhu, ulwene nijova isi kuuti mukave uvupoki.
Sikuti Ine ndikudalira umboni wa munthu; koma ndikunena zimenezi kuti mupulumutsidwe.
35 UYohani umwofughi alyahufisie uvwakyang'haani kulyumue, ndavule itaala vule jiviika na kumulika mung'hiisi, umue mulyahovwike vwimila uluo ku nsiki ndebe.
Yohane anali ngati nyale imene imayaka ndi kuwala, ndipo inu kwa kanthawi munasankha kusangalala ndi kuwala kwakeko.
36 Neke une nili ni mhola sino sikunyoleka fiijo kukila sino alyoliike uYohani, ulwakuva imbombo sino nivomba, sino alyamheliile uNhaata kuuti nivombe, se sino sikunyoleka kuuti uNhaata juno asung'hile.
“Koma Ine ndili ndi umboni woposa uja wa Yohane. Pakuti ntchito imene Atate andipatsa kuti ndiyikwaniritse ndi imene ndikugwira, ndipo ikundichitira umboni kuti Atate andituma Ine.
37 Ghope uNhaata juno asunghile une, ikwoleka imhola sango. Umue namughelile nambe lusiku kupulika ilisio lyake, kukumwagha vule alivuo unsiki ghwoni.
Ndipo Atate amene anandituma Ine, Iye mwini wandichitira umboni. Inu simunamvepo mawu ake kapena kuona maonekedwe ake,
38 Kange imbulanisio saake nasili nkate mulyumue ulwakuva namukumwitika juno asung'hilue kulyumue.
kapena mawu ake kukhala mwa inu, pakuti simukhulupirira Iye amene anamutuma.
39 Mughimba kulolesia mu malembe amimike, ulwakuva musagha kuti nkate umuo mukava uvwumi uvwa kuvusila kusila, amalembe aghu ghikunyoleka une. (aiōnios g166)
Inu mumasanthula malemba chifukwa mumaganiza kuti mʼmalembamo muli moyo wosatha. Awa ndi malemba amene akundichitira umboni. (aiōnios g166)
40 Neke umue namulonda kukwisa kulyune, kuuti mu pelue uvwumi uvwumi uvwa kuvusila kusila.
Koma inu mukukana kubwera kwa Ine kuti mukhale ndi moyo.
41 Une nanihuviila avaanhu vanginie,
“Ine sindilandira ulemu kuchokera kwa anthu
42 neke nikagwile kuuti nkate mulyumue namuli nu lughano lwa Nguluve.
koma Ine ndikukudziwani. Ndikudziwa kuti mʼmitima mwanu mulibe chikondi cha Mulungu.
43 Une nisile mu vutavulilua uvwa Nhaata ghwango, umue namukunyupila. Neke ujunge angiise mu vutavulilua vwake jujuo, mwale mukumwupila.
Ine ndabwera mʼdzina la Atate anga, ndipo inu simukundirandira Ine; koma wina wake akabwera mʼdzina la iye mwini, inu mudzamulandira.
44 Lino ndepoonu mukunyitika ndaani umue mwe vano mulonda kughinisivua na vaanhu, namulonda kughinisivua nu Nguluve juno ali jumo mwene?
Kodi inu mudzakhulupirira bwanji ngati mumapatsana ulemu wina ndi mnzake, ndipo simufuna kulandira ulemu kuchokera kwa Mulungu yekhayo?
45 Mulekaghe piiti ue nilikuvatwala kwa Nhaata avahighe. UMoose ghwe juno ilikuvatwala muhighue ulwakuva ghwe juno mukumhuviila.
“Koma inu musaganize kuti Ine ndidzakunenezani kwa Atate. Wokunenezani ndi Mose, amene inu mwayikapo chiyembekezo chanu.
46 Musava mukumwitika uMoose, ngale mukunyitika na juune, ulwakuva alyalembile imhola sango.
Ngati mukanakhulupirira Mose, mukanakhulupiriranso Ine, pakuti iye analemba za Ine.
47 Neke nave namukwitika amasio ghano alyalembile uMoose, ndepoonu mukwitika ndaani amasio ghango?
Koma ngati simukhulupirira zimene iye analemba, mudzakhulupirira bwanji zimene Ine ndikunena?”

< Yohani 5 >