< Екклезіяст 6 >

1 Є ще зло, що я бачив під сонцем, і багато його між людьми́:
Ine ndinaona choyipa china pansi pano, ndipo chimasautsa anthu kwambiri:
2 Ось люди́на, що Бог їй багатство дає, і маєтки та славу, і недостатку ні в чо́му, чого́ зажадає, не чує вона для своєї душі, але Бог не дав вла́ди їй те спожива́ти, — бо чужа люди́на те поїсть: Це марно́та й неду́га тяжка́!
Mulungu amapereka chuma, zinthu ndi ulemu kwa munthu, kotero kuti munthuyo sasowa kanthu kalikonse kamene akukalakalaka, koma Mulungu samulola kuti adyerere zinthuzo, ndipo mʼmalo mwake amadyerera ndi mlendo. Izi ndi zopandapake, ndi zoyipa kwambiri.
3 Якби сотню дітей наплоди́в чоловік, і прожи́в пречисле́нні літа́, і дні віку його були довгі, але не наси́тилась добрим душа його, а до того не мав би й належного по́хорону, то кажу́: недоно́скові краще від нього!
Ngakhale munthu atabereka ana 100 ndi kukhala ndi moyo zaka zambiri; komatu ngakhale atakhala zaka zambiri chotani, ngati iye sangadyerere chuma chake ndi kuyikidwa mʼmanda mwaulemu, ine ndikuti mtayo umamuposa iyeyo.
4 Бо в марно́ті прийшов він, і в те́мряву йде, і в те́мряві сховане буде іме́ння його, —
Mtayo umangopita pachabe ndipo umapita mu mdima, ndipo mu mdimamo dzina lake limayiwalika.
5 ані сонця не бачив він, ані пізнав: йому́ спокійніше від того!
Ngakhale kuti mtayowo sunaone dzuwa kapena kudziwa kanthu kalikonse, koma umapumula kuposa munthu uja,
6 А коли б він жив дві́чі по тисячі літ, та не бачив добра́, — то хіба не до місця одно́го все йде?
ngakhale munthuyo atakhala ndi moyo zaka 2,000, koma ndi kulephera kudyerera chuma chake. Kodi onsewa sapita malo amodzi?
7 Увесь труд люди́ни — для рота її, і пожада́ння її не випо́внюються.
Ntchito yonse ya munthu imathera pakamwa pake, komatu iye sakhutitsidwa ndi pangʼono pomwe.
8 Бо що більшого має мудрець, ніж безглуздий, що має убогий над те, що перед живими уміє ходити?
Kodi munthu wanzeru amaposa motani chitsiru? Kodi munthu wosauka amapindula chiyani podziwa kukhala bwino pamaso pa anthu ena?
9 Краще бачити очима, аніж мандрува́ти жада́ннями, — і тако́ж це марно́та та ло́влення вітру...
Kuli bwino kumangoona zinthu ndi maso kusiyana ndi kumangozilakalaka mu mtima. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
10 Що було́, тому йме́ння його вже нада́не давно, і відо́ме, що він чоловік, і він не може правува́тися з сильнішим від нього,
Chilichonse chimene chilipo anachitchula kale dzina, za mmene munthu alili nʼzodziwika; sangathe kutsutsana ndi munthu amene ali wamphamvu kupambana iyeyo.
11 бо багато рече́й, що марно́ту примно́жують, але яка ко́ристь від них для люди́ни?
Mawu akachuluka zopandapake zimachulukanso, nanga munthu zimamupindulira chiyani?
12 Бо хто знає, що́ добре люди́ні в житті, за небагатьох днів марно́го життя її, які пробуває вона, немов тінь? Та й що́ хто розкаже люди́ні, що́ буде під сонцем по ній?
Pakuti ndani amene amadziwa chomwe ndi chabwino pa moyo wa munthu, pakuti moyo wake ndi wa masiku ochepa ndi opandapake, umangopitira ngati mthunzi. Ndani amene angamufotokozere zimene zidzachitika pansi pano iye atapita?

< Екклезіяст 6 >