< Від Луки 12 >

1 Того ча́су, як зібралися десятитисячні на́товпи наро́ду, — аж топтали вони один о́дного, — Він почав промовляти перш до учнів Своїх: „Стережіться ро́зчини фарисейської, що є лицемі́рство!
Nthawi yomweyo, anthu miyandamiyanda atasonkhana, ndi kumapondanapondana, Yesu anayamba kuyankhula poyamba kwa ophunzira ake, nati, “Chenjereni ndi yisiti wa Afarisi, amene ndi chinyengo.
2 Бо немає нічо́го захо́ваного, що не відкриється, ні таємного, що не ви́явиться.
Palibe chinthu chophimbika chimene sichidzawululika, kapena chobisika chimene sichidzadziwika.
3 Тому все, що́ казали ви по́темки, — при світлі почується, що́ ж шептали на вухо в коморах, — на даха́х проповідане бу́де.
Chimene mwanena mu mdima chidzamveka dzuwa likuwala, ndipo zimene mwanongʼona mʼkhutu mʼchipinda chamʼkati, zidzayankhulidwa pa denga la nyumba.
4 Кажу́ ж вам, Своїм друзям: Не бійтеся тих, хто тіло вбиває, а потім більш нічого не може вчинити!
“Ine ndikuwuzani, abwenzi anga, musachite mantha ndi amene amapha thupi chifukwa akatero sangachitenso kanthu.
5 Але вкажу вам, кого треба боятися: Бійтесь того́, хто має вла́ду, убивши, укинути в геє́нну. Так, кажу́ вам: Того бійтеся! (Geenna g1067)
Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. (Geenna g1067)
6 Чи ж не п'ять горобців продають за два гро́ші? Та проте перед Богом із них ні один не забутий.
Kodi atimba asanu samagulidwa ndi ndalama ziwiri? Ngakhale zili chomwecho palibe imodzi ya izo imene imayiwalika ndi Mulungu.
7 Але навіть воло́сся вам на голові порахо́ване все. Не бійтесь: вартніші ви за багатьох горобців!
Ndithudi, tsitsi lonse la mʼmutu mwanu ndi lowerengedwa. Musachite mantha; inu ndi oposa kwambiri mpheta zambiri.
8 Кажу ж вам: Кожного, хто перед людьми́ Мене визнає, того визнає й Син Лю́дський перед Ангола́ми Божими.
“Ine ndikukuwuza kuti, aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Mwana wa Munthu adzamuvomerezanso pamaso pa angelo a Mulungu.
9 Хто ж Мене відцурається перед людьми́, того відцураються перед ангола́ми Божими.
Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu adzakanidwanso pamaso pa angelo a Mulungu.
10 І кожному, хто скаже слово на Лю́дського Сина, йому про́ститься; а хто зневажа́тиме Духа Святого, — не про́ститься.
Ndipo aliyense amene ayankhulira Mwana wa Munthu mawu oyipa adzakhululukidwa, koma iye wochitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa.
11 А коли вас водитимуть до синагог, і до уря́дів, і до влад, — не турбуйтеся, я́к або що́ відповідати чи що́ говорити, —
“Akadzakutengerani ku masunagoge pamaso pa oweruza ndi a maulamuliro, musadere nkhawa mmene mudzadzitchinjirizire nokha kapena chimene mudzayankhule,
12 Дух бо Святий вас навчи́ть тієї години, що́ потрібно казати!“
pakuti Mzimu Woyera nthawi imeneyo adzakuphunzitsani zoyenera kunena.”
13 І озвався до Нього один із наро́ду: „Учителю, скажи братові моєму, щоб він спа́дщиною поділився зо мною“.
Munthu wina mʼgulu la anthu anati kwa Iye, “Aphunzitsi, muwuzeni mʼbale wanga andigawireko chuma chamasiye.”
14 А Він відказав йому: „Чоловіче, хто поставив над вами Мене за суддю або за поді́льника?“
Yesu anayankha kuti, “Munthu iwe, ndani anandiyika Ine kukhala woweruza kapena wogawa chuma pakati panu?”
15 І промовив до них: „Глядіть, остерігайтеся всякої заже́рливости, — бо життя чоловіка не залежить від достатку маєтку його“.
Kenaka Iye anawawuza kuti, “Chenjerani! Khalani tcheru ndi makhalidwe onse adyera; moyo wa munthu sukhala chifukwa cha kuchuluka kwa zimene ali nazo.”
