< До галатів 1 >

1 Апо́стол Павло́, поставлений ні від людей, ані від чоловіка, але́ від Ісуса Христа й Бога Отця, що з мертвих Його воскресив,
Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
2 і присутня зо мною вся браття, до Церко́в галаті́йських:
pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
3 благодать вам і мир від Бога, Отця нашого, і Господа Ісуса Христа,
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
4 що за наші гріхи дав Само́го Себе, щоб від злого сучасного віку нас визволити, за волею Бога й Отця нашого, — (aiōn g165)
Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn g165)
5 Йому слава на віки́ вічні, амі́нь! (aiōn g165)
Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
6 Дивуюся я, що ви так скоро відхи́люєтесь від того, хто покликав Христовою благодаттю вас, на іншу Єва́нгелю,
Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
7 що не інша вона, але деякі є, що вас непокоять, і хочуть перевернути Христову Єва́нгелію.
umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
8 Але якби й ми або а́нгол із неба зачав благовісти́ти вам не те, що ми вам благовісти́ли, — нехай буде прокля́тий!
Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
9 Як ми перше казали, і тепер знов кажу́: коли хто вам не те благовісти́ть, що ви прийняли́, — нехай буде прокля́тий!
Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
10 Бо тепер чи я в людей шукаю призна́ння чи в Бога? Чи лю́дям дба́ю я догоджа́ти? Бо коли б догоджав я ще лю́дям, я не був би рабо́м Христовим.
Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
11 Звіщаю ж вам, браття, що Єва́нгелія, яку я благовісти́в, — вона не від людей.
Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
12 Бо я не прийняв, ні навчився її від люди́ни, але об'явленням Ісуса Христа.
Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
13 Чули бо ви про моє поступо́вання перше в юдействі, що Божу Церкву жорсто́ко я переслідував та руйнував її.
Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
14 І я перевищував в юдействі багатьох своїх рове́сників роду мого, бувши запе́клим прихильником моїх отці́вських переда́нь.
Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
15 Коли ж Бог, що вибрав мене від утро́би матері моєї і покликав благода́ттю Своєю, уподобав
Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
16 виявити мною Сина Свого, щоб благовістив я Його між поганами, — я не радився зараз із тілом та кров'ю,
kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
17 і не відправився в Єрусалим до апо́столів, що передо мною були, а пішов я в Ара́бію, і зно́ву вернувся в Дама́ск.
Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
18 По трьох ро́ках пото́му пішов я в Єрусалим побачити Ки́фу, і в нього пробув днів із п'ятнадцять.
Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
19 А іншого з апо́столів я не бачив, крім Якова, брата Господнього.
Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
20 А що вам пишу́, ось кажу́ перед Богом, що я не обманюю!
Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
21 Пото́му пішов я до си́рських та кілікі́йських країн.
Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
22 Церква́м же Христовим в Юдеї я знаний не був особисто, -
Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
23 тільки чули вони, що той, що колись переслідував їх, благовісти́ть тепер віру, що колись руйнував був її.
Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
24 І сла́вили Бога вони через мене!
Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.

< До галатів 1 >