< 2 до коринтян 10 >

1 А я сам, Павло, благаю вас ла́гідністю й ласка́вістю Христовою; я, коли присутній — слухня́ний між вами, а не бувши між вами — сміли́вий я супроти вас.
Mwa kufatsa ndi kuleza mtima kwa Khristu, ndikukupemphani, ine Paulo amene anthu ena amati ndimachita manyazi tikaonana maso ndi maso ndi inu, koma wosaopa pamene ndili kutali nanu!
2 І благаю, щоб я, прибувши, не осмі́лився надією, що нею я ду́маю сміли́вим бути проти деяких, що про нас вони гада́ють, ніби ми поступаємось за тілом.
Ndikukupemphani kuti ndikadzafika kumeneko ndisadzachite kuyankhula mwamphamvu monga mmene ndimayembekezera kudzachita kwa anthu ena amene amaganiza kuti machitidwe athu ndi ofanana ndi anthu a dziko lapansi.
3 Бо хо́дячи в тілі, не за тілом воюємо ми, —
Ngakhale ife timakhala mʼdziko lapansi, sitimenya nkhondo monga mmene dziko lapansi limachitira.
4 зброя бо нашого воюва́ння не тілесна, але міцна́ Богом на зруйнува́ння тверди́нь, — ми руйнуємо за́думи,
Pakuti zida zathu zankhondo si zida za dziko lapansi. Koma ndi mphamvu zochokera kwa Mulungu zotha kugwetsa malinga.
5 і всяке ви́несення, що підіймається проти пізна́ння Бога, і поло́нимо всяке знання́ на по́слух Христові,
Timagonjetsa maganizo onse onyenga ndiponso kudzikuza kulikonse kolimbana ndi anthu kuti asadziwe Mulungu. Ndipo timagonjetsa ganizo lililonse kuti limvere Khristu.
6 і покарати ми готові всякий непо́слух, коли зді́йсниться послух ваш.
Ndipo ife tidzakhala okonzeka kulanga aliyense wosamvera ngati inuyo mutakhala omvera kwenikweni.
7 Чи на обличчя ви дивитеся? Як хто певний про себе, що Христовий він, нехай ду́має знов по собі, що як сам він Христовий, так само Христові й ми.
Inu mukuweruza potengera zimene maso anu akuona. Ngati wina akutsimikiza kuti ndi wake wa Khristu, iye aganizenso kuti ifenso ndife a Khristu monga iye.
8 Бо коли б я ще більш став хвалитися нашою вла́дою, яку дав нам Господь на збудува́ння, а не на зруйнува́ння ваше, то не осоро́млюсь.
Tsono ngