< Від Матвія 21 >

1 А коли вони набли́зились до Єрусалиму, і прийшли до Вітфагі́ї, до гори до Оли́вної, тоді Ісус вислав двох учнів,
Akuyandikira ku Yerusalemu anafika ku Betifage pa phiri la Olivi, Yesu anatumiza ophunzira awiri,
2 до них, кажучи: „Ідіть у село, яке перед вами, і зна́йдете зараз ослицю прив'язану та з нею осля́; відв'яжіть, і Мені приведіть їх.
nawawuza kuti, “Pitani ku mudzi uli patsogolo panu, ndipo mukakangolowa mʼmenemo mukapeza bulu womangidwa ali ndi mwana pa mbali pake. Mukawamasule ndipo mubwere nawo kwa Ine.
3 А як хто вам що́ скаже, відкажіть, що їх потребує Госпо́дь, — і він зараз пошле їх“.
Wina akakayankhula, mukamuwuze kuti Ambuye akuwafuna, ndipo adzawatumiza nthawi yomweyo.”
4 А це сталось, щоб спра́вдилось те, що сказав був пророк, промовляючи:
Izi zinachitika kukwaniritsa zimene zinayankhulidwa ndi mneneri:
5 „Скажіте Сіонській доньці́: Ось до тебе йде Цар твій! Він покі́рливий, і всів на осла, — на осля, під'яре́мної сина“.
“Uza mwana wamkazi wa Ziyoni, taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yofatsa ndi yokwera pa bulu, pa kamwana ka bulu, mwana wa nyama yonyamula katundu.”
6 А учні пішли та й зробили, як звелів їм Ісус.
Ophunzirawo anapita nachita monga Yesu anawalamulira.
7 Вони привели́ до Ісуса ослицю й осля́, і одежу поклали на них, — і Він сів на них.
Anabweretsa bulu ndi mwana wake, nayala zovala zawo pa abuluwo, ndipo Yesu anakwerapo.
8 І багато народу стелили одежу свою по дорозі, інші ж різали віття з дерев і стели́ли дорогою.
Gulu lalikulu la anthu linayala zovala zawo mu msewu pamene ena anadula nthambi zamitengo ndi kuziyala mu msewumo.
9 А наро́д, що йшов перед Ним і поза́ду, викрикував, кажучи: „Оса́нна Сину Давидовому! Благословенний, хто йде у Господнє Ім'я́! Осанна на висоті!“
Magulu amene anali patsogolo pake ndi amene amamutsatira anafuwula kuti, “Hosana Mwana wa Davide!” “Wodala Iye amene abwera mʼdzina la Ambuye!” “Hosana mmwambamwamba!”
10 А коли увійшов Він до Єрусалиму, то здвигнулося ціле місто, питаючи: „Хто́ це такий?“
Yesu atalowa mu Yerusalemu, mzinda wonse unatekeseka ndipo anthu anafunsa kuti, “Ndani ameneyu?”
11 А наро́д говорив: „Це Пророк, — Ісус із Назаре́ту Галілейського!“
Magulu a anthu anayankha kuti, “Uyu ndi Yesu, mneneri wochokera ku Nazareti.”
12 Потому Ісус увійшов у храм Божий, і вигнав усіх продавців і покупців у храмі, і попереверта́в грошомінам столи, та осло́ни — продавцям голубів.
Yesu analowa mʼdera lina la Nyumba ya Mulungu ndipo anatulutsa kunja anthu onse amene ankachita malonda. Anagubuduza matebulo a osinthira ndalama ndi mipando ya ogulitsa nkhunda.
13 І сказав їм: „Написано: „Дім Мій — буде домом молитви, “а ви робите з нього „печеру розбійників“.
Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzatchedwa Nyumba ya mapemphero koma inu mwayisandutsa phanga la anthu achifwamba.”
14 I приступили у храмі до Нього сліпі та криві, — і Він їх уздоро́вив.
Anthu osaona ndi olumala anabwera kwa Iye mʼNyumba ya Mulungu ndipo anawachiritsa.
15 А первосвященики й книжники, бачивши чуда, що Він учинив, і дітей, що в храмі викрикували: „Осанна Сину Давидовому“, обурилися,
Koma akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo ataona zodabwitsa zimene anachita, komanso ana akufuwula mʼNyumbayo kuti, “Hosana kwa Mwana wa Davide,” anapsa mtima.
16 та й сказали Йому: „Чи ти чуєш, що кажуть вони?“А Ісус відказав їм: „Так. Чи ж ви не читали нікол́и: „Із уст немовлят, і тих, що ссуть, учинив Ти хвалу“?
Anamufunsa kuti, “Kodi mukumva zimene anawa akunena?” Yesu anayankha nati, “Inde. Kodi simunawerenge kuti, “Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda mwatuluka mayamiko?”
17 І покинувши їх, Він вийшов за місто в Віфа́нію, — і там ніч перебув.
