< Дії 19 >

1 І сталося, що коли Аполло́с перебував у Кори́нті, то Павло, перейшовши горі́шні країни, прибув до Ефе́су, і деяких учнів знайшов,
Apolo ali ku Korinto, Paulo anadutsa mʼmayiko a ku mtunda ndipo anafika ku Efeso. Kumeneko anapeza ophunzira ena.
2 та й спитав їх: „Чи ви Духа Святого одержали, як увірували?“А вони відказали йому: „Та ми навіть не чули, чи є Дух Святий!“
Iye anawafunsa kuti, “Kodi munalandira Mzimu Woyera pamene munakhulupirira?” Iwo anayankha kuti, “Ayi, ife sitinamvepo kuti kuli Mzimu Woyera.”
3 І він запитав: „Тож у що́ ви христились?“Вони ж відказали: В Іванове хрищення“.
Tsono Paulo anawafunsa kuti, “Nanga munabatizidwa ndi ubatizo wotani?” Iwo anati, “Ubatizo wa Yohane.”
4 І промовив Павло: „Таж Іван христив хрищенням на покая́ння, говорячи лю́дям, щоб вірили в Того, Хто при́йде по ньому, цебто в Ісуса“.
Paulo anati, “Ubatizo wa Yohane unali wa kutembenuka mtima. Iye anawuza anthu kuti akhulupirire amene amabwera, ameneyo ndiye Yesu.”
5 Як почули ж ́, то христились вони в Ім'я́ Господа Ісуса.
Atamva zimenezi, anabatizidwa mʼdzina la Ambuye Yesu.
6 А коли Павло руки на них покла́в, то зійшов на них Дух Святий, — і різними мовами стали вони промовляти та пророкувати!
Pamene Paulo anawasanjika manja, Mzimu Woyera anadza pa iwo ndipo anayankhula mʼmalilime ndipo ananenera.
7 А всіх їх було́ чоловіка з двана́дцять.
Anthu onsewo analipo khumi ndi awiri.
8 А до синагоги ввійшовши, промовляв він відважно, три місяці про Боже Царство навчаючи та переконуючи.
Paulo analowa mʼsunagoge ndipo anayankhula molimba mtima kwa miyezi itatu, kuwatsutsa mowakopa za ufumu wa Mulungu.
9 А коли опиралися дехто й не вірували, і дорогу Господню лихосло́вили перед наро́дом, то він їх покинув і виділив учнів, і щодня проповідував у школі одно́го Тира́на.
Koma ena anawumitsa mitima; anakana kukhulupirira ndipo ananyoza Njirayo pa gulu la anthu. Kotero Paulo anawasiya. Iye anatenga ophunzirawo ndipo amakambirana tsiku ndi tsiku mʼsukulu ya Turano.
10 Це ж два роки продовжувалось, так що всі, хто замешкував в Азії, юдеї та ге́ллени, слухали слово про Господа.
Izi zinachitika kwa zaka ziwiri, kotero kuti Ayuda onse ndi Agriki amene amakhala ku Asiya anamva Mawu a Ambuye.
11 І Бог чуда чинив надзвича́йні руками Павловими,
Mulungu anachita zodabwitsa zapadera kudzera mwa Paulo.
12 так що навіть хустки́ й пояси́ з його тіла прино́сили хворим, — і хвороби їх кидали, і ду́хи лукаві вихо́дили з них.
Kotero kuti mipango yopukutira thukuta ndi yovala pogwira ntchito, zomwe zinakhudza thupi la Paulo amapita nazo kwa odwala ndipo amachiritsidwa ndiponso mizimu yoyipa mwa iwo imatuluka.
13 Дехто ж із мандрівни́х ворожби́тів юдейських зачали́ закликати Ім'я́ Господа Ісуса над тими, хто мав злих духів, проказуючи: Заклинаємо вас Ісусом, Якого Павло́ проповідує!“
Ayuda ena amene ankayendayenda kutulutsa mizimu yoyipa anayesa kugwiritsa ntchito dzina la Ambuye Yesu pa amene anali ndi ziwanda. Iwo popemphera amati, “Ine ndikulamulira utuluke, mʼdzina la Yesu amene Paulo amamulalikira.”
14 Це ж робили якісь сім синів юдейського первосвященика Ске́ви.
Amene ankachita zimenezi anali ana asanu ndi awiri a Skeva, mkulu wa ansembe wa Chiyuda.
15 Відповів же злий дух і сказав їм: „Я знаю Ісуса, і знаю Павла, а ви хто такі?“
Tsiku lina mzimu woyipa unawayankha kuti, “Yesu ndimamudziwa ndiponso Paulo ndimamudziwa, nanga inu ndinu ndani?”
