< Об'явлення 16 >

1 І я почув гучний голос із храму, що казав до семи анголів: „Ідіть, і вилийте на землю сім чаш гніву Божого!“
Kenaka ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Nyumba ya Mulungu ija kuwuza angelo asanu ndi awiri kuti, “Pitani, katsanulireni pa dziko lapansi ukali wa Mulungu umene uli mʼmbale zisanu ndi ziwirizi!”
2 I пішов перший ангол, і вилив на землю чашу свою. І шкідливі та люті болячки обсіли людей, хто мав знаме́но звіри́ни й вклонявсь її о́бразу.
Mngelo woyamba anapita natsanula mbale yake pa dziko lapansi ndipo zilonda zoyipa ndi zowawa zinabuka pa anthu amene anali ndi chizindikiro cha chirombo chija, napembedza fano lake.
3 А другий ангол вилив свою чашу до моря. І сталася кров, немов у мерця́, — і кожна істота жива вмерла в морі.
Mngelo wachiwiri anapita natsanula mbale yake pa nyanja ndipo madzi ake anasanduka magazi, magazi ake ngati a munthu wakufa. Chamoyo chilichonse cha mʼnyanjamo chinafa.
4 Третій же ангол вилив чашу свою на річки́ та на водні джере́ла, — і сталася кров.
Mngelo wachitatu anapita natsanula mbale yake pa mitsinje ndi akasupe amadzi ndipo zinasanduka magazi.
5 І почув я ангола вод, який говорив: „Ти праведний, що Ти є й що Ти був, і святий, що Ти це присудив!
Kenaka ndinamva mngelo wolamulira madzi uja akuti, “Inu mwachita chilungamo, Inu Woyerayo, amene mulipo ndipo munalipo;
6 Бо вони пролили́ кров святих та пророків, — і Ти дав їм напитися крови. Вони варті того!“
pakuti iwo anakhetsa magazi a oyera anu ndi aneneri anu, nʼchifukwa chake mwawapatsa magazi kuti amwe, zomwe zikuwayenera.”
7 І я чув, як же́ртівник говорив: „Так, Господи, Боже Вседержи́телю! Правдиві й справедливі суди Твої!“
Kenaka ndinamva mawu ochokera ku guwa lansembe akuti, “Inde, Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse, chiweruzo chanu ndi choona ndi cholungama.”
8 А ангол четвертий вилив свою чашу на сонце. І да́но йому палити людей огнем.
Mngelo wachinayi anapita natsanula mbale yake pa dzuwa ndipo dzuwa linapatsidwa mphamvu yopsereza anthu ndi moto.
9 І спека велика палила людей, і зневажа́ли вони Ім'я Бога, що має вла́ду над карами тими, — і вони не покаялися, щоб славу віддати Йому́.
Anapserera nako kutentha kwakukuluko ndipo anatukwana Mulungu, amene anali ndi ulamuliro pa miliri imeneyi, koma anakana kulapa ndi kumulemekeza.
10 А п'ятий ангол вилив чашу свою на престола звіри́ни. І затьми́лося царство її, і люди від болю кусали свої язики́,
Mngelo wachisanu anapita natsanula mbale yake pa mpando waufumu wa chirombo chija ndipo mdima unagwa ponse pamene panali ufumu wake. Anthu analuma malilime awo chifukwa cha ululu.
11 і Бога Небесного вони зневажа́ли від болю свого й від своїх болячо́к, — та в учинках своїх не пока́ялись!
Ndipo anatukwana Mulungu wakumwamba chifukwa cha maululu awo ndi zilonda zawo koma anakana kulapa pa zimene anachita.
12 Шостий же ангол вилив чашу свою на річку велику Ефра́т, — і вода її висохла, щоб пригото́вити дорогу царям, які від схід сонця.
Mngelo wachisanu ndi chimodzi anapita natsanula mbale yake pa mtsinje waukulu wa Yufurate, ndipo madzi ake anaphwa kuti pakhale njira yodzera mafumu ochokera kummawa.
13 І я бачив, що вихо́дили з уст змі́я, і з уст звіри́ни, і з уст неправдивого пророка три ду́хи нечисті, як жа́би, —
Kenaka ndinaona mizimu yoyipa itatu imene inkaoneka ngati achule; inatuluka mʼkamwa mwa chinjoka chija, mʼkamwa mwa chirombo chija ndi mʼkamwa mwa mneneri wonyenga uja.
14 це духи де́монські, що чинять озна́ки. Вони виходять до царів усього світу, щоб зібрати їх на війну того великого дня Вседержителя Бога.
Imeneyi ndiyo mizimu ya ziwanda imene imachita zizindikiro zodabwitsa ndipo imatuluka kupita kwa mafumu a dziko lonse, kukawasonkhanitsa ku nkhondo ya pa tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuzonse.
15 Ось іду, немов злодій! Блаженний, хто чуйни́й, і одежу свою береже, щоб наги́м не ходити, і щоб не бачили га́ньби його!
“Taonani, ndikubwera ngati mbala! Wodala munthu amene ali maso, nasunga zovala zake, kuti asayende maliseche kuti angaonetse maliseche ake.”
16 І зібрав їх на місце, яке по-єврейському зветься Армагеддо́н.
Kenaka mizimu ija inasonkhanitsa pamodzi mafumu ku malo amene mʼChihebri amatchedwa Armagedo.
17 Сьомий же ангол вилив чашу свою на повітря. І голос гучни́й залунав від небесного храму з престолу, говорячи: „Сталося!“
Mngelo wachisanu ndi chiwiri anatsanulira mbale yake mu mlengalenga ndipo ku Nyumba ya Mulungu kunamveka mawu ofuwula kuchokera ku mpando waufumu kuti, “Kwatha!”
18 I сталися бли́скавки й гу́ркіт та гро́ми, і сталось велике трясі́ння землі, якого не було́, відко́ли люди́на живе на землі. Великий такий землетру́с, такий міцний!
Kenaka kunachitika mphenzi, phokoso, mabingu ndi chivomerezi choopsa. Chivomerezi ngati ichi sichinachitikepo chikhalire cha munthu pa dziko lapansi. Chinali chivomerezi choopsa kwambiri.
19 І місто велике розпа́лося на три частини, і попадали лю́дські міста́. І великий Вавилон був згаданий перед Богом, щоб дати йому чашу вина Його лютого гніву.
Mzinda waukuluwo unagawika magawo atatu ndipo mizinda ya mitundu ya anthu inagwa. Mulungu anakumbukira Babuloni Wamkulu namupatsa chikho chake chodzaza ndi vinyo wa ukali wa mkwiyo wake.
20 І зник кожен о́стрів, і не зна́йдено гір!
Chilumba chilichonse chinathawa ndipo mapiri sanaonekenso.
21 І великий град, як важкі тягарі́, падав із неба на людей. І люди зневажали Бога за покара́ння градом, — бо кара Його була дуже велика!
Matalala akuluakulu olemera pafupifupi makilogalamu makumi asanu anagwa kuchokera kumwamba kugwera pa anthu. Ndipo anthu anatukwana Mulungu chifukwa cha mliri wa matalala popeza unali mliri woopsa kwambiri.

< Об'явлення 16 >