< 2 до коринтян 7 >

1 Отож, мої любі, мавши ці обі́тниці, очистьмо себе від усякої не́чисти тіла та духа, — і творімо святиню у Божім страху́!
Abwenzi okondedwa, popeza tili ndi malonjezo amenewa, tiyeni tidziyeretse, kusiyana nazo zilizonse zimene zikhoza kudetsa thupi ndi mzimu, ndipo tiyesetse kukhala oyera mtima poopa Mulungu.
2 Дайте місце для нас! Ми ніко́го не скривдили, ніко́го не зіпсували, нікого не ошука́ли!
Mutipatse malo mʼmitima mwanu. Ife sitinalakwire munthu aliyense, kapena kuyipitsa munthu aliyense, kapena kumuchenjerera munthu aliyense.
3 Говорю́ не на о́суд, бо я перед тим був сказав, що ви в серцях наших, щоб нам із вами чи померти чи жити.
Sindikunena izi kuti mupezeke olakwa. Ndinanena kale kuti ife timakuganizirani kwambiri kotero kuti tili pamodzi, ngakhale tikhale moyo kapena timwalire.
4 У мене велика сміли́вість до вас, велика мені похвала́ з вас, я повний потіхи, збагачаюся радістю при всякому нашому горі.
Ndimakukhulupirirani kwambiri ndipo ndimakunyadirani kwambiri. Ndikulimbikitsidwa kwambiri; mʼmasautso athu onse, chimwemwe changa chilibe malire.
5 Бо коли ми прийшли в Македо́нію, тіло наше не мало спочинку нія́кого, у всьому бідуючи: назовні — бої, страхіття — всере́дині.
Pakuti titafika ku Makedoniya, sitinapume nʼkomwe, koma tinavutitsidwa mbali zonse. Kunja kunali mikangano, ndipo mʼmitima mwathu munali mantha.
6 Але Бог, що тішить прини́жених, потішив нас при́ходом Тита,
Koma Mulungu, amene amatonthoza mtima wopsinjika, anatitonthoza mtima ndi kufika kwa Tito,
7 і не тільки його прибуття́м, а й поті́шенням, що ним він потішився з вас, коли розповідав нам про вашу журбу́, про ваш смуток, про вашу горли́вість до мене, так що я більше тішився.
sikubwera kwake kokhako, komanso mawu achilimbikitso amene analandira kuchokera kwa inu. Iye anatiwuza kuti mukufuna kundiona, zachisoni chanu chachikulu, ndi kudzipereka kwanu kwa ine, motero chimwemwe changa chinachuluka kuposa kale.
8 Коли я й засмутив вас листом, то не каюся, хоч і каявся був, бо бачу, що той лист засмутив вас, хоч і часово.
Ngakhale kalata yanga ija inakupwetekani mtima, sindikudandaula kuti ndinalemberanji. Ngakhale zinandikhudza, ndikudziwa kuti kalata yanga inakupwetekani, koma kwa kanthawi kochepa.
9 Я радію тепер не тому́, що ви засмутились, а що ви засмутилися на покая́ння, бо ви засмутились для Бога, щоб ні в чо́му не мати втрати від нас.
Koma tsopano ndine wokondwa, osati chifukwa chakuti kalatayo inakupwetekani, koma chifukwa chakuti chisoni chanu chinakuthandizani kutembenuka mtima. Pakuti munamva chisoni monga mmene Mulungu amafunira, choncho simunapwetekedwe mwanjira iliyonse.
10 Бо смуток для Бога чинить каяття́ на спасі́ння, а про нього не жалуємо, а смуток світськи́й — чинить смерть.
Chisoni chimene Mulungu amafuna chimabweretsa kutembenuka mtima komwe kumabweretsa chipulumutso, ndipo sichikhumudwitsa. Koma chisoni cha dziko lapansi chimabweretsa imfa.
11 Бо ось саме це, що ви засмутились для Бога, яку пильність велику воно вам зробило, яку оборону, яке обурення, який страх, яке бажа́ння, яку горливість, яку по́мсту! Ви в усім показали, що чисті ви в справі.
Taonani zimene chisoni chimene Mulungu amafuna chatulutsa mwa inu. Chatulutsa khama lalikulu, chakuthandizani kuti mudzikonze nokha, chakukwiyitsani kwambiri, komanso chakupatsani mantha aakulu. Chakuchititsani kuti mufune kundiona ine, mwakhudzidwa kwambiri ndipo mukufuna kuonetsetsa kuti chilungamo chachitikadi. Pa nkhani yonseyi, mwaonetsadi kuti ndinu osalakwa.
12 А коли я й писав вам, то не через того, хто кри́вдить, і не через покри́вдженого, а щоб виявилася для вас наша пильність про вас перед Богом.
Choncho ngakhale ndinakulemberani kalata ija, sindinayilembe ndi chifukwa cha amene analakwayo kapena wolakwiridwa, koma ndinayilemba kuti inuyo muone kudzipereka kwanu kwa ife pamaso a Mulungu.
13 Тому́ то потіхою вашою вті́шились ми, а ще більше зраділи ми радістю Тита, що ви всі заспоко́їли духа його.
Zimenezi zatilimbikitsa kwambiri. Kuwonjezera pa zotilimbikitsazo, tinakondwa kwambiri poona chisangalalo cha Tito, chifukwa nonsenu munamuthandiza kukhazikitsa mtima wake pansi.
14 Бо коли я про вас йому чим похвалився, то не осоро́мився; але як ми вам говорили все правду, так і наша хвала́ перед Титом правдива була́!
Ndinamuwuza kuti ndimakunyadirani, ndipo simunandichititse manyazi. Koma monga zonse zimene tinakuwuzani zinali zoona, tsono zomwe ndinawuza Tito zokunyadirani zinali zoona.
15 І серце його прихильніше до вас, коли згадує він про покору всіх вас, як його прийняли́ ви були зо стра́хом і тремті́нням.
Ndipo chikondi chake pa inu nʼchachikulu kwambiri akakumbukira kuti nonse munali omvera, munamulandira ndi mantha ndi kunjenjemera.
16 Отож, тішуся я, що мо́жу покластись у всьому на вас!
Ndine wokondwa kuti ndingathe kukukhulupirirani pa zonse.

< 2 до коринтян 7 >