< 2 до коринтян 12 >

1 Не кори́сно хвалитись мені, бо я прийду́ до видінь і об'я́влень Господніх.
Ndiyenera kupitiriza kudzitamandira. Ngakhale palibe choti ndipindule, ndipitiriza kufotokoza za masomphenya ndi mavumbulutso ochokera kwa Ambuye.
2 Я знаю чоловіка в Христі, що він чотирна́дцять ро́ків тому — чи в тілі, не знаю, чи без тіла, не знаю, знає Бог — був узятий до третього неба.
Ndikudziwa munthu mwa Khristu amene zaka khumi ndi zinayi zapitazo anatengedwa kupita kumwamba kwachitatu. Sindikudziwa ngati zinachitika ali mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu.
3 І чоловіка я знаю такого, — чи в тілі, чи без тіла, не знаю, знає Бог, —
Ndipo ndikumudziwa munthu ameneyu. Sindikudziwa ngati zinachitika mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu.
4 що до ра́ю був узятий, і чув він слова́ невимо́вні, що не можна люди́ні їх висловити.
Munthuyu anatengedwa kupita ku paradizo. Ndipo anamva zinthu zosatheka kuneneka, zinthu zimene munthu saloledwa kunena.
5 Отаким похвалюся, а собою хвалитись не буду, — хіба тільки своїми не́мочами.
Ndidzatamanda za munthu ngati ameneyu, koma sindidzadzitamandira ine mwini kupatula za kufowoka kwanga.
6 Бо коли я захо́чу хвалитись, то безумний не бу́ду, бо правду казатиму; але стримуюсь я, щоб про мене хто більш не поду́мав, ніж бачить у мені або чує від мене.
Ngakhale nditafuna kudzitamandira, sindingakhale chitsiru, chifukwa ndikunena zoona. Koma ndimapewa kuti pasapezeke munthu wondiganizira moposera chimene ndili chifukwa cha zimene ndimachita kapena kuyankhula,
7 А щоб я через пребагато об'я́влень не велича́вся, то да́но мені в тіло колючку, — посланця́ сатани, щоб бив в обличчя мене, щоб я не велича́вся.
kapena chifukwa cha mavumbulutso aakulu kuposa awa. Choncho, kuti ndisadzitukumule, ndinayikidwa minga mʼthupi langa, wamthenga wa Satana, kuti adzindizunza.
8 Про нього три ра́зи благав я Господа, щоб він відступився від мене.
Katatu konse ndinapempha Ambuye kuti andichotsere.
9 І сказав Він мені: „До́сить тобі Моєї благодаті, — бо сила Моя здійснюється в немочі“. Отож, краще я буду хвалитись своїми не́мочами, щоб сила Христова вселилася в мене.
Koma anandiwuza kuti, “Chisomo changa ndi chokukwanira, pakuti mphamvu zanga zimaoneka kwathunthu mwa munthu wofowoka.” Choncho ndidzadzitamandira mokondwera chifukwa cha zofowoka zanga, kuti mʼkutero mphamvu ya Khristu ikhale pa ine.
10 Тому любо мені перебува́ти в неду́гах, у при́кростях, у бі́дах, у переслідуваннях, в утисках через Христа. Коли бо я слаби́й, тоді я сильни́й.
Tsono, chifukwa cha Khristu, ndimakondwera pamene ndili wofowoka, pamene akundinyoza, pamene ndikumva zowawa, ndi pamene akundizunza ndi kundisautsa. Pakuti pamene ndili wofowoka ndiye kuti ndili wamphamvu.
11 Хва́лячися, я став нерозумний, — до того мене ви примусили. Бо хвалити мене мали б ви, — бо ні в чо́му я не залиши́вся позад від найперших апо́столів, хоч я й ніщо.
Ndadzisandutsa wopusa, koma inu mwandichititsa zimenezi. Ndinu amene munayenera kundichitira umboni. Ngakhale kuti sindine kanthu, koma sindine wochepetsetsa kwa “atumwi apamwamba” aja.
12 А ознаки апо́стола виявилися між вами в усякім терпінні, у знаме́нах і чу́дах та в силах.