16 І ско́чив на них чоловік, що в ньому злий дух був, і, перемігші обох, поду́жав їх так, що втекли вони з дому нагі́ та пора́нені.
Pamenepo munthu amene anali ndi mzimu woyipa anawalumphira nawagwira onse. Iye anawamenya kwambiri, kotero kuti anathawa mʼnyumbamo ali maliseche, akutuluka magazi.
17 І це стало відо́ме юдеям та ге́лленам, усім, що в Ефесі замешкують, — і о́страх напав на всіх їх, і сла́вилося Ім'я́ Господа Ісуса.
Ayuda ndi Agriki okhala ku Efeso atamva zimenezi, anachita mantha, ndipo anthu anachitira ulemu dzina la Ambuye Yesu koposa.
18 І багато-хто з тих, що ввірували, прихо́дили, визнаваючи та відкриваючи вчинки свої.
Ambiri a iwo amene tsopano anakhulupirira anafika ndi kuvomereza poyera ntchito zawo zoyipa.
19 І багато-хто з тих, що займалися ча́рами, позно́сили книги свої та й перед усіма́ попалили. І злічили ціну́ їх, і вийшло на срібло п'ятдесят тисяч драхм.
Ambiri amene amachita za matsenga anasonkhanitsa mabuku awo pamodzi nawatentha pamaso pa anthu onse. Atawonkhetsa mtengo wa mabukuwo, unakwanira ndalama zasiliva 50,000.
20 Так могуче росло та зміцнялося Вожеє Слово!
Kotero Mawu a Ambuye anapitirira kufalikira ndipo anagwira ntchito mwamphamvu.
21 А як спо́внилось це, Павло в Дусі задумав перейти Македо́нію та Ахаю, та й удатись у Єрусалим, говорячи: „Як побу́ду я там, то треба мені й Рим побачити“.
Zonsezi zitachitika Paulo anatsimikiza zopita ku Yerusalemu kudzera ku Makedoniya ndi ku Akaya. Iye anati, “Kuchokera kumeneko, ndiyenera kukafikanso ku Roma.”
22 Тож він послав у Македо́нію двох із тих, що служили йому, Тимофі́я й Ера́ста, а сам позостався якийсь час ув Азії.
Iye anatuma anthu awiri amene amamuthandiza, Timoteyo ndi Erasto ku Makedoniya, pamene iye anakhalabe ku Asiya kwa kanthawi.
23 І ро́зрух чималий був стався там ча́су того за Господню дорогу.
Pa nthawi yomweyo panachitika chipolowe chachikulu chifukwa cha Njira ya Ambuye.
24 Бо один золота́р, Дмитро на ім'я́, що робив срібляні́ Артемі́дині храмки, та ремісникам заробі́ток чималий давав,
Mmisiri wantchito zasiliva, dzina lake Demetriyo, amene amapanga mafano asiliva a Atemi ankabweretsa phindu lalikulu kwa amisiri a kumeneko.
25 згромадив він їх і ще інших подібних робі́тників, та й промовив: „Ви знаєте, мужі, що з цього ремесла́ заробі́ток ми маємо.
Iye anasonkhanitsa pamodzi amisiriwo, pamodzinso ndi anthu ena ogwira ntchito yomweyo ndipo anati, “Anthu inu, mukudziwa kuti ife timapeza chuma chathu kuchokera pa ntchito imeneyi.
26 І ви бачите й чуєте, що не тільки в Ефе́сі, але мало не в усій Азії — цей Павло збаламу́тив і відвернув багате́нно наро́ду, говорячи, ніби то не боги, що руками поро́блені.
Ndipo inu mukuona ndi kumva kuti munthu uyu Paulo wakopa ndi kusokoneza anthu ambiri a ku Efeso ndiponso pafupifupi dziko lonse la Asiya. Iye akunena kuti milungu yopangidwa ndi anthu si milungu ayi.
27 І не тільки оце нам загрожує, що при́йде зайняття в упадок, а й храм богині великої Артемі́ди в ніщо́ зарахується, і буде зруйнована й ве́лич тієї, що шанує її ціла Азія та цілий світ“.
Choopsa ndi chakuti sikungowonongeka kwa ntchito yathu yokha ayi, komanso kuti nyumba ya mulungu wamkulu wamkazi Atemi idzanyozedwa ndipo mulungu wamkazi weniweniyo amene amapembedzedwa ku Asiya konse ndi dziko lapansi, ukulu wake udzawonongekanso.”
