< Ісая 59 >

1 Ото ж бо, Господня рука не скоро́тшала, щоб не помагати, і Його ву́хо не стало тяжки́м, щоб не чути,
Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
2 бо то тільки пере́ступи ваші відді́лювали вас від вашого Бога, і ваші прови́ни хова́ли обличчя Його від вас, щоб Він не почув, —
Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
3 бо ваші долоні запля́млені кров'ю, ваші ж пальці — беззаконням, уста ваші гово́рять неправду, язик ваш белько́че лихе!
Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
4 Немає ніко́го, хто б кликав на суд, і нікого нема, хто судився б попра́вді, — кожен надію кладе на марно́ту й говорить неправду, вагітні́є бідою й поро́джує зло́чин!
Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
5 Виси́джують я́йця гадю́чі та тчуть павути́ння: хто з'їсть з їхніх яєць, помирає, а з розбитого — га́дина ви́йде.
Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
6 Нитки їхні не стануть одежею, і ви́робами своїми вони не покри́ються: їхні діла́ — діла кривди, і в їхніх рука́х — чин наси́льства.
Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
7 Їхні но́ги біжать на лихе, і спішать проливати неви́нну кров, їхні думки́ — думки кривдні, руїна й поги́біль на їхніх доро́гах!
Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
8 Доро́ги споко́ю не знають, і правосу́ддя немає на їхніх стежка́х, — вони покрутили собі свої сте́жки, і кожен, хто нею ступає, не знає споко́ю.
Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
9 Тому́ віддали́лося право від нас, і не сяга́є до нас справедли́вість! чекаємо світла, — та ось темнота́, чекаємо ся́йва — та й у те́мнощах хо́димо!
Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Ми ма́цаємо, мов невидю́щі, за сті́ну, навпо́мацки хо́димо, мов ті безо́кі; спотика́ємося ми опі́вдні, немов би смерко́м, між здоровими ми, як померлі!
Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 Усі ми реве́мо, як ведме́ді, і мов голуби́ ті постійно ворко́чемо, чекаємо права — й немає, спасі́ння — й від нас віддали́лось воно.
Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 Бо помно́жились наші пере́ступи перед Тобою, і свідку́ють на нас гріхи наші, бо з нами пере́ступи наші, а наші прови́ни — ми знаємо їх!
Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 Ми зраджували й говорили неправду на Господа, і повідступа́ли від нашого Бога, казали про у́тиск та ві́дступ, вагітні́ли й виду́мували з свого серця слова́ неправди́ві.
Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 І правосу́ддя наза́д відступи́лося, а справедливість здале́ка стоїть, бо на майда́ні спіткну́лася правда, праведність ж не може прийти, —
Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 і правда зникла, а той, хто від злого відходить, грабо́ваний. І це бачить Господь, — і лихе в Його о́чах, що права нема!
Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
16 І Він бачив, що немає ніко́го, і дивува́всь, що немає засту́пника. Та раме́но Його Йому допомогло́, і Його праведність підпе́рла Його, —
Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
17 і Він зодягну́в праведність, як па́нцер, а шоло́ма спасі́ння — на Свою голову, і зодягну́в шати по́мсти, як одяг, і покри́вся горли́вістю, мов би плаще́м!
Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
18 Надолу́жить Він гнівом Своїм ворога́м згідно з учи́нками їхніми. Своїм супроти́вним — запла́тою, острова́м надолу́жить запла́ту.
Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
19 І будуть боятися Йме́ння Господнього з за́ходу, а слави Його́ — зо схід сонця, бо при́йде, як річка рвучка́, — вітер Господній її пожене́, —
Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
20 і при́йде Викупи́тель Сіо́нові й тим, хто вернувся із про́гріху в Якові, каже Господь.
“Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
21 А Я — ось із ними умова Моя, говорить Господь: Мій Дух, який на тобі, та слова́ Мої, що поклав Я до уст твоїх, не усту́плять вони з твоїх уст, і з уст наща́дків твоїх, і з уст нащадків пото́мства твого́, говорить Господь, відтепе́р й аж навіки!
Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.

< Ісая 59 >