< Дії 4 >

1 А коли промовляли вони до наро́ду оце́, до них приступили священики, і вла́да сторожі храму й саддукеї,
Pamene Petro ndi Yohane amayankhula ndi anthu, kunabwera ansembe, mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndiponso Asaduki.
2 обурюючись, що навчають наро́д та звіщають в Ісусі воскресі́ння з мертвих.
Iwo anakhumudwa kwambiri chifukwa atumwiwo amaphunzitsa anthu ndi kumalalikira za kuuka kwa akufa mwa Yesu.
3 І руки наклали на них, і до в'язниці всадили до ра́нку, бо вже вечір настав був.
Iwo anagwira Petro ndi Yohane, popeza kunali kutada, anawayika mʼndende mpaka mmawa mwake.
4 І багато-хто з тих, хто слухав слово, увірували; число ж мужів таки́х було тисяч із п'ять.
Koma anthu ambiri amene anamva uthenga anakhulupirira, ndipo chiwerengero cha anthu chinakwana 5,000.
5 І сталось, що ра́нком зібралися в Єрусалимі начальники їхні, і старші та книжники,
Mmawa mwake olamulira, akulu ndi aphunzitsi a malamulo anasonkhana mu Yerusalemu.
6 і Анна первосвященик, і Кайя́фа, і Іван, і Олександер, і скільки було їх із роду первосвященичого.
Panali Anasi, Mkulu wa ansembe, Kayafa, Yohane ndi Alekisandro ndi ana a banja la mkulu wa ansembe.
7 І, поставивши їх посере́дині, запиталися: „Якою ви силою чи яким ви ім'я́м те робили?“
Iwo anayimiritsa Petro ndi Yohane patsogolo pawo nayamba kuwafunsa kuti, “Kodi munachita zimenezi ndi mphamvu yanji kapena mʼdzina la yani?”
8 Тоді Петро, переповнений Духом Святим, промовив до них: „Начальники люду та старши́ни Ізраїлеві!
Petro wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anawawuza kuti, “Inu olamulira ndi akulu!
9 Як сьогодні беруть нас на до́пит про те доброді́йство недужій люди́ні, як вона вздоро́влена, -
Ngati ife tikufunsidwa lero chifukwa cha ntchito yabwino imene yachitika pa munthu wolumala miyendo ndi mmene iye anachiritsidwira,
10 нехай буде відо́мо всім вам, і всім лю́дям Ізраїлевим, що Ім'я́м Ісуса Христа Назаряни́на, що Його розп'яли́ ви, та Його воскресив Бог із мертвих, — Ним поставлений він перед вами здоровий!
tsono dziwani izi inu ndi aliyense mu Israeli: munthuyu akuyima pamaso panu, wochiritsidwa kwathunthu, ndi chifukwa cha dzina la Yesu Khristu wa ku Nazareti amene munamupachika koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa.
11 Він „камінь, що ви, будівни́чі, відкинули, але каменем став Він нарі́жним!“
Iye ndi “‘Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana, umenewo wasanduka mwala wa pa ngodya!’
12 І нема ні в кім іншім спасі́ння. Бо під небом нема іншого Йме́ння, даного людям, що ним би спасти́ся ми мали“.
Chipulumutso sichipezeka mwa wina aliyense; pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo limene lapatsidwa kwa anthu limene tiyenera kupulumutsidwa nalo.”
13 А бачивши сміли́вість Петра та Івана, і спостерігши, що то люди оби́два невчені та про́сті, дивувалися, і пізнали їх, що вони з Ісусом були́.
Ataona kulimba mtima kwa Petro ndi Yohane ndi kuzindikira kuti anali osaphunzira, anthu wamba, anadabwa kwambiri ndipo anazindikira kuti anthuwa anakhala pamodzi ndi Yesu.
14 Та бачивши, що вздоро́влений чоловік стоїть з ними, нічого навпро́ти сказати не могли.
Koma popeza iwo amamuona munthu amene anachiritsidwa atayima pamodzi ndi iwo, palibe chimene akananena.
15 І, звелівши їм вийти із синедріо́ну, зачали радитися між собою,
Chifukwa chake anawalamula kuti atuluke mʼbwalo la milandu ndipo akulu abwalowo anayamba kukambirana.
16 говорячи: „Що́ робити нам із цими людьми́? Бож усім ме́шканцям Єрусалиму відо́мо, що вчинили вони явне чудо, і не можемо того заперечити.
Iwo anafunsana kuti, “Kodi anthuwa tichite nawo chiyani? Pakuti aliyense okhala mu Yerusalemu akudziwa kuti achita chodabwitsachi, ndipo ife sitingathe kukana.
17 Та щоб більш не поши́рювалось це в наро́ді, то з погрозою заборонімо їм, щоб ніко́му з людей вони не говорили про Це Ім'я́“.
Koma kuti mbiriyi isapitirire kuwanda pakati pa anthu, ife tiwachenjeze anthu amenewa kuti asayankhulenso kwa wina aliyense mʼdzina la Yesu.”
18 І, закли́кавши їх, наказали їм не говорити, і взагалі не навчати про Ісусове Йме́ння.
Pamenepo anawayitananso ndipo anawalamula kuti asayankhule kapena kuphunzitsa konse mʼdzina la Yesu.
19 І відповіли́ їм Петро та Іван, та й сказали: „Розсудіть, чи це справедливе було б перед Богом, щоб слухатись вас більш, як Бога?
