< Єзекіїль 9 >

1 І кликнув Він в уші мої сильним голосом, кажучи: „Набли́зьте кара́телів міста, і кожен нехай має в своїй руці свої нищівні́ знаря́ддя“.
Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.”
2 І ось прийшли шість чоловіка з дороги горі́шньої брами, що зве́рнена на пі́вніч, і кожен мав у своїй руці свої знаря́ддя розбива́ння, а серед них один чоловік був одя́гнений в льняне́, а пи́сарський калама́р був при сте́гнах його. І вони прийшли, і стали при мідяно́му же́ртівнику.
Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.
3 А слава Ізраїлевого Бога підняла́ся з-над Херуви́ма, що була над ним, до порога дому. І закли́кав Він чоловіка, одя́гненого в льняне́, що пи́сарський калама́р був при сте́гнах його.
Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake
4 І сказав Господь до нього: „Перейди сере́диною міста, сере́диною Єрусалиму, і зроби зна́ка на чо́лах людей, що зідхають та стогнуть над усіма́ тими гидо́тами, що робляться в його сере́дині“.
ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”
5 А до інших Він сказав при мені: „Ходіть за ним у місті, і вбивайте; нехай ваше око не має милосердя, і ви не зми́луйтеся!
Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo.
6 Старо́го, юнака, і ді́вчину, і дітей та жінок позабива́йте доще́нту, а до кожної люди́ни, що на ній цей знак, не піді́йдете; а зачне́те від Моєї святині“. І зачали́ вони від тих старих людей, що були перед домом.
Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
7 І сказав Він до них: „Занечи́стіть цей дім, і напо́вніть подві́р'я тру́пами, і вийдіть!“І вони повихо́дили, і вбивали в місті.
Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse.
8 І сталося, коли вони вбивали, то я позостався, і впав на своє обличчя, і кли́кав та казав: „О Господи, Боже, чи Ти ви́губиш увесь останок Ізраїлів, виливаючи гнів Свій на Єрусалим?“
Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”
9 І сказав Він до мене: „Провина дому Ізраїля й Юди дуже-дуже велика, і земля напо́внена душогу́бствами, а місто повне кривди. Бо вони кажуть: Господь покинув цей Край, і Господь не бачить.
Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’
10 І також Я, — не змилосе́рдиться око Моє, і не змилуюсь Я, їхню доро́гу Я дам на їхню голову!“
Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”
11 І ось чоловік, одя́гнений в льняне́, що калама́р був при сте́гнах його, приніс відповідь, кажучи: „Я зробив, як мені наказав Ти!“
Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”

< Єзекіїль 9 >