< Дії 26 >

1 А Агріппа сказав до Павла: „Дозволяємо тобі говорити про себе само́го“. Павло тоді простягнув руку, і промовив у своїй обороні:
Ndipo Agripa anawuza Paulo kuti, “Takulola kuti unene mawu ako.” Paulo anatambasula dzanja lake nayamba kudziteteza kuti,
2 „О ца́рю Агріппо! Уважаю себе за щасливого, що сьогодні я перед тобою боронитися маю з усьо́го, у чім мене винуватять юдеї,
“Mfumu Agripa ine ndikudziyesa wa mwayi kuyima pamaso panu lero lino ndi kudziteteza, kutsutsa zonse zimene Ayuda andinenera,
3 особливо ж тому́, що ти знаєш усі юдейські звича́ї та супере́чки. Тому я прошу́ мене вислухати терпля́че.
ndipo makamaka chifukwa inu mukudziwa bwino miyambo yonse ya Chiyuda ndiponso zonse zimene amatsutsana. Nʼchifukwa chake ndikukupemphani kuti mundimvetsere moleza mtima.
4 А життя моє зма́лку, що споча́тку точилося в Єрусалимі серед наро́ду мого, знають усі юдеї,
“Ayuda onse akudziwa za moyo wanga mmene ndakhalira kuyambira ndili mwana, kuchokera pachiyambi cha moyo wanga mʼdziko lathu ndiponso mu Yerusalemu.
5 які відають зда́вна мене, аби тільки схотіли засві́дчити, — що я жив фарисеєм за найдокладнішою сектою нашої віри.
Iwo akundidziwa kuyambira kalekale ndipo angathe kuchitira umboni kuti ndakhala ndili Mfarisi moyo wanga wonse, mmodzi wa gulu limene limasamala chipembedzo chathu koposa.
6 І тепер я стою отут су́джений за надію обі́тниці, що Бог дав ії нашим отцям,
Ndipo tsopano ndikuyimbidwa mlandu lero chifukwa cha chiyembekezo changa pa zimene Mulungu analonjeza makolo athu.
7 а її викона́ння чекають побачити наші дванадцять племен, слу́жачи Богові безперестанно вдень та вночі. За цю надію, о ца́рю, мене винуватять юдеї!
Ili ndi lonjezo limene mafuko athu khumi ndi awiri akuyembekezera kuti likwaniritsidwe pamene akupembedza Mulungu molimbika usana ndi usiku. Wolemekezeka Mfumu, nʼchifukwa cha chiyembekezo chimenechi Ayuda kuti akundiyimba mlandu.
8 Чому ви вважаєте за неймовірне, що Бог воскрешає померлих?
Nʼchifukwa chiyani ena a inu mukuganiza kuti nʼkosatheka kuti Mulungu aukitse akufa?
9 Правда, ду́мав був я, що мені нале́жить чинити багато ворожого проти Ймення Ісуса Назаряни́на,
“Inenso ndimaganiza kuti ndimayenera kuchita zinthu zambiri pofuna kuthana ndi dzina la Yesu wa ku Nazareti.
10 що я в Єрусалимі й робив, і багато кого зо святих до в'язниць я замкнув, як отримав був вла́ду від первосвящеників; а як їх убивали, я голос давав проти них.
Ndipo izi ndi zimene ndinazichita ku Yerusalemu. Ndi ulamuliro wa akulu a ansembe, ine ndinayika mʼndende oyera mtima ambiri, ndipo pamene amaphedwa, ine ndimavomereza.
11 І часто по всіх синагогах караючи їх, до богозневаги примушував я, а лютуючи ве́льми на них, переслідував їх навіть по закордонних містах.
Nthawi zambiri ndinkapita mʼsunagoge iliyonse kuti alangidwe, ndipo ndinayesera kuwakakamiza kuti achitire chipongwe Mulungu. Mu mkwiyo wangawo, ndimapita ngakhale ku mizinda yachilendo kuti ndikawazunze.
12 Коли в цих справах я йшов до Дамаску зо вла́дою та припору́ченням первосвящеників,
“Pa ulendo wina wotere, ndikupita ku Damasiko ndi mphamvu ndi ulamuliro ochokera kwa akulu a ansembe,
13 то опі́вдні, о ца́рю, на дорозі побачив я світло із неба, ясніше від світлости сонця, що ося́яло мене та тих, хто разом зо мною йшов!
Wolemekezeka Mfumu, nthawi ya masana pamene ndimayenda pa msewu, ndinaona kuwala kuchokera kumwamba koposa kuwala kwa dzuwa kutandizungulira ine pamodzi ndi anzangawo.
14 І як ми всі повалились на землю, я голос почув, що мені говорив єврейською мовою: „Савле, Савле, — чому ти Мене переслідуєш? Трудно тобі бити ногою колю́чку!“
Tonse tinagwa pansi ndipo ndinamva mawu mʼChihebri akuti, ‘Saulo, Saulo chifukwa chiyani ukundizunza Ine? Nʼkovuta kulimbikira mtunda wopanda madzi.’”
15 А я запитав: „Хто Ти, Господи?“А Він відказав: „Я Ісус, що Його переслідуєш ти.
Ndipo ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu, amene iwe ukumuzunza.
16 Але підведи́ся, і стань на ноги свої. Бо на те Я з'явився тобі, щоб тебе вчинити слугою та свідком того, що ти бачив та що Я відкрию тобі.
Tsopano dzuka ndipo imirira. Ine ndaonekera kwa iwe kuti ndikusankhe kuti ukhale mtumiki ndiponso mboni ya zimene waziona za Ine ndiponso zimene ndidzakuonetsa.