Ndipo anawasiya natuluka mu mzindawo ndi kupita ku Betaniya, kumene anakagona.
18 А вранці, до міста вертаючись, Він зголоднів.
Mmamawa, pamene amabwera ku mzinda, anamva njala.
19 І побачив Він при дорозі одне фі́ґове дерево, і до нього прийшов, та нічого, крім листя само́го, на нім не знайшов. І до нього Він каже: „Нехай пло́ду із тебе не буде ніко́ли повіки!“І фіґове дерево зараз усохло. (aiōn g165)
Ataona mtengo wamkuyu mʼmbali mwa msewu, anapitapo koma sanapeze kanthu koma masamba okhaokha. Pamenepo anati kwa mtengowo, “Usadzabalenso chipatso!” Nthawi yomweyo mtengowo unafota. (aiōn g165)
20 А учні, побачивши це, дивувалися та говорили: „Як швидко всохло це фіґове дерево!“
Ophunzira ataona zimenezi, anadabwa nafunsa kuti, “Kodi mtengo wamkuyuwu wauma msanga bwanji?”
21 Ісус же промовив у відповідь їм: „Поправді кажу́ вам: Коли б мали ви віру, і не мали су́мніву, то вчинили б не тільки як із фіговим деревом, а якби й цій горі ви сказали: „Порушся та кинься до моря“, — то й станеться те!
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ngati muli ndi chikhulupiriro ndipo simukayika, simudzangochita zokha zachitika kwa mkuyuzi, koma mudzatha kuwuza phiri ili kuti, ‘Pita, kadziponye wekha mʼnyanja,’ ndipo zidzachitikadi.
22 І все, чого ви в молитві попросите з вірою, — то одержите“.
Ngati mukhulupirira, mudzalandira chilichonse chimene muchipempha mʼpemphero.”
23 А коли Він прийшов у храм і навчав, поприхо́дили первосвященики й старші наро́ду до Нього й сказали: „Якою Ти вла́дою чиниш оце? І хто Тобі вла́ду цю дав?“
Yesu analowa mʼNyumba ya Mulungu, ndipo pamene ankaphunzitsa, akulu a ansembe ndi akuluakulu anabwera kwa Iye namufunsa kuti, “Muchita izi ndi ulamuliro wanji ndipo anakupatsani ndani ulamuliro umenewu?”
24 Ісус же промовив у відповідь їм: „Запитаю й Я вас одне слово. Як про нього дасте Мені відповідь, то й Я вам скажу́, якою вла́дою Я це чиню́.
Yesu anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani funso limodzi, mukandiyankha, Inenso ndikukuwuzani ndi ulamuliro wa yani umene ndikuchitira izi.
25 Іванове хрищення звідки було: із неба, чи від людей?“Вони ж міркували собі й говорили: „Коли скажемо: „Із неба“, відкаже Він нам: „Чого ж ви йому не повірили?“
Ubatizo wa Yohane unachokera kuti? Kumwamba kapena kwa anthu?” Anakambirana pakati pawo ndipo anati, “Tikati, ‘Kuchokera kumwamba,’ Iye adzafunsa kuti, ‘Bwanji simunakhulupirire?’
26 А як скажемо: „Від людей“, — боїмося наро́ду, бо Івана вважають усі за пророка“.
Koma tikati, ‘Kuchokera kwa anthu,’ ife tikuopa anthuwa, pakuti onse amakhulupirira kuti Yohane anali mneneri.”
27 І сказали Ісусові в відповідь: „Ми не знаємо“. Відказав їм і Він: „То й Я вам не скажу́, якою владою Я це чиню́.
Choncho anamuwuza Yesu kuti, “Sitikudziwa.” Pamenepo Iye anati, “Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wa yani umene ndichitira izi.”
28 А як вам здається? Один чоловік мав двох синів. Прийшовши до першого, він сказав: „Піди но, дитино, сьогодні, працюй у винограднику!“
“Kodi muganiza bwanji? Panali munthu wina anali ndi ana aamuna awiri. Anapita kwa woyamba nati, ‘Mwanawe pita kagwire ntchito lero mʼmunda wamphesa.’
29 А той відповів і сказав: „Готовий, панотче“, — і не пішов.
“Iye anayankha kuti, ‘Sindipita,’ koma pambuyo pake anasintha maganizo napita.
30 І, прийшовши до другого, так само сказав. А той відповів і сказав: „Я не хочу“. А потім покаявся, і пішов.
“Kenaka abambowo anapita kwa mwana winayo nanena chimodzimodzi. Iye anayankha kuti, ‘Ndipita abambo,’ koma sanapite.
31 Котрий же з двох учинив волю батькову?“Вони кажуть: „Останній“. Ісус промовляє до них: „Поправді кажу вам, що ми́тники та блудоді́йки випере́джують вас у Боже Царство.
