< Ісая 23 >

1 Пророцтво про Тир. Голосіть, кораблі Таршішу, бо Тир поруйно́ваний: без домів і без входу з кіттейського кра́ю. Так було їм відкрито.
Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
2 Замовчіте, мешка́нці надмо́р'я! Сидо́нські купці, які морем пливуть, тебе перепо́внили.
Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
3 І насіння Шіхору у во́дах великих, жни́во Ріки то набу́ток його, і наро́дам він став за торго́вицю.
Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
4 Соро́мся, Сидо́не, сказало бо море, мо́рська тверди́ня, говорячи: я не терпіла з поро́ду та не породила, і не виховала юнакі́в, і дівчат я не ви́кохала.
Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
5 Коли до Єгипту ця звістка прибу́де, вони затремтя́ть, як на зві́стку про Тир.
Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
6 Перейді́ть до Таршішу, ридайте, мешка́нці надмо́р'я!
Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
7 Чи це ваше місто веселе, що поча́ток його з давен-да́вна? Його но́ги несуть його в далечину́ осели́тися.
Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
8 Хто́ це постанови́в був про Тир, що корони давав, що князя́ми бували купці його, а його торговці́ на землі були в шані?
Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
9 Господь Саваот це призна́чив, щоб збезче́стити пиху́ всякій славі, щоб усіх славних землі злегкова́жити.
Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
10 Перейди ти свій край, мов Ріка́, до́чко Таршішу, — вже нема перепо́ни —
Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
11 Свою руку простя́г Він на море, і царства затря́с! Господь про Ханаан наказав, щоб тверди́ню його зруйнува́ти,
Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
12 і сказав: Не будеш ти більше радіти, збезчещена ді́вчино, до́чко Сидону! Уставай, перейди до Кіттіму, але й там ти спочи́нку не ма́тимеш.
Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
13 Це земля ханаанська; на ніщо́ оберну́всь цей наро́д, — Ашшур для пустинних звірі́в влаштува́в був її. Вони збудува́ли тут ба́шти варто́ві, і пала́ци її повалили, у руїну її оберну́ли.
Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
14 Голосіть, кораблі Таршішу, бо спусто́шена ваша тверди́ня!
Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
15 І станеться в день той, Тир буде забутий на сімдесят літ, як дні панува́ння одно́го царя. По семидесяти літах станеться Тирові, як у тій пісні блудни́ці:
Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
16 „Візьми гу́сла, і пройди́ся по місті, забута блудни́це! Приємно заграй, багато пісе́нь заспіва́й, щоб тебе пригада́ли!“
“Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
17 І буде, як сімдесят літ покінчи́ться, згадає про Тира Господь, і зно́ву він братиме плату за блудоді́йство, і чинитиме блуд з усіма царствами світу на поверхні землі.
Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
18 І стане набу́ток його та прибуток його із торгі́влі Господе́ві присвя́ченим. Не буде збиратися він і не буде ховатись, бо набу́ток його буде тим, хто сидітиме перед обличчям Господнім, щоб їсти доси́та та мати розкішну одежу.
Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.

< Ісая 23 >