28 Почувши ж оце, вони перепо́внились гнівом, та й стали кричати, говорячи: „Артемі́да ефе́ська велика!“
Atamva zimenezi, anakwiya kwambiri ndipo anayamba kufuwula kuti, “Wamkulu ndi Atemi.”
29 І місто напо́внилось за́колотом. І кинулися однодушно до видо́вища, схопи́вши Павло́вих супу́тників — Гая та Ариста́рха, македо́нян.
Nthawi yomweyo mu mzinda wonse munabuka chipolowe. Anthu anagwira Gayo ndi Aristariko, anzake a Paulo a ku Makedoniya, ndipo anathamangira nawo ku bwalo la masewero.
30 Як Павло ж хотів у наро́д увійти, то учні його не пустили.
Paulo anafuna kulowa pakati pa gulu la anthu, koma ophunzira anamuletsa.
31 Також дехто з азі́йських начальників, що були йому при́ятелі, послали до нього й просили, щоб він не вдава́всь на видо́вище.
Ngakhale olamulira ena aderalo, amene anali abwenzi a Paulo, anatumiza uthenga kumuletsa kuti asayesere kulowa mʼbwalomo.
32 І кожен що інше кричав, бо збори бурхли́ві були, і багате́нно з них навіть не знали, чого ради зібралися.
Munali chisokonezo mʼbwalomo pakuti ena amafuwula zina, enanso zina. Anthu ambiri sanadziwe ngakhale chomwe anasonkhanira.
33 А з наро́ду взяли Олександра, бо юдеї його висували. І Олекса́ндер дав знака рукою, і хотів ви́правдатися перед наро́дом.
Ayuda anamukankhira Alekisandro kutsogolo, ndipo ena anafuwula kumulangiza iye. Iye anatambasula dzanja kuti anthu akhale chete kuti afotokozere anthu nkhaniyo.
34 А коли розпізнали, що юде́янин він, то злилися всі в один голос, і годин зо дві гукали: „Артеміда ефеська велика!“
Koma pamene anthuwo anazindikira kuti ndi Myuda, onse pamodzi kwa maora awiri anafuwula kuti, “Wamkulu ndi Atemi wa ku Efeso!”
35 А як писар міськи́й заспоко́їв наро́д, то промовив: „Мужі ефеські, яка ж то люди́на не знає, що місто Ефес — то храмо́вий догля́дач Артеміди великої й її образу, упалого з неба?
Mlembi wa mzindawo anakhazikitsa bata gulu la anthuwo ndipo anati, “Anthu a ku Efeso, kodi ndani pa dziko lonse lapansi amene sadziwa kuti mzinda wa Efeso umayangʼanira nyumba ya mulungu wamkulu Atemi ndi fanizo lake, limene linagwa kuchokera kumwamba?
36 Коли ж цьому перечити не можна, то потрібно вам бути спокійними, і не роби́ти необачно нічо́го.
Chifukwa chake popeza zinthu izi palibe amene angazikane, inu mukuyenera kukhala chete osachita kanthu kalikonse mofulumira.
37 А ви ж привели́ цих людей, що ані святокрадці, ані вашої богині не знева́жили.
Inu mwabweretsa anthu awa pano, ngakhale kuti iwo sanabe mʼnyumba zathu zamapemphero kapena kunenera chipongwe mulungu wathu wamkazi.
38 Отож, як Дмитро та його ремісники мають справу на ко́го, то суди є на ринку й проконсули, — один о́дного хай позивають.
Ngati tsono Demetriyo ndi amisiri anzake ali ndi nkhani ndi munthu wina aliyense, mabwalo a milandu alipo, oweruza aliponso. Akhoza kukapereka nkhaniyo kwa oweruza milanduwo.
39 А коли чогось іншого допомина́єтеся, то те вирішиться на зако́ннім зібра́нні.
Ngati mukufuna kubweretsa kanthu kali konse, ziyenera kukatsimikizidwa ndi bwalo lovomerezeka.
40 Бо ось є небезпека, що нас за сьогоднішній ро́зрух оскаржити можуть, і немає жа́дної причини, якою могли б виправдати це зборище“.
Monga mmene zililimu, ife titha kuzengedwa mlandu woyambitsa chipolowe chifukwa cha zimene zachitika lerozi. Motero ife sitingathe kufotokoza za chipolowechi popeza palibe nkhani yake.”
41 І, промовивши це, розпустив він громаду.
Iye atatha kunena zimenezi anawuza gulu la anthulo kuti libalalike.

< Дії 19 >