< Від Луки 20 >

1 І сталось одно́го з тих днів, як навчав Він у храмі людей, та Добру Нови́ну звіщав, прийшли первосвященики й книжники з старшими,
Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
2 та й до Нього промовили, кажучи: „Скажи нам, якою вла́дою Ти чиниш оце? Або хто Тобі вла́ду цю дав?“
Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”
3 І промовив до них Він у відповідь: „Запитаю й Я вас одну річ, — і відповідайте Мені:
Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe,
4 Іванове хрищення з неба було́, чи від людей?“
‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’”
5 Вони ж міркували собі й говорили: „Коли скажемо: „З неба“, відкаже: „Чого ж ви йому не повірили?“
Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’
6 А як скажемо: „Від людей“, то всі люди камінням поб'ють нас, бо були переко́нані, що Іван — то пророк“.
Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”
7 І вони відповіли, що не знають, ізвідки.
Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”
8 А Ісус відказав їм: „То й Я не скажу́ вам, якою вла́дою Я це чиню́“.
Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”
9 І Він розповідати почав людям при́тчу оцю. „Один чоловік насадив виноградника, і віддав його винаря́м, та й відбув на час довший.
Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali.
10 А певного ча́су послав він раба до своїх винарі́в, щоб дали йому частку з плоді́в виноградника. Та побили його винарі, і відіслали ні з чим.
Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu.
11 І знову послав він до них раба і́ншого, а вони й того збили й знева́жили, — та й відіслали ні з чим.
Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu.
12 І послав він ще третього, а вони й того зранили й вигнали.
Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.
13 Сказав тоді пан виноградника: „Що́ маю робити? Пошлю свого сина улю́бленого, — може його посоро́мляться“.
“Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’
14 Винарі́ ж, як його вгледіли, міркували собі та казали: „Це спадкоє́мець; ходім, замордуймо його, щоб спа́дщина наша була́“.
“Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’
15 І вони його вивели за виноградника, та й убили... Що́ ж зробить їм пан виноградника?
Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha. “Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa?
16 Він при́йде та й вигубить цих винарів, виноградника ж іншим віддасть“. Слухачі ж повіли́: „Нехай цього не станеться!“
Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.” Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”
17 А Він глянув на них та й сказав: „Що ж оце, що написане: „Камінь, що його будівничі відкинули, той нарі́жним став каменем!
Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti, “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana wasanduka mwala wa pa ngodya.
18 Кожен, хто впаде́ на цей камінь — розі́б'ється, а на кого він сам упаде́, — то розчавить його́“.
Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’”
19 А книжники й первосвященики руки на Нього хотіли накласти тієї години, але побоялись наро́ду. Бо вони розуміли, що про них Він цю притчу сказав.
Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.
20 І вони слідкували за Ним, і підіслали підгля́дачів, які праведних із себе вдавали, щоб зловити на слові Його, і Його видати урядові й вла́ді намісника.
Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza.
21 І вони запитали Його та сказали: „Учителю, знаємо ми, що Ти добре говориш і навчаєш, і не дивишся на обли́ччя, але наставляєш на Божу дорогу правдиво.
Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi.
22 Чи годи́ться давати податок для ке́саря, чи ні?“
Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”
23 Знаючи ж їхню хитрість, сказав Він до них: „Чого ви Мене випробо́вуєте?
Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti,
24 Покажіте дина́рія Мені. Чий образ і напис він має?“Вони відказали: „Кесарів“.
“Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”
25 А Він їм відказав: „Тож віддайте ке́сареве — ке́сареві, а Богові — Боже!“
Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.” Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”
26 І не могли вони перед людьми́ зловити на слові Його. І дивува́лись вони з Його відповіді, та й замовкли.
Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.
27 І підійшли дехто із саддукеїв, що твердять, ніби немає воскресі́ння, і запитали Його,
Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso.
28 та сказали: „Учителю, Мойсей написав нам: „Як умре кому брат, який має дружи́ну, а помре бездітний, — то нехай його брат візьме дружи́ну, і відно́вить насіння для брата свого“.
Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
29 Було ж сім братів. І перший, узявши дружи́ну, бездітний умер.
Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana.
30 І другий узяв був ту дружи́ну, та й той вмер бездітний.
Wachiwiri
31 І третій узяв був її, так само й усі се́меро, — і вони дітей не позоставили, та й повмирали.
ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana.
32 А по всіх умерла й жінка.
Pa mapeto pake mkaziyo anafanso.
33 А в воскресі́нні котро́му із них вона дружи́ною буде? Бо семеро мали за дружину її“.
Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”
34 Ісус же промовив у відповідь їм: „Женяться й заміж виходять сини цього віку. (aiōn g165)
Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn g165)
35 А ті, що будуть достойні того віку й воскресі́ння з мертвих, — не будуть ні женитись, ні заміж вихо́дити, (aiōn g165)
Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn g165)
36 ні вмерти вже не можуть, бо рівні вони ангола́м, і вони сини Божі, синами воскресі́ння бувши.
Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa.
37 А що мертві встають, то й Мойсей показав — при кущі, — коли він назвав Господа „Богом Авраамовим, і Богом Ісаковим, і Богом Якововим“.
Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’
38 Бог же не є Богом мертвих, а живих, бо всі в Нього живуть.“
Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”
39 Дехто ж із книжників відповіли та сказали: „Учителю, — Ти добре сказав!“
Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!”
40 І вже не насмілювалися питати Його ні про що́.
Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.
41 І сказав Він до них: „Як то кажуть, що Христос син Давидів?
Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide?
42 Таж Давид сам говорить у книзі Псалмів: „Промовив Господь Господе́ві моєму: сядь право́руч Мене,
Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani ku dzanja langa lamanja,
43 поки не покладу́ Я Твоїх ворогів підніжком ногам Твоїм!“
mpaka Ine nditasandutsa adani anu chopondapo mapazi anu?’
44 Отже, Давид Його Господом зве, — як же Він йому син?“
Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”
45 І, як увесь наро́д слухав, Він промовив до учнів Своїх:
Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake,
46 „Стережіться книжників, що хочуть у довгих одежах ходити, і люблять привіти на ринках, і перші лавки́ в синагогах, і перші місця на бенке́тах,
“Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando.
47 що вдови́ні хати́ поїдають, і моляться довго напо́каз, — вони тяжче осу́дження при́ймуть!“
Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”

< Від Луки 20 >