< До римлян 7 >

1 Чи ви не знаєте, браття, — бо говорю́ тим, хто знає Закона, — що Зако́н панує над люди́ною, поки вона живе?
Kodi simukudziwa abale kuti Malamulo ali ndi ulamuliro pa munthu pokhapokha ngati ali ndi moyo? Ine ndikuyankhula kwa anthu amene akudziwa Malamulo.
2 Бо замі́жня жінка, поки живе чоловік, прив'язана до нього Законом; а коли помре чоловік, вона звільняється від закону чоловіка.
Mwachitsanzo, Malamulo amati mkazi wokwatiwa ndi womangidwa ndi lamulo kwa mwamuna wakeyo nthawi yonse pamene mwamuna wakeyo ali moyo. Koma ngati mwamuna wake amwalira, mkaziyo ndi womasulidwa ku lamulo la ukwati.
3 Тому то, поки живе чоловік, вона буде вважатися перелю́бницею, якщо стане дружи́ною іншому чоловікові; коли ж чоловік помре, вона вільна від Зако́ну, і не буде перелю́бницею, якщо стане за дружи́ну іншому чоловікові.
Koma ngati iye akwatiwa ndi mwamuna wina pamene mwamuna wake ali moyo, amatchedwa wachigololo. Koma ngati mwamuna wakeyo amwalira, mkaziyo amasuka ku lamulo ndipo si wachigololo, ngakhale kuti wakwatiwa ndi mwamuna wina.
4 Так, мої браття, і ви вмерли для Зако́ну через тіло Христове, щоб належати вам іншому, Воскре́слому з мертвих, щоб прино́сити плід Богові.
Chimodzimodzi inunso, abale anga, munafa ku Malamulo kudzera mʼthupi la Khristu, kuti mukwatiwe ndi wina, ndi Iye amene anauka kwa akufa kuti tibalire Mulungu chipatso.
5 Бо коли ми жили за ті́лом, то при́страсті гріховні, що похо́дять від Закону, ді́яли в наших членах, щоб прино́сити плід смерти.
Pakuti pamene tinkalamulidwa ndi khalidwe lathu lauchimo, zilakolako zauchimo zimene Malamulo anaziwutsa zinkagwira ntchito mʼmatupi mwathu kotero kuti zinabala imfa.
6 А тепер ми звільни́лись від Закону, умерши для того, чим були зв'язані, щоб служити нам обно́вленням духа, а не старістю букви.
Koma tsopano tamasulidwa ku Malamulowo pakuti tinafa ku zimene zinkatimanga, ndipo Mzimu Woyera akutithandiza kutumikira Mulungu mʼnjira yatsopano ndipo osati mʼnjira yakale yolembedwa.
7 Що ж скажемо? Чи Зако́н — то гріх? Зо́всім ні! Але я не пізнав гріха, як тільки через Зако́н, бо я не знав би пожадливости, коли б Закон не наказував: „Не пожада́й“.
Nanga ife tinene chiyani? Kodi Malamulo ndi oyipa? Ayi. Nʼkosatheka! Kunena zoona, popanda Malamulo, ine sindikanazindikira tchimo. Pakuti sindikanadziwa kuti kusirira ndi tchimo ngati Malamulo sakananena kuti, “Usasirire.”
8 Але гріх, узявши при́від від заповіді, зробив у мені всяку пожадливість, бо без Закону гріх мертвий.
Koma chifukwa cha Malamulo uchimo unapeza mwayi owutsa mʼkati mwanga khalidwe lililonse la kusirira. Pakuti pakanapanda Malamulo, uchimo ukanakhala wopanda mphamvu.
9 А я колись жив без Закону, але, коли прийшла заповідь, то гріх ожив,
Nthawi ina ndinali ndi moyo popanda Malamulo. Koma nditayamba kudziwa Malamulo, pomwepo uchimo unayamba kuphuka,
10 а я вмер; і сталася мені та заповідь, що для життя, на смерть,
ndipo ine ndinafa. Ine ndinazindikira kuti Malamulo omwe ankayenera kubweretsa moyo anabweretsa imfa.
11 бо гріх, узявши причину від заповіді, звів мене, і нею вмертви́в.
