< До галатів 3 >

1 О, ви нерозумні гала́ти! Хто вас звів не кори́тися правді, вас, яким перед очима Ісус Христос переднакре́слений був, як ніби між вами розп'я́тий?
Agalatiya opusa inu, anakulodzani ndani? Tinamuonetsa poyera pamaso panu Yesu Khristu monga wopachikidwa pa mtanda.
2 Це одне хочу знати від вас: чи ви прийняли́ Духа ділами Зако́ну, чи із про́повіді про віру?
Ine ndikufuna ndiphunzire kuchokera kwa inu chinthu chimodzi ichi: Kodi munalandira Mzimu pochita ntchito za lamulo, kapena pokhulupirira zimene munamva?
3 Чи ж ви аж такі нерозумні? Духом почавши, кінчите́ тепер тілом?
Kani ndinu opusa chotere? Inu mutayamba ndi Mzimu, kodi mukufuna kutsiriza ndi ntchito zathupi?
4 Чи ви так багато терпіли нада́рмо? Коли б тільки надармо!
Kodi munavutika kwambiri pachabe, ngati kunali kwachabedi?
5 Отже, Той, Хто вам Духа дає й чуда чинить між вами, — чи чинить ділами Зако́ну, чи із про́повіді про віру?
Kodi Mulungu amene anakupatsani Mzimu wake ndi kuchita zodabwitsa pakati panu, amachita zimenezi chifukwa mumachita ntchito za lamulo kapena chifukwa mumakhulupirira zimene munamva?
6 Так як Авраа́м „був увірував в Бога, — і це залічено за праведність йому“.
Nʼchimodzimodzinso Abrahamu, “Iye anakhulupirira Mulungu, ndipo Mulungu anamutenga kukhala wolungama.”
7 Тож знайте, що ті, хто від віри, — то сини Авраа́мові.
Tsono zindikirani kuti amene akhulupirira, ndi ana a Abrahamu.
8 І Писа́ння, передбачивши, що вірою Бог виправдає поган, благовісти́ло Авраамові: „Благосло́вляться в тобі всі наро́ди!“
Malemba anaonetseratu kuti Mulungu adzalungamitsa anthu a mitundu ina mwachikhulupiriro, ndipo ananeneratu Uthenga Wabwino kwa Abrahamu kuti, “Mitundu yonse ya anthu idzadalitsika kudzera mwa iwe.”
9 Тому́ ті, хто від віри, бу́дуть поблагосло́влені з вірним Авраамом.
Choncho iwo amene ali ndi chikhulupiriro ndi odalitsidwa pamodzi ndi Abrahamu, munthu wachikhulupiriro.
10 А всі ті, хто на діла Зако́ну покладається, — вони під прокля́ттям. Бо написано: , Прокля́тий усякий, хто не триває в усьому, що написано в книзі Зако́ну, щоб чинити оте!“
Onse amene amadalira ntchito za lamulo ndi otembereredwa, pakuti zalembedwa mʼBuku la Malamulo kuti, “Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita zonse zimene zalembedwa mʼBuku la Malamulo.”
11 А що перед Богом Зако́ном ніхто не виправдується, то це ясно, бо „праведний житиме вірою“.
Chodziwikiratu nʼchakuti palibe amene amalungamitsidwa pamaso pa Mulungu ndi lamulo, chifukwa, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
12 А Зако́н не від віри, але „хто чинитиме те, той житиме ним“.
Koma chikhulupiriro si Malamulo, chifukwa Malemba akuti, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.”
13 Христос відкупив нас від прокля́ття Зако́ну, ставши прокля́ттям за нас, бо написано: „Прокля́тий усякий, хто ви́сить на дереві“,
Khristu anatiwombola ku temberero la lamulo pokhala temberero mʼmalo mwathu, pakuti analemba kuti, “Aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa.”
14 щоб Авраамове благослове́ння в Ісусі Христі поши́рилося на поган, щоб обі́тницю Духа прийняти нам вірою.
Iye anatiwombola ife ndi cholinga chakuti madalitso woperekedwa kwa Abrahamu abwere kwa anthu a mitundu ina kudzera mwa Khristu Yesu, kuti ndi chikhulupiriro tilandire lonjezo la Mzimu.
15 Браття, кажу́ я по-лю́дському: навіть лю́дського затве́рдженого заповіту ніхто не відкидає та до нього не додає.
Abale, ndiloleni ndipereke chitsanzo cha zochitika mʼmoyo wa tsiku ndi tsiku. Pangano likakhazikitsidwa palibe amene angachotsepo kapena kuwonjezerapo, choncho ndi chimodzimodzi pa nkhani iyi.