16 I Він розповів їм притчу, говорячи: „В одного багача гойно нива вродила була́.
Ndipo Iye anawawuza fanizo ili, “Munda wa munthu wina wachuma unabereka kwambiri.
17 І міркував він про себе й казав: „Що́ робити, що не маю куди зібрати пло́дів своїх?“
Iye anaganiza kuti, ‘Ndichite chiyani? Ndilibe malo osungiramo mbewu zanga.’
18 І сказав: „Оце я зроблю́, — порозва́люю клу́ні свої, і просторні́ші поставлю, і позбираю туди пашню́ свою всю та свій достаток.
“Ndipo Iye anati, ichi ndi chimene ndidzachite: Ndidzaphwasula nkhokwe zanga zonse ndi kumanga zokulirapo, ndipo ndidzasungira mʼmenemo mbewu ndi katundu.
19 І скажу́ я душі своїй: „Душе́, маєш багато добра, на багато ро́ків скла́деного. Спочивай, їж та пий, і веселися!“
Ndipo ndidzawuza moyo wanga kuti, ‘Uli nazo zinthu zabwino zambiri zimene zikhalepo zaka zambiri, usapupulume; idya, imwa ndi kukondwera.’”
20 Бог же до нього прорік: „Нерозумний, — но́чі цієї ось душу твою зажадають від тебе, і кому позоста́неться те, що ти був наготовив?“
“Koma Mulungu anati kwa iye, ‘Iwe wopusa! Usiku womwe uno moyo wako udzachotsedwa kwa iwe, ndipo ndi ndani amene adzatenge zimene iwe wadzikonzera?’
21 Так буває і з тим, хто збирає для себе, та не багатіє в Бога“.
“Umu ndi mmene zidzakhalire ndi aliyense amene amadziwunjikira chuma, koma si wachuma pamaso pa Mulungu.”
22 І промовив Він у́чням Своїм: „Через це кажу вам: Не журіться про життя, — що́ ви будете їсти, і ні про тіло, — у що́ ви зодя́гнетеся.
Kenaka Yesu anati kwa ophunzira ake, “Choncho Ine ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu, zimene mudzadya; kapena za thupi lanu, zimene mudzavala.
23 Бо більше від ї́жі життя, а тіло від одягу.
Moyo uposa chakudya, ndi thupi liposa chovala.
24 Погляньте на га́йвороння, що не сіють, не жнуть, нема в них комори, ні клуні, — проте Бог їх годує. Скільки ж більше за птахів ви варті!
Taonani makwangwala: iwo safesa kapena kukolola, alibe nyumba zosungamo zinthu kapena nkhokwe; komabe, Mulungu amawadyetsa. Koposa kotani inu amene ndi ofunikira kuposa mbalame.
25 Хто ж із вас, коли жу́риться, добавити зможе до зросту свого бодай ліктя одно́го?
Ndi ndani wa inu akhoza kuwonjeza ora pa moyo wake chifukwa cha kudandaula?
26 Тож коли ви й найменшого не подола́єте, то чого ж ви про інше клопо́четеся?
Popeza simungathe kuchita kanthu kakangʼono aka, nʼchifukwa chiyani mumadandaula ndi zinazi?
27 Погляньте на ті он ліле́ї, як вони не пряду́ть, ані тчуть. Але́ говорю́ вам, що й сам Соломон у всій славі своїй не вдягався отак, як одна з них!
“Taonani mmene maluwa amakulira. Iwo sagwira ntchito kapena kusoka zovala. Koma Ine ndikuwuzani kuti, ngakhale Solomoni muulemelero wake wonse sanavalepo ngati limodzi la awa.
28 І коли он траву, що сьогодні на полі, а взавтра до пе́чі вкидається, Бог так зодягає, скільки ж краще зодя́гне Він вас, маловірні!
Ngati umu ndi mmene Mulungu amavekera udzu wakuthengo, umene lero ulipo ndipo mawa uponyedwa pa moto, nanga Iye adzakuvekani inu motani. Haa! Inu achikhulupiriro chochepa!
29 І не шукайте, що́ будете їсти, чи що́ будете пити, і не клопочіться.
Ndipo musayike mtima wanu pa zimene mudzadye kapena kumwa; musade nazo nkhawa.
30 Бо всього цього́ й люди світу оцьо́го шукають, Отець же ваш знає, що того́ вам потрібно.
Pakuti anthu akunja amathamanga kufunafuna zinthu zotere, ndipo Atate amadziwa kuti mumazifuna zimenezi.
31 Шукайте отож Його Царства, а це вам додасться!
Koma funafunani ufumu wake, ndipo mudzapatsidwa zonsezi.
32 Не лякайся, черідко мала́, бо сподо́балося Отцю вашому дати вам Царство.
“Musachite mantha, inu kagulu kankhosa, pakuti zinakondweretsa Atate anu kuti akupatseni ufumu.
33 Продавайте достатки свої та ми́лостиню подавайте. Робіть кали́тки собі не старі́ючі, — неви́черпний скарб той у небі, куди не закрадається зло́дій, і міль де не то́чить.
Gulitsani zonse zimene muli nazo, ndipo ndalama zake mupereke kwa osauka. Dzipezereni zikwama zandalama zimene sizidzatha, ndi kudzikundikira chuma chomwe sichidzatha kumwamba, kumene mbala sizingafikeko, ndipo dzimbiri silingawononge.
34 Бо де скарб ваш, там буде й серце ваше!
Popeza kumene kuli chuma chanu, mtima wanunso udzakhala komweko.”
35 Нехай підпере́зані будуть вам сте́гна, а світла ручні́ позасвічувані!
“Khalani okonzekeratu ndipo nyale zanu ziziyaka,
36 І будьте подібними до людей, що очікують пана свого́, коли ве́рнеться він із весі́лля, щоб, як при́йде й застукає, відчинити негайно йому́.
ngati anthu oyembekezera kubwera kwa mbuye wawo kuchokera kuphwando la ukwati, kuti pamene afika ndi kugogoda akhoza nthawi yomweyo kumutsekulira chitseko.
37 Блаженні раби ті, що пан, коли при́йде, то зна́йде, що пильнують вони! Поправді кажу́ вам: підпере́жеться він і їх посадо́вить, і, підійшовши, буде їм послуго́вувати.
Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo pobwera adzawapeze akudikira. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti adzakonzekera kuwatumikira, adzakhala nawo pa tebulo ndipo adzabwera ndi kuwatumikira.
38 І коли при́йде о другій чи при́йде о третій сторо́жі, та зна́йде так само, — блаженні вони!
Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo adzawapeze ali okonzeka, ngakhale iye atabwera pa ora lachiwiri kapena lachitatu usiku.
39 Знайте ж це, що коли б знав госпо́дар, о котрі́й то годині підкра́деться злодій, то він пильнував би, і́ свого б дому не дав підкопати.
Koma zindikirani izi: Ngati mwini nyumba akanadziwa ora limene mbala ibwera, sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
40 Тому будьте готові і ви, — бо при́йде Син Лю́дський тієї години, коли ви не ду́маєте!“
Inunso muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa ora limene simukumuyembekezera Iye.”
41 Озвався ж Петро: „Господи, чи до нас кажеш при́тчу оцю, чи до всіх?“
Petro anafunsa kuti, “Kodi mukunena fanizoli kwa ife, kapena kwa aliyense?”
42 А Господь відказав: „Хто ж тоді вірний і мудрий домоправи́тель, що пан настано́вить його над своїми челя́дниками, щоб давати харч ви́значену своєчасно?
Ambuye anayankha kuti, “Kodi tsono woyangʼanira wokhulupirika ndi wanzeru ndani? Kodi ndi amene mbuye wake wamuyika kukhala oyangʼanira antchito ake kuti aziwapatsa ndalama yachakudya pa nthawi yake yoyenera?
43 Блаженний той раб, що пан його при́йде та зна́йде, що робить він так!
Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera.
44 Поправді кажу́ вам, що над всім маєтком своїм він поставить його.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
45 А коли раб той скаже у серці своїм: „Заба́риться пан мій прийти“, і зачне бити слуг та служниць, їсти та пити та напиватися,
Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo aziganiza mu mtima mwake kuti, ‘Bwana wanga akuchedwa kwambiri kubwera,’ ndipo kenaka ndi kuyamba kumenya antchito aamuna ndi aakazi ndi kudya, kumwa ndi kuledzera.
46 то при́йде раба того пан за дня, якого він не сподівається, і о годині, якої не знає, — і розі́тне його пополовині, і визначить долю йому з невірними!
Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.
47 А раб той, що знав волю свого госпо́даря, але не приготува́в, ані не вчинив згідно волі його, буде тяжко побитий.
“Wantchito amene amadziwa chifuniro cha mbuye wake koma wosakonzeka kapena wosachita chimene mbuye wake akufuna adzakwapulidwa zikwapu zambiri.
48 Хто ж не знав, а вчинив каригі́дне, буде мало він битий. Тож від кожного, кому да́но багато, багато від нього й жадатимуть. А кому багато пові́рено, від того ще більше жадатимуть.
Koma wantchito amene sadziwa koma nʼkuchita zinthu zoyenera chilango, adzakwapulidwa zikwapu zochepa. Aliyense amene anapatsidwa zambiri, adzayenera kubwezanso zambiri; ndipo amene anamusungitsa zambiri, adzamulamula kuti abweze zambirinso.”
49 Я прийшов огонь кинути на землю, — і як Я пра́гну, щоб він уже запала́в!
“Ine ndabwera kudzayatsa moto pa dziko lapansi, ndipo ndikanakonda ukanayaka kale.
50 Я ж маю христитися хрищенням, — і як Я мучуся, поки те спо́вниться!
Koma Ine ndiyenera kubatizidwa, ndipo ndikusautsika mu mtima mpaka utachitika!
51 Чи ви ду́маєте, що прийшов Я мир дати на землю? Ні, кажу вам, але по́діл!
Kodi mukuganiza kuti Ine ndinabwera kudzabweretsa mtendere pa dziko lapansi? Ayi, Ine ndikukuwuzani kuti, ndinabweretsa kugawikana.
52 Віднині бо п'ятеро в домі одно́му поді́лені бу́дуть: троє супроти двох, і двоє супроти трьох.
Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo mʼbanja limodzi mudzakhala anthu asanu ndipo adzawukirana wina ndi mnzake, atatu kuwukira awiri, ndipo awiri kuwukira atatu.
53 Стане ба́тько на сина, а син проти батька, мати проти дочки́, а дочка́ проти матері, свекруха навпроти невістки своєї, а невістка навпроти свекрухи!“
Anthu adzawukirana. Abambo kudzawukira mwana wawo wamwamuna, mwana wawoyo adzawukira abambo ake. Amayi adzawukira mwana wawo wamkazi, mwana wawoyo adzawukira amayi ake. Amayi adzawukira mpongozi wawo wamkazi, mpongoziyo adzawukira amayiwo.”
54 Промовив же Він і до наро́ду: „Як побачите хмару, що з за́ходу суне, то кажете за́раз: Зближається дощ“, — і так і буває.
Iye anati kwa gulu la anthu, “Pamene mukuona mtambo ukukwera kummawa, nthawi yomweyo inu mumati, ‘kugwa mvula,’ ndipo imagwadi.
55 А коли віє вітер півде́нний, то кажете: „Буде спеко́та“, — і́ буває.
Ndipo pamene mphepo yakummwera ikuwomba, inu mumati ‘kutentha’ ndipo kumaterodi.
56 Лицеміри, — лице неба й землі розпізна́ти ви вмієте, чому ж не розпізна́єте часу цього?
Achiphamaso inu! Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a dziko lapansi ndi thambo. Zikutheka bwanji kuti simukudziwa kumasulira kwa nthawi ino?
57 Чого ж і самі по собі ви не судите, що́ справедливе?
“Bwanji simukuzindikira nokha zoyenera kuchita?
58 Бо коли до уря́ду ти йдеш зо своїм супроти́вником, попильнуй з ним зала́годити по дорозі, щоб тебе до судді не потяг він, а суддя щоб прислужникові не віддав тебе, а прислужник щоб не посадив до в'язниці тебе.
Pamene mukupita kwa woweruza ndi amene munalakwirana naye, yesetsani kwambiri kuti muyanjane naye mʼnjiramo, chifukwa mukapanda kutero akhoza kukutengerani ku bwalo la milandu ndipo woweruzayo adzakuperekani kwa woyangʼanira ndende, ndipo woyangʼanira ndendeyo adzakuponyani mʼndende.
59 Поправді кажу́ тобі: Не ви́йдеш ізвідти, поки не віддаси й останнього ше́ляга!“
Ine ndikuwuzani kuti, simudzatulukamo mpaka mutalipira ndalama zonse.”

< Від Луки 12 >