< 3 Івана 1 >

1 Ста́рець — улю́бленому Гаєві, якого я направду люблю́.
Ndine mkulu wampingo, kulembera: Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.
2 Улю́блений, — я молюся, щоб добре вело́ся в усьому тобі, і щоб був ти здоровий, як добре веде́ться душі твоїй.
Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu.
3 Бо я дуже зрадів, як прийшли були браття, і засві́дчили правду твою, як ти живеш у правді.
Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi.
4 Я не маю більшої радости від цієї, щоб чути, що діти мої живуть у правді.
Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.
5 Улю́блений, — вірно ти чи́ниш, як що робиш для братті та для чужи́нців, —
Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo.
6 вони про любов твою свідчили Церкві; добре ти зробиш, як їх ви́провадиш, як достойно для Бога,
Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu.
7 бо вийшли вони ради Йме́ння Його, нічого не взявши від поган.
Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira.
8 Отож, ми повинні приймати таких, щоб бути співробі́тниками правді.
Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.
9 Я до Церкви писав був, але Діотре́ф, що любить бути першим у них, нас не приймає.
Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera.
10 Тому́ то, коли я прийду́, то згадаю про вчинки його, що їх ро́бить, словами лихими обмовля́ючи нас. І він тим не задово́льнюється, — а й сам не приймає братів, і тим, що бажають приймати, боронить, і виго́нить із Церкви.
Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.
11 Улюблений, — не робися подібним до лихо́го, а до доброго: доброчинець від Бога, а злочинець Бога не бачив.
Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu.
12 Про Димитрія сві́дчили всі й сама правда. І сві́дчимо й ми, а ви знаєте, що свідчення наше правдиве.
Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.
13 Багато хотів я писати, та не хочу писати до тебе чорнилом та очерети́нкою,
Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata.
14 але маю надію побачити тебе незаба́ром, і говорити уста́ми до уст. Мир тобі! Друзі вітають тебе. Привітай друзів пойменно! Амі́нь.
Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso. Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.

< 3 Івана 1 >