< Від Марка 2 >

1 Коли ж Він по кількох днях прийшов знов до Капернау́му, то чутка пішла, що Він удома.
Patapita masiku pangʼono, Yesu atalowanso mu Kaperenawo, zinamveka kuti wabwera ali mʼnyumba.
2 І зібралось багато, аж вони не вміщалися навіть при две́рях. А Він їм виголошував слово.
Choncho anthu ambiri anasonkhana kotero kuti panalibenso malo, ngakhale ndi pa khomo pomwe, ndipo Iye anawalalikira mawu.
3 І прийшли ось до Нього, несучи розсла́бленого, якого не́сли четверо.
Amuna anayi anabwera, atanyamula munthu wofa ziwalo.
4 А що через наро́д до Ньо́го набли́зитися не могли, то стелю розкри́ли, де Він був, і пробравши, звісили ложе, що на ньому лежав розсла́блений.
Popeza sakanatha kufika naye kwa Yesu chifukwa cha gulu la anthu, anasasula denga chapamwamba pamene panali Yesu, ndipo atabowoleza, anatsitsa mphasa yomwe munthu wofa ziwaloyo anagonapo.
5 А Ісус, віру їхню побачивши, каже розсла́бленому: „Відпускаються, сину, гріхи тобі!“
Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati kwa wofa ziwaloyo, “Mwana, machimo ako akhululukidwa.”
6 Там же сиділи дехто з книжників, і в серцях своїх ду́мали:
Ndipo ena mwa aphunzitsi amalamulo anakhala pansi pomwepo, namaganiza mʼmitima mwawo kuti,
7 „Чого Він говорить отак? Зневажає Він Бога. Хто може прощати гріхи, окрім Бога Само́го?“
“Nʼchifukwa chiyani munthuyu ayankhula chotere? Iye akuchitira mwano Mulungu! Ndani angakhululukire munthu machimo kupatula Mulungu yekha?”
8 І зараз Ісус відчув Духом Своїм, що вони так міркують собі, і сказав їм: „Що́ таке ви в серцях своїх ду́маєте?
Nthawi yomweyo Yesu anadziwa mu mzimu wake kuti izi ndi zimene ankaganiza mʼmitima yawo, ndipo anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukuganiza zinthu izi?
9 Що́ легше: сказати розсла́бленому: „Гріхи відпускаються тобі“, чи сказати: „Уставай, візьми ложе своє та й ходи“?
Chapafupi nʼchiyani; kunena kwa wofa ziwaloyu kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kuti, ‘Imirira, tenga mphasa yako ndipo yenda?’
10 Але щоб ви знали, що Син Лю́дський має вла́ду прощати гріхи на землі“, — каже розсла́бленому:
Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo.” Anati kwa wofa ziwaloyo,
11 „Тобі Я наказую: Уставай, візьми ложе своє, та й іди у свій дім!“
“Ndikuwuza iwe, imirira, tenga mphasa yako ndipo pita kwanu.”
12 І той устав, і негайно взяв ложе, — і вийшов перед усіма́, так що всі дивувались і сла́вили Бога, й казали: „Ніко́ли такого не бачили ми!“
Anayimirira, nanyamula mphasa yake natuluka onse akumuona. Izi zinadabwitsa aliyense ndipo anayamika Mulungu nati, “Sitinaonepo zinthu ngati izi!”
13 І вийшов над море Він знов. А ввесь на́товп до Нього прихо́див, — і Він їх навчав.
Yesu anatulukanso napita kumbali ya nyanja. Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye, ndipo anayamba kuliphunzitsa.
14 А коли Він прохо́див, то побачив Леві́я Алфі́євого, що сидів на ми́тниці, і каже йому: „Іди за Мною!“Той устав, і пішов услід за Ним.
Pamene ankayendabe, anaona Levi mwana wa Alufeyo atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anamuwuza kuti, “Tsate Ine.” Ndipo Levi anayimirira namutsata Iye.
15 Коли ж Він сидів при столі́ в його домі, то багато ми́тників і грішників сиділи з Ісусом та з у́чнями Його; бо було їх багато, і вони ходили за Ним.
