< Дії 15 >

1 А дехто, що з Юдеї прийшли, навчали братів: „Якщо ви не обріжетеся за звича́єм Мойсеєвим, то спастися не можете“.
Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.”
2 Коли ж суперечка повстала й чимале змага́ння в Павла́ та в Варнави з ними, то постановили, щоб Павло́ та Варнава, та дехто ще інший із них, пішли в справі цій до апо́столів й старших у Єрусалим.
Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi.
3 Тож вони, відпроваджені Церквою, ішли через Фінікі́ю та Самарі́ю, розповідаючи про поганське наве́рнення, і радість велику чинили всім браттям.
Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse.
4 Коли ж в Єрусалим прибули́ вони, були прийняті Церквою, та апо́столами, та старши́ми, і вони розповіли́, як багато вчинив Бог із ними.
Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.
5 Але дехто, що вві́рували з фарисейської партії, устали й сказали, що потрібно поганів обрі́зувати й наказати, щоб Зако́на Мойсеєвого берегли.
Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”
6 І зібрались апо́столи й старші, щоб розглянути справу оцю.
Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi.
7 Як велике ж змага́ння повстало, Петро встав і промовив до них: „Мужі-браття, ви знаєте, що з давнішніх днів вибрав Бог поміж нами мене́, щоб погани почули слово Єва́нгелії через у́ста мої, та й увірували.
Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira.
8 І засві́дчив їм Бог Серцезнавець, давши їм Духа Святого, як і нам,
Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife.
9 і між нами та ними різни́ці Він жодної не вчинив, очистивши вірою їхні серця.
Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro.
10 Отож, чого Бога тепер споку́шуєте, щоб учням на шию покласти ярмо́, якого ані наші отці, ані ми не здола́ли поне́сти?
Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza?
11 Та ми віруємо, що спасе́мося благода́ттю Господа Ісуса так само, як і вони“.
Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”
12 І вся громада замовкла, і слухали пильно Варнаву й Павла, що розповідали, які то знаме́на та чу́да вчинив через них Бог між поганами!
Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo.
13 Як замовкли ж вони, то Яків озвався й промовив: „Мужі-браття, послухайте також мене.
Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani.
14 Си́мон ось розповів, як зглянувся Бог від поча́тку, щоб вибрати люд із поганів для Йме́ння Свого.
Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake.
15 І пророчі слова́ з цим погоджуються, як написано:
Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,
16 „Пото́му вернуся, і відбуду́ю Давидову ски́нію занепалу, і відбудую руїни її, і наново поставлю її,
“‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso,
17 щоб шукали Господа люди зосталі та всі наро́ди, над якими Ім'я́ Моє кликано, — говорить Господь, що чинить це все!
kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye, ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa, akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi
18 Господе́ві відвіку відо́мі всі вчинки Його“. (aiōn g165)
zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn g165)
19 Тому ду́маю я, щоб не турбувати поган, що до Бога наверта́ються,
“Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu.
20 але написати до них, щоб стри́мувались від занечи́щення і́дольського, та від блу́ду, і задушени́ни, і від кро́ви.
Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi.
21 Бо своїх проповідників має Мойсей по містах здавенда́вна, і щосуботи читають його в синагогах“.
Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”
22 Тоді постановили апо́столи й старші з ці́лою Церквою вибрати му́жів із них, і послати до Антіохі́ї з Павло́м та Варна́вою Юду, що зветься Варса́вва, і Силу, му́жів проводирів між братами,
Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale,
23 написавши свої́ми руками оце́: „Апостоли й старші брати до братів, що з поган в Антіохі́ї, і Си́рії, і Кілікі́ї: Вітаємо вас!
kuti akapereke kalata yonena kuti, Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu, Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya: Tikupereka moni.
24 Через те, що ми чули, що деякі з вас, яким ми того не дору́чували, стурбували наукою вас, і захитали вам душі,
Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani.
25 то ми постановили однодушно, зібравшися, щоб о́браних мужів послати до вас із коханими нашими — Варнавою та Павло́м,
Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba,
26 людьми́ тими, що ду́ші свої віддали́ за Ім'я́ Господа нашого Ісуса Христа.
anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
27 Тож ми Юду та Силу послали, що вияснять усно те саме.
Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba.
28 Бо зво́лилось Духові Святому і нам, — тягару́ вже нія́кого не наклада́ти на вас, окрім цього необхідного:
Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi:
29 стри́муватися від ідольських жертов та крови, і задушени́ни, та від блу́ду. Оберегаючися від того, ви зробите добре. Бувайте здорові!“
Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi. Tsalani bwino.
30 Посланці́ ж прийшли в Антіохі́ю, і, зібравши наро́д, доручили листа.
Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo.
31 А перечитавши, раділи з поті́шення того.
Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso.
32 А Юда та Сила, самі бувши пророками, частим словом підбадьо́рували та зміцняли братів.
Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo.
33 А як перебули́ вони там якийсь час, то брати їх відпустили з миром до тих, хто їх вислав.
Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma.
34 Але Сила схотів лиши́тися там, а Юда вернувся до Єрусалиму.
Koma Sila anasankha kuti akhale komweko.
35 А Павло з Варнавою в Антіохії жили́, навчаючи та благові́стячи ра́зом із іншими багатьома́ Слово Господнє.
Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.
36 А по декількох днях промовив Павло́ до Варнави: „Ходімо знов, і відвідаймо наших братів у кожному місті, де ми провіщали Слово Господнє, — як вони пробува́ють“.
Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.”
37 А Варнава хотів був узяти з собою Івана, що зва́ний був Ма́рком.
Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo.
38 Та Павло́ вважав за потрібне не брати з собою того, хто від них відлучився з Памфілії, та з ними на працю не йшов.
Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito.
39 І повстала незгода, і розлучились вони між собою. Тож Варнава взяв Ма́рка, і попли́нув до Кіпру.
Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro.
40 А Павло вибрав Силу й пішов, Божій благода́ті братами доручений.
Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka.
41 І проходив він Си́рію та Кілікі́ю, Церкви́ зміцнюючи.
Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.

< Дії 15 >