17 Визволяю тебе від твого наро́ду та від поган, до яких Я тебе посилаю, —
Ine ndidzakulanditsa mʼmanja mwa anthu a mtundu wako ndiponso mwa anthu a mitundu ina. Ine ndikukutuma kwa iwo,
18 відкрити їм очі, щоб вони наверну́лись від те́мряви в світло та від сатани́ної вла́ди до Бога, щоб вірою в Мене отримати їм дарува́ння гріхів і насліддя з освяченими“.
kuti ukatsekule maso awo kuti atembenuke mtima kuchoka ku mdima ndi kulowa mʼkuwala, kuchoka ku mphamvu za Satana ndi kupita kwa Mulungu, kuti alandire chikhululukiro cha machimo awo ndi kukhala mʼgulu la amene akuyeretsedwa chifukwa chokhulupirira Ine.
19 Через це я, о ца́рю Агріппо, не був супротивний видінню небесному,
“Nʼchifukwa chake Mfumu Agripa, sindinakane kumvera masomphenya wochokera kumwamba.
20 але ме́шканцям перше Дамаску, потім Єрусалиму й усякого кра́ю юдейського та поганам я проповідував, щоб пока́ялися й наверну́лись до Бога, і чинили діла, гі́дні покая́ння.
Kuyambira kwa anthu a ku Damasiko, a ku Yerusalemu, a ku Yudeya konse ndi kwa anthu a mitundu inanso, ndinalalikira kuti akuyenera kulapa ndi kutembenukira kwa Mulungu ndikuti aonetse kulapa kwawo mwa ntchito zawo.
21 Через це юдеї в святині схопи́ли мене та й хотіли роздерти.
Ichi nʼchifukwa chake Ayuda anandigwira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nafuna kundipha.
22 Але, поміч від Бога одержавши, я стою́ аж до дня сьогоднішнього та свідкую мало́му й великому, нічого не розповідаючи, окрім того, що сказали Пророки й Мойсей, що статися має, —
Koma Mulungu wakhala akundithandiza mpaka lero lino. Ine ndayima pano kuti ndichitire umboni kwa anthu onse otchuka ndi anthu wamba. Ine sindikunena zina zowonjezera koma zimene Aneneri ndi Mose ananena kuti zidzachitika.
23 що має Христос постраждати, що Він, як перший воскреснувши з мертвих, проповідувати буде світло народові й поганам!“
Iwo ananena kuti Khristu adzamva zowawa ndipo popeza Iye adzakhala woyamba kuuka kwa akufa, adzalalikira za kuwunika kwa anthu a mtundu wake ndiponso kwa anthu a mitundu ina.”
24 Коли ж він боронився отак, то Фест проказав гучни́м голосом: „Дурієш ти, Павле! Велика наука доводить тебе до нерозуму“!
Paulo akudziteteza, Festo anakweza mawu nati, “Wazungulira mutu Paulo! Kuphunzira kwako kwakuchititsa misala.”
25 А Павло: „Не дурію — сказав, — о Фесте достойний, але провіщаю слова правди та щирого розуму.
Paulo anayankha nati, “Wolemekezeka Festo, sindine wozungulira mutu. Zimene ndikunena ndi zoona ndiponso za nzeru.
26 Цар бо знає про це, — до нього з відвагою я й промовляю. Бо не гада́ю я, щоб із цього щобудь схова́лось від нього, — бо не в за́кутку ді́ялось це.
Mfumu ikuzidziwa bwino zinthu izi, ndipo ndikuyankhula momasuka kwa iyo. Ine ndikukhulupirira kuti palibe kanthu nʼkamodzi komwe kamene sukukadziwa, chifukwa izi sizinachike mseri.
27 Чи віруєш, ца́рю Агріппо, Пророкам? Я знаю, що віруєш“.
Mfumu Agripa, kodi mumakhulupirira mawu a aneneri? Ine ndikudziwa kuti mumakhulupirira.”
28 Агріппа ж Павлові: „Ти малощо не намовляєш мене, щоб я став християни́ном“.
Kenaka Agripa anati kwa Paulo, “Kodi ukuganiza kuti mʼkanthawi kochepa kotere ungandikope kuti ndikhale Mkhristu?”
29 А Павло: „Благав би я Бога, щоб чи мало, чи багато, — не тільки но ти, але й усі, хто чує сьогодні мене, зробились такими, як і я, крім оцих ланцюгів“.
Paulo anayankha kuti, “Ngakhale kanthawi kochepa kapena nthawi yayitali, ine ndikupempha kwa Mulungu kuti osati inu nokha koma aliyense amene akundimva lero lino akhale monga ine, kupatulapo maunyolo okhawa.”
30 І встав цар та намісник, і Верні́ка та ті, хто з ними сидів.
Mfumu inayimirira pamodzi ndi bwanamkubwa ndi Bernisi ndiponso anthu onse amene anakhala nawo pamodzi.
31 І на́бік вони відійшли, і розмовляли один до одно́го й казали: „Нічого, ва́ртого смерти або ланцюгів, чоловік цей не робить!“
Inatuluka mʼchipindamo, ndipo pamene imayankhula inati, “Munthu uyu sanachite kanthu koyenera kuphedwa kapena kumangidwa.”
32 Агріппа ж до Феста сказав: „Міг би бути відпу́щений цей чоловік, якби не відкликавсь був до ке́саря“
Agripa anati kwa Festo, “Munthu uyu akanamasulidwa akanakhala kuti sanapemphe zokaonekera kwa Kaisara.”

< Дії 26 >