< Від Луки 17 >

1 І сказав Він до учнів Своїх: „Неможливо, щоб спокуси не мали прийти; але горе тому́, через кого приходять вони!
Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
2 Краще б такому було́, коли б жо́рно млино́ве на шию йому почепити та й кинути в море, аніж щоб спокусив він одно́го з мали́х цих!
Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
3 Уважайте на себе! Коли провини́ться твій брат, докори́ йому, а коли він покається, то вибач йому.
Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
4 І хоча б сім раз денно він провинивсь проти тебе, і сім раз звернувся до тебе, говорячи: „Каюся“, — вибач йому́!“
Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
5 І сказали апо́столи Господу: „Дода́й Ти нам віри!“
Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
6 А Господь відказав: „Коли б мали ви віру, хоч як зе́рно гірчи́чне, і сказали шовко́виці цій: „Ви́рвися з коренем і посадися до моря“, — то й послухала б вас!
Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
7 Хто ж із вас, мавши раба, що оре́ чи пасе, скаже йому, як він ве́рнеться з поля: „Негайно йди та сідай до столу“?
“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
8 Але чи ж не скаже йому: „Приготуй що вече́ряти, і підпережись, і мені прислуго́вуй, аж поки я їстиму й питиму, а пото́му ти сам будеш їсти та пити“?
Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
9 Чи ж він дякує тому рабові, що наказане виконав?
Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
10 Так і ви, коли зробите все вам нака́зане, то кажіть: „Ми — нікчемні раби, бо зробили лиш те, що повинні зробити були́!“
Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
11 І сталось, коли Він ішов до Єрусалиму, то прохо́див поміж Самарі́єю та Галілеєю.
Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
12 І, коли вхо́див до одно́го села, перестріли Його десять мужів, слаби́х на проказу, що стали здалека.
Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
13 І голос піднесли вони та й казали: „Ісусе, Наставнику, — змилуйсь над нами!“
ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
14 І, побачивши їх, Він промовив до них: „Підіть і покажіться священикам!“І сталось, коли вони йшли, то очи́стились.
Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
15 Один же з них, як побачив, що видужав, то верну́вся, і почав гучни́м голосом сла́вити Бога.
Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
16 І припав він обличчям до ніг Його, складаючи дяку Йому. А то самаряни́н був...
Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
17 Ісус же промовив у відповідь: „Чи не десять очи́стилось, — а дев'ять же де́?
Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
18 Чому́ не вернулись вони хвалу́ Богові віддати, крім цього́ чужинця?“
Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
19 І сказав Він йому: „Підведися й іди: твоя віра спасла тебе!“
Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
20 А як фарисеї спитали Його, коли Царство Боже при́йде, то Він їм відповів і сказав: „Царство Боже не при́йде помітно,
Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
21 і не скажуть: „Ось тут“, або: „Там“. Бо Боже Царство всере́дині вас!“
kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
22 І сказав Він до учнів: „Прийдуть дні, коли побажаєте бачити один з днів Сина Лю́дського, — та не побачите.
Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
23 І скажуть до вас: „Ось тут“, чи: „Ось там“, — не йдіть, і за ним не біжіть!
Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
24 Бо як бли́скавка, бли́снувши, світить із о́дного кра́ю під небом до другого кра́ю під небом, так буде Свого дня й Син Лю́дський.
Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
25 А перше належить багато страждати Йому, і відцурається рід цей від Нього.
Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
26 І, як було за днів Но́євих, то буде так само й за днів Сина Лю́дського:
“Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
27 їли, пили, женилися, заміж вихо́дили, аж до того дня, коли „Ной увійшов до ковче́гу“; прийшов же потоп, — і всіх вигубив.
Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
28 Так само, як було за днів Ло́тових: їли, пили, купували, продавали, садили, будували;
“Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
29 того ж дня, як Лот вийшов із Содо́му, — огонь із сіркою з неба лину́в, і всіх погубив.
Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
30 Так буде й того дня, як Син Лю́дський з'я́виться!
“Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
31 Хто буде того дня на домі, а речі його будуть у домі, нехай їх забрати не зла́зить. Хто ж на полі, так само нехай назад не верта́ється, —
Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
32 пам'ятайте про Ло́тову дружи́ну!
Kumbukirani mkazi wa Loti!
33 Хто дба́тиме зберегти свою душу, — той погубить її, а коли хто погубить, — той оживить її.
Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
34 Кажу вам: удвох будуть ночі тієї на о́дному ліжкові: один ві́зьметься, а другий поли́шиться.
Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
35 Дві моло́тимуть ра́зом, — одна ві́зьметься, а друга полишиться.
Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
36 Двоє будуть на полі, — один ві́зьметься, а другий полишиться!“
Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
37 І казали вони Йому в відповідь: „Де, Господи?“А Він відказав їм: „Де труп, там зберуться й орли“.
Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”

< Від Луки 17 >