Pakuti uchimo unapeza mwayi chifukwa cha Malamulo ndipo kudzera mʼMalamulowo, unandinyenga ndi kundiyika mu imfa.
12 Тому́ то Зако́н святий, і заповідь свята, і праведна, і добра.
Choncho lamulo ndi loyera, lolungama ndi labwino.
13 Тож чи добре стало мені смертю? Зо́всім ні! Але гріх, щоб стати гріхом, приніс мені смерть добром, щоб гріх став мі́цно грі́шний через за́повідь.
Kodi chomwe ndi chabwino tsopano chinasanduka imfa kwa ine? Si choncho ayi! Koma kuti uchimo uzindikirike kuti ndi uchimo unabala imfa mwa ine kudzera mu chomwe chinali chabwino, kotero kuti kudzera mu lamulo uchimo ukhale oyipa kopitirira.
14 Бо ми знаємо, що Зако́н духовний, а я тіле́сний, про́даний під гріх.
Ife tikudziwa kuti Malamulo ndi auzimu; koma ine ndine munthu wofowoka chabe, wogulitsidwa ngati kapolo ku uchimo.
15 Бо що́ я виконую, не розумію; я бо чиню не те, що́ хочу, але що́ нена́виджу, те я роблю́.
Ine sindizindikira zimene ndimachita. Pakuti zimene ndimafuna kuchita sindizichita koma zimene ndimadana nazo ndi zimene ndimazichita.
16 А коли роблю́ те, чого я не хо́чу, то згоджуюсь із Законом, що він добрий,
Ndipo ngati ndimachita zimene sindimafuna kuzichita, ndiye kuti ndikuvomereza kuti lamulo ndi labwino.
17 а тому вже не я це виконую, але гріх, що живе в мені.
Monga mmene zililimu, si inenso mwini amene ndimazichita zimenezi, koma tchimo limene lili mʼkati mwanga.
18 Знаю бо, що не живе в мені, цебто в тілі моїм, добре; бо бажа́ння лежить у мені, але щоб виконати добре, того не знахо́джу.
Ine ndikudziwa kuti mwa ine mulibe kanthu kabwino, ndiye kuti mʼthupi langa lauchimo. Pakuti ndimafuna kuchita zabwino, koma ndimalephera kuzichita.
19 Бо не роблю́ я доброго, що хочу, але зле, чого не хочу, це чиню.
Ine sindichita zabwino zimene ndimafuna koma ndimachita zonyansa zimene sindikuzifuna.
20 Коли ж я роблю́ те, чого не хочу, то вже не я це виконую, але гріх, що живе в мені.
Tsopano ngati ine ndimachita zimene sindikuzifuna, si inenso amene ndimazichita, koma ndi tchimo limene lili mʼkati mwanga.
21 Тож знахо́джу зако́на, коли хочу робити добро, — що зло лежить у мені.
Tsono ndapeza kuti lamuloli likugwira ntchito. Ngakhale ndimafuna kuchita zabwino, zoyipa zili nane pomwepo.
22 Бо маю задово́лення в Законі Божому за вну́трішнім чолові́ком,
Mtima wanga umakondwera ndi lamulo la Mulungu.
23 та бачу інший зако́н у членах своїх, що воює проти закону мого розуму, і поло́нить мене законом гріховним, що знахо́диться в членах моїх.
Koma mʼkati mwanga ndimaona lamulo lina likugwira ntchito kulimbana ndi zomwe mtima wanga umavomereza. Lamulo limenelo landisandutsa wamʼndende walamulo la uchimo lomwe likugwira ntchito mʼkati mwa ziwalo zanga.
24 Нещасна я люди́на! Хто мене ви́зволить від тіла цієї смерти?
Kalanga ine! Adzandipulumutsa ndani ku thupi la imfali?
25 Дякую Богові через Ісуса Христа, Господа нашого. Тому́ то я сам служу́ розумом Законові Божому, але тілом — закону гріховному.
Atamandike Mulungu, amene amandipulumutsa kudzera mwa Yesu Khristu Ambuye athu! Kotero tsono, ineyo ndi mtima wanga ndimatumikira lamulo la Mulungu, koma ndi thupi langa ndimatumikira lamulo la uchimo.

< До римлян 7 >