< 2 до коринтян 4 >

1 Ось тому́, мавши за милосердям Божим таке служі́ння, ми не тратимо відваги,
Choncho popeza mwachifundo cha Mulungu tili ndi utumiki uwu, sititaya mtima.
2 але ми відреклися тайного со́рому, не хо́дячи в хитрості та не перекручуючи Божого Слова, але з'я́вленням правди доручуємо себе кожному сумлінню лю́дському перед Богом.
Koma ife takaniratu njira zonse zachinsinsi ndi zochititsa manyazi. Sitichita kanthu mwachinyengo kapena mopotoza Mawu a Mulungu. Mʼmalo mwake, timayankhula choonadi poyera pamaso pa Mulungu, kufuna kuti aliyense ativomereze mu mtima mwake.
3 Коли ж наша Єва́нгелія й закрита, то закрита для тих, хто гине, —
Koma ngakhale uthenga wathu wabwino utakhala wophimbika, ndi wophimbika kwa okhawo amene akutayika.
4 для невіруючих, яким бог цього віку засліпив розум, щоб для них не зася́яло світло Єва́нгелії слави Христа, а Він — образ Божий. (aiōn g165)
Mulungu wa dziko lapansi anachititsa khungu anthu osakhulupirira, kuti asathe kuona kuwala kwa Uthenga Wabwino umene umaonetsa ulemerero wa Khristu, amene ndi chifaniziro cha Mulungu. (aiōn g165)
5 Бо ми не себе самих проповідуємо, але Христа Ісуса, Господа, ми ж самі — раби ваші ради Ісуса.
Choncho sitilalikira za ife eni, koma Yesu Khristu monga Ambuye, ife ndife atumiki anu chifukwa cha Yesu.
6 Бо Бог, що звелів був світлу зася́яти з те́мряви, у серцях наших зася́яв, щоб просвітити нам знання́ слави Божої — в Особі Христовій.
Pakuti Mulungu amene anati, “Kuwala kuwunike kuchokera mu mdima,” Iyeyo ndiye anawunikira mʼmitima mwathu kutipatsa kuwala kuti tidziwe ulemerero wa Mulungu umene ukuoneka pa nkhope ya Yesu Khristu.
7 А ми маємо скарб цей у посу́динах гли́няних, щоб ве́лич сили була Божа, а не від нас.
Koma tili ndi chuma ichi mʼmbiya zadothi, kusonyeza kuti mphamvu yoposayi, imachokera kwa Mulungu osati kwa ife.
8 У всьому нас тиснуть, та не поти́снені ми; ми в важки́х обставинах, але не впадаємо в ро́зпач.
Tapanikizika kwambiri mbali zonse koma osaphwanyika; tathedwa nzeru koma osataya mtima;
9 Переслідують нас, але ми не полишені; ми повалені, та не погублені.
tazunzidwa, koma osasiyidwa; takanthidwa, koma osawonongeka.
10 Ми за́всіди носимо в тілі ме́ртвість Ісусову, щоб з'явилося в нашому тілі й життя Ісусове.
Nthawi zonse tikuyenda nayo imfa ya Yesu mʼthupi mwathu, kuti moyo wake Yesu uwonekenso mʼthupi mwathu.
11 Бо за́всіди нас, що живемо́, віддають на смерть за Ісуса, щоб з'явилось Ісусове в нашому смертельному тілі.
Pakuti nthawi zonse, ngakhale tili ndi moyo, tikuperekedwa ku imfa chifukwa cha Yesu, kuti moyo wake wa Yesu uwonekenso mʼmatupi mwathu amene amafa.
12 Тому́ то смерть діє в нас, а життя — у вас.
Choncho imfa ikugwira ntchito mwa ife, koma moyo ukugwira ntchito mwa inu.
13 Та мавши того ж духа віри, за написаним: „Вірував я, через те говорив“, і ми віруємо, тому то й говоримо,
Kwalembedwa kuti, “Ndinakhulupirira; nʼchifukwa chake ndinayankhula.” Popeza ife tili ndi mtima womwewo wokhulupirira, ifenso timakhulupirira ndi kuyankhula,
14 знавши, що Той, Хто воскресив Господа Ісуса, воскреси́ть з Ісусом і нас, і поставить із вами.
chifukwa timadziwa kuti amene anaukitsa Ambuye Yesu kwa akufa adzatiukitsanso ife pamodzi ndi Yesu, natipereka ife ndi inu pamaso pake.
15 Усе бо для вас, щоб благода́ть, розмножена через багатьох, збагати́ла подяку на Божу славу.
Zonsezi nʼkuti inu mupindule, kuti chisomochi chifikire anthu ochuluka kwambiri, amenenso adzathokoza mochuluka kwambiri ndi kupereka ulemerero kwa Mulungu.
16 Через те ми відваги не тратимо, бо хоч ни́щиться зовнішній наш чоловік, зате день-у-день відновля́ється внутрішній.
Nʼchifukwa chake ife sititaya mtima. Ngakhale thupi lathu likunka lifowokerafowokera, koma mʼkatimu tikulimbikitsidwa mwatsopano tsiku ndi tsiku.
17 Бо тепе́рішнє легке наше горе достачає для нас у безмірнім багатстві славу вічної ваги, (aiōnios g166)
Pakuti masautso athu ndi opepuka ndi a kanthawi, koma akutitengera ulemerero wamuyaya umene ndi wopambana kwambiri. (aiōnios g166)
18 коли ми не дивимося на види́ме, а на невиди́ме. Бо види́ме - дочасне, невиди́ме ж - вічне! (aiōnios g166)
Motero sitiyangʼana zinthu zimene ndi zooneka ndi maso, koma zinthu zimene ndi zosaoneka. Pakuti zimene zimaoneka ndi zosakhalitsa, koma zimene sizioneka ndi zamuyaya. (aiōnios g166)

< 2 до коринтян 4 >