Koma Petro ndi Yohane anayankha kuti, “Weruzani nokha ngati nʼkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu.
20 Бо не можемо ми не казати про те, що́ ми бачили й чули!“
Ife sitingaleke kuyankhula za zimene tinaziona ndi kuzimva.”
21 А вони пригрози́ли їм ще, і відпустили їх, не знайшовши нічо́го, щоб їх покарати, через людей, бо всі сла́вили Бога за те, що сталось.
Atawonjeza kuwaopseza anawamasula. Sanathe kugwirizana njira yowalangira, chifukwa anthu onse amayamika Mulungu chifukwa cha zimene zinachitika.
22 Бо ро́ків більш сорока мав той чоловік, що на нім відбулося це чудо вздоро́влення.
Ndipo munthu amene anachiritsidwayo anali ndi zaka makumi anayi.
23 Коли ж їх відпустили, вони до своїх прибули́ й сповістили, про що́ первосвященики й старші до них говорили.
Atamasulidwa Petro ndi Yohane anapita kwa anzawo ndipo anawafotokozera zonse zimene akulu a ansembe ndi akulu anawawuza.
24 Вони ж, вислухавши, однодушно свій голос до Бога підне́сли й промовили: „Владико, що небо, і землю, і море, і все, що в них є, Ти створив!
Anthu atamva zimenezi anafuwula ndi mtima umodzi napemphera kwa Mulungu. Iwo anati, “Ambuye wolamulira zonse, Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi nyanja ndiponso zonse zili mʼmenemo.
25 Ти уста́ми Давида, Свого слуги́, отця нашого, сказав Духом Святим: „Чого люди бунтуються, а наро́ди задумують ма́рне?
Inu munayankhula mwa Mzimu Woyera kudzera pakamwa pa Davide kholo lathu, mtumiki wanu kuti, “‘Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu, ndipo akonzekera kuchita zopandapake?
26 Повстають царі зе́мні, і збираються старші докупи на Господа та на Христа Його“.
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.’
27 Бо справді зібралися в місці оцім проти Отрока Святого Твого Ісуса, що Його намастив Ти, Ірод та По́нтій Пилат із поганами та з наро́дом Ізраїлевим,
Zoonadi, Herode ndi Pontiyo Pilato anasonkhana pamodzi ndi amitundu ndiponso Aisraeli, mu mzinda muno, kupanga zolimbana ndi mtumiki wanu woyera Yesu, amene Inu munamudzoza.
28 учинити оте, що рука Твоя й воля Твоя наперед встановили були, щоб збуло́ся.
Iwo anachita zimene munakonzeratu mwachifuniro chanu ndi mphamvu yanu kuti zichitike.
29 І тепер споглянь, Господи, на їхні погрози, і дай Своїм рабам із повною сміли́вістю слово Твоє повіда́ти,
Tsopano, Ambuye taonani kuti atiopseza, tithandizeni ife atumiki anu, kuti tiyankhule mawu anu molimba mtima.
30 коли руку Свою простягатимеш Ти на вздоро́влення, і щоб знаме́на та чуда чинились Ім'я́м Твого Святого Отрока Ісуса“.
Tambasulani dzanja lanu kuchiritsa anthu ndipo kuti, zizindikiro zodabwitsa zichitike mʼdzina la mtumiki wanu woyera Yesu.”
31 Як вони ж помолились, затряслося те місце, де зібрались були, і перепо́внилися всі Святим Духом, — і зачали говори́ти Слово Боже з сміли́вістю!
Iwo atatha kupemphera, malo amene anasonkhanapo anagwedezeka. Ndipo iwo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo anayankhula Mawu a Mulungu molimba mtima.
32 А люди, що ввірували, мали серце одне й одну душу, і жоден із них не вважав що з маєтку свого́ за своє, але в них усе спі́льним було́.
Okhulupirira onse anali a mtima umodzi, ndi maganizo amodzi. Palibe munthu amene amati zomwe anali nazo zinali zake zokha, koma amagawana chilichonse chimene anali nacho.
33 І апо́столи з вели́кою силою свідчили про воскресіння Ісуса Господа, і благода́ть велика на всіх них була!
Atumwi anapitirira kuchitira umboni mwa mphamvu zakuuka kwa Ambuye Yesu, ndipo pa iwo panali chisomo chochuluka.
34 Бо жоден із них не терпів недостачі: бо, хто мав поле чи дім, продавали, і заплату за про́даж прино́сили,
Panalibe anthu osowa kanthu pakati pawo. Pakuti amene anali ndi malo, kapena nyumba amagulitsa ndi kubweretsa ndalamazo
35 та й клали в ногах у апо́столів, — і роздавалося кожному, хто потре́бу в чім мав.
ndi kuzipereka kwa atumwi, ndipo zimagawidwa kwa aliyense amene anali ndi chosowa.
36 Так, Йо́сип, що Варна́вою — що в перекладі є „син потіхи“— був про́званий від апо́столів, Левит, родом кі́прянин,
Yosefe, wa fuko la Levi, wochokera ku Kupro amene atumwi anamutcha Barnaba, kutanthauza kuti mwana wachilimbikitso,
37 мавши поле, продав, а гроші приніс, та й поклав у ногах у апо́столів.
anagulitsa munda wake ndipo anadzapereka ndalamazo kwa atumwi.

< Дії 4 >