Yesu atakalandira chakudya ku nyumba kwa Levi, amisonkho ambiri ndi “ochimwa” ankadya naye pamodzi ndi ophunzira ake, pakuti anali ambiri amene anamutsatira.
16 Як побачили ж книжники та фарисеї, що Він їсть із грішниками та з ми́тниками, то сказали до учнів Його: „Чому́ то Він їсть із ми́тниками та з грішниками?“
Pamene aphunzitsi amalamulo a Afarisi anamuona akudya ndi “ochimwa” ndi amisonkho, anafunsa ophunzira ake kuti, “Chifukwa chiyani amadya ndi olandira msonkho ndi ochimwa?”
17 А Ісус, як почув, промовляє до них: „Лі́каря не потребують здорові, а слабі. Я не прийшов кликати праведних, але грішників (на покая́ння).“
Yesu atamva zimenezi, anawawuza kuti, “Anthu amene ali bwino safuna singʼanga koma odwala. Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa.”
18 А учні Іванові та фарисейські по́стили. І приходять вони, та й говорять до Нього: „Чому́ учні Іванові та фарисейські по́стять, а учні Твої не по́стять?“
Ndipo ophunzira a Yohane ndi a Afarisi amasala kudya. Anthu ena anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Zitheka bwanji kuti ophunzira a Yohane ndi ophunzira a Afarisi amasala kudya, koma anu satero?”
19 Ісус же промовив до них: „Хіба по́стити можуть гості весільні, поки з ними ще є молоди́й? Доки мають вони молодо́го з собою, то по́стити не можуть.
Yesu anayankha nati, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya bwanji pamene iye ali nawo pamodzi? Iwo sangatero, pamene iye ali nawo pamodzi.
20 Але при́йдуть ті дні, коли заберуть молодо́го від них, — то й по́стити бу́дуть вони за тих днів.
Koma nthawi idzafika pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo, ndipo pa tsiku limenelo adzasala kudya.
21 І не пришива́є ніхто до старої одежі ла́тки з сукна сирово́го, а як ні, то край ла́тки ново́ї оді́рветься там від старо́го, — і дірка стане ще гірша.
“Palibe amene amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale. Ngati atatero, chigamba chatsopanocho chidzazomola chovala chakalecho, kukulitsa chibowocho.
22 І ніхто не вливає вина молодого в старі бурдюки́, а то попрориває вино бурдюки, — і вино й бурдюки пропаду́ть, а вливають вино молоде до нови́х бурдюкі́в“.
Ndipo palibe amene amathira vinyo watsopano mʼmatumba akale a vinyo. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba a vinyo ndipo vinyoyo pamodzi ndi matumbawo zidzawonongeka. Ayi, satero, amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso.”
23 І сталось, як Він перехо́див лана́ми в суботу, Його учні дорогою йшли, та й стали коло́сся зривати.
Tsiku lina la Sabata, Yesu amadutsa pakati pa minda ya tirigu, ndipo ophunzira ake amayenda naye limodzi, nayamba kubudula ngala za tiriguyo.
24 Фарисеї ж казали Йому: Подивись, чому́ роблять у суботу вони, чого не годи́ться?“
Afarisi anati kwa Iye, “Taonani, chifukwa chiyani akuchita chosaloledwa ndi lamulo pa Sabata?”
25 А Він їм відказав: „Чи ж ви не читали ніко́ли, що зробив був Давид, як потребу він мав та сам зголоднів був і ті, що були з ним?
Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali osowa ndi anamva njala?
26 Як він увійшов був до Божого дому — за первосвященика Авіята́ра, — і спожив хліби показні́, яких їсти не можна було́, — тільки священикам, — і дав він і тим, хто був із ним?“
Pa nthawi ya Abiatara mkulu wa ansembe, iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndi kudya buledi wopatulika amene amaloledwa kuti adye ndi ansembe okha. Ndipo anapereka wina kwa anzake.”
27 І сказав Він до них: „Субота постала для чоловіка, а не чоловік для суботи,
Pamenepo anawawuza kuti, “Sabata linapangidwira munthu, osati munthu kupangidwira Sabata.
28 а тому то Син Лю́дський Господь і суботі“.
Choncho Mwana wa Munthu ali Ambuye ngakhale wa Sabata.”

< Від Марка 2 >