16 А обі́тниці да́ні були Авраамові й насінню його. Не говориться: „і насінням“, як про багатьох, але як про одно́го: „і Насінню твоєму“, яке є Христос.
Malonjezo awa anaperekedwa kwa Abrahamu ndi kwa mbewu yake. Malemba sakunena kuti, “kwa mbewu zake,” kutanthauza anthu ambiri, koma, “kwa mbewu yako,” kutanthauza munthu mmodzi, amene ndi Khristu.
17 А я кажу́ це, що заповіту, від Бога затве́рдженого, Зако́н, що прийшов по чотириста тридцяти роках, не відкидає, щоб обі́тницю він зруйнував.
Chimene ndikutanthauza ine ndi ichi: Malamulo amene anabwera patatha zaka 430, sangathetse pangano limene linakhazikitsidwa kale ndi Mulungu ndi kuliwononga lonjezolo.
18 Бо коли від Зако́ну спадщина, то вже не з обі́тниці; Авраамові ж Бог дарував із обі́тниці.
Ngati madalitso athu akudalira ntchito za lamulo ndiye kuti madalitsowo sakupatsidwa chifukwa cha lonjezo. Koma Mulungu mwachisomo chake anadalitsa Abrahamu kudzera mu lonjezo.
19 Що ж Зако́н? Він був даний з причини пере́ступів, аж поки при́йде Насіння, якому обі́тниця да́на була́; він учинений був анголами рукою посере́дника.
Nanga tsono cholinga cha lamulo chinali chiyani? Linaperekedwa chifukwa cha zolakwa mpaka itafika mbewu imene lonjezo limanena. Malamulowo anaperekedwa ndi angelo kudzera mwa mʼkhalapakati.
20 Але посере́дник не є для одно́го, Бог же один.
Ngakhale zili chomwecho, mʼkhalapakati sayimira mbali imodzi yokha, koma Mulungu ndi mmodzi.
21 Отож, чи ж Зако́н проти Божих обі́тниць? Зо́всім ні! Якби бо був да́ний Зако́н, щоб він міг оживляти, то праведність справді була б від Зако́ну!
Kodi ndiye kuti lamulo limatsutsana ndi malonjezo a Mulungu? Ayi. Nʼkosatheka! Pakuti ngati tikanapatsidwa malamulo opatsa moyo ndiye kuti mwa lamulo tikanakhala olungama.
22 Та все зачинило Писа́ння під гріх, щоб віруючим була да́на обі́тниця з віри в Ісуса Христа.
Koma Malemba akunenetsa kuti dziko lonse lili mu ulamuliro wauchimo, kuti mwachikhulupiriro mwa Yesu Khristu, chimene chinalonjezedwa chiperekedwe kwa amene akhulupirira.
23 Але поки прийшла віра, під Зако́ном стере́жено нас, за́мкнених до при́ходу віри, що мала об'яви́тись.
Chikhulupiriro ichi chisanabwere, ife tinali mʼndende ya lamulo, otsekeredwa mpaka pamene chikhulupiriro chikanavumbulutsidwa.
24 Тому то Зако́н вихо́вником був до Христа, щоб нам виправдатися вірою.
Choncho lamulo linayikidwa kukhala lotiyangʼanira kuti lititsogolere kwa Khristu kuti tilungamitsidwe mwachikhulupiriro.
25 А як віра прийшла, то вже ми не під вихо́вником.
Tsopano pakuti chikhulupiriro chabwera, ife sitilinso mu ulamuliro wa lamulo.
26 Бо ви всі сини Божі через віру в Христа Ісуса!
Nonse ndinu ana a Mulungu kudzera mʼchikhulupiriro mwa Khristu Yesu,
27 Бо ви всі, що в Христа охристилися, у Христа зодягну́лися!
pakuti nonse amene munalumikizana ndi Khristu mu ubatizo munavala Khristu.
28 Нема юдея, ні грека, нема раба, ані вільного, нема чоловічої статі, ані жіночої, — бо всі ви один у Христі Ісусі!
Palibe Myuda kapena Mgriki, kapolo kapena mfulu, mwamuna kapena mkazi, pakuti nonse ndinu amodzi mwa Khristu Yesu.
29 А коли ви Христові, то ви Авраамове насіння й за обі́тницею спадкоємці.
Ngati inu muli ake a Khristu, ndiye kuti ndinu mbewu ya Abrahamu, ndi olowamʼmalo molingana ndi lonjezo.

< До галатів 3 >