“Ndani wa awiriwa anachita chimene abambo ake amafuna?” Anamuyankha nati, “Woyambayo.” Yesu anawawuza kuti, “Ndikuwuzani zoonadi, kuti amisonkho ndi adama akulowa mu ufumu wa Mulungu inu musanalowemo.”
32 Бо прийшов був до вас дорогою праведности Іван, та йому не повірили ви, а ми́тники та блудоді́йки йняли йому віри. А ви бачили, та проте не покаялися й опісля́, щоб повірити йому.
Pakuti Yohane anabwera kwa inu kuti akuonetseni njira yachilungamo, koma inu simunakhulupirire iye, koma amisonkho ndi adama anamukhulupirira. Koma ngakhale munaona izi, simunatembenuke mtima ndi kumukhulupirira iye.
33 Послухайте іншої притчі. Був госпо́дар один. Насадив виноградника він, обгородив його муром, ви́довбав у ньому чави́ло, башту поставив, — і віддав його винаря́м, та й пішов.
“Tamverani fanizo lina: Panali mwini munda amene anadzala mphesa. Anamanga mpanda kuzungulira mundawo, nakumba moponderamo mphesa ndipo anamanga nsanja. Kenaka anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi ena napita pa ulendo.
34 Коли ж надійшов час плоді́в, він до винарів послав рабів своїх, щоб прийняти плоди́ свої.
Pamene nthawi yokolola inakwana, anatumiza antchito ake kwa matenanti aja kuti akatenge zipatso zake.
35 Винарі ж рабів його похапали, — і одно́го побили, а другого замордували, а того вкаменува́ли.
“Alimi aja anagwira antchito ake; namenya mmodzi, napha wina, ndi kumuponya miyala wachitatuyo.
36 Знов послав він інших рабів, більш як перше, — та й їм учинили те саме.
Kenaka anatumiza antchito ena oposa oyambawo ndipo matenantiwo anawachitira chimodzimodzi.
37 Нарешті послав до них сина свого́ і сказав: „Посоро́мляться сина мого“.
Pomalizira anatumiza mwana wake. Anati adzamuchitira ulemu mwana wanga.
38 Але́ винарі́, як побачили сина, міркувати собі стали: „Це спадкоє́мець; ходім, замордуймо його, — і заберемо його спа́дщину!“
“Koma alimiwo ataona mwanayo anati kwa wina ndi mnzake, ‘Uyu ndiye olowa mʼmalo mwa abambo ake. Tiyeni timuphe ndipo titenge cholowa chake.’
39 І, схопи́вши його, вони вивели за виноградник його, та й убили.
Pamenepo anamutenga namuponyera kunja kwa munda wamphesa namupha.
40 Отож, як прибу́де той пан виноградника, що́ зробить він тим винаря́м?“
“Tsono akabwera mwini munda wamphesa adzachita nawo chiyani matenantiwo?”
41 Вони кажуть Йому: „Злочинців погубить жорсто́ко, виноградника ж віддасть іншим винаря́м, що будуть плоди́ віддавати йому своєча́сно“.
Iwo anayankha kuti, “Adzawapha moyipa alimi oyipawo ndipo adzabwereketsa mundawo kwa alimi ena amene adzamupatsa gawo lake la mbewu pa nthawi yokolola.”
42 Ісус промовляє до них: „Чи ви не читали ніко́ли в Писа́нні: Камінь, що його будівничі відкинули, — той наріжним став каменем; від Господа сталося це, і дивне воно в очах наших!“
Yesu anawawuza kuti, “Kodi simunawerenge mʼmalemba kuti: “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana, womwewo wasanduka mwala wofunika kwambiri wa pa ngodya. Ambuye wachita izi, ndipo ndi zodabwitsa mʼmaso mwathu.’
43 Тому́ кажу вам, що від вас Царство Боже відійметься, і дасться наро́дові, що плоди́ його буде прино́сити.
“Nʼchifukwa chake ndi kukuwuzani kuti ufumu wa Mulungu udzalandidwa kwa inu ndipo udzapatsidwa kwa anthu amene adzabereka chipatso chake.
44 І хто впаде́ на цей камінь — розі́б'ється, а на кого він сам упаде — то розча́вить його́“.
Amene agwa pa mwalawu adzadukaduka, ndipo amene udzamugwere udzamuthudzula.”
45 А як первосвященики та фарисеї почули ці притчі Його, то вони зрозуміли, що про них Він гово́рить.
Akulu a ansembe ndi Afarisi atamva mafanizo a Yesu, anadziwa kuti ankanena iwo.
46 І намага́лись схопи́ти Його, але́ побоялись людей, бо вважали Його за Пророка.
Pamenepo anafuna njira yoti amugwirire, koma anaopa gulu la anthu chifukwa anthu onse ankakhulupirira kuti Iye anali mneneri.

< Від Матвія 21 >