Ndinapirira pokuonetserani zizindikiro za mtumwi weniweni, pochita pakati panu zizindikiro, zodabwitsa ndi ntchito zamphamvu.
13 Що бо є, що ним ви пони́зилися більше від інших Церков? Хіба те, що я сам тягаре́м вам не був? Даруйте мені цю провину!
Kodi inu munaoneka ochepa motani ku mipingo ina, kupatula kuti sindinali cholemetsa kwa inu? Mundikhululukire cholakwa chimenechi!
14 Ось утре́тє готовий прийти я до вас, і не буду для вас тягаре́м, — не шукаю бо вашого я, тільки вас. Не діти повинні збирати маєток батька́м, але дітям батьки́.
Ndakonzeka tsopano kudzakuyenderani kachitatu, ndipo sindidzakhala cholemetsa kwa inu chifukwa ndikungofuna inuyo osati zinthu zanu. Pakuti ana sasamalira makolo koma makolo ndiwo asamalira ana.
15 Я ж з охотою ви́трачуся й себе ви́трачу за душі ваші, хоч що більше люблю́ вас, то менше я лю́блений.
Motero ndidzakondwera kukupatsani zanga zonse zimene ndili nazo ndi kudziperekanso ine mwini chifukwa cha inu. Kodi ine ndikamakukondani kwambiri chotere, inuyo mudzandikonda pangʼono?
16 Та нехай буде так, — тягара́ я на вас не поклав, але, бувши хитрий, я лукавством від вас брав.
Ena mwa inu amavomereza kuti sindinali cholemetsa. Komabe ena amaganiza kuti ndine wochenjera, ndipo ndinakuchenjererani.
17 Чи я використо́вував вас через когось із тих, кого́ до вас посилав?
Kodi ndinakudyerani masuku pamutu kudzera mwa wina aliyense amene ndinamutumiza kwa inu?
18 Ублагав я був Тита, і з ним послав брата. Чи Тит ви́користав вас чим? Хіба ми ходили не в одно́му дусі? Хіба не одни́ми стопа́ми?
Ndinamupempha Tito kuti abwere kwanuko ndipo ndinamutumiza pamodzi ndi mʼbale wathu. Kodi kapena Tito anakudyerani masuku pamutu? Kodi iye ndi ine sitinachite zinthu mofanana ndi Mzimu mmodzi yemweyo?
19 Чи ви зно́ву не ду́маєте, що виправдуємось перед вами? Перед Богом, у Христі ми говоримо, а все, любі, на вашу будову!
Kodi mukuyesa kuti nthawi yonseyi takhala tikudzitchinjiriza tokha? Takhala tikuyankhula pamaso pa Mulungu monga anthu amene ali mwa Khristu; ndipo abwenzi okondedwa, chilichonse chimene timachita ndi chofuna kukulimbikitsani.
20 Я ж боюся, щоб, прийшовши, не знайшов вас такими, якими не хо́чу, і щоб мене не знайшли ви таким, якого не хочете, — хай не будуть між вами суперечка, заздрість, гніви, обмани, сва́ри, на́шепти, пихи́, безладдя,
Pakuti ndikuona kuti pamene ndibwera sindidzakupezani monga mmene ndikufunira kuti muzikhalira, ndipo simungadzandione monga mmene mukufunira kundionera. Ndikuopa kuti pangadzakhale mkangano, nsanje, kupserana mitima, kugawikana, ugogodi, miseche, kudzitukumula ndi chisokonezo.
21 щоб зно́ву, коли я прийду́, не прини́зив мене поміж вами мій Бог, і щоб мені не оплакувати багатьох, що перше згрішили були, і не покаялися в нечи́стості, і в пере́любі, і в розпусті, що ко́їли їх.
Ndikuopa kuti pamene ndidzabwerenso, Mulungu adzandichepetsa pamaso panu, ndipo ndidzamva chisoni ndi ambiri amene anachimwa kale ndipo sanalape zonyansa, zachigololo ndi zilakolako zoyipa zimene anachita.

< 2 до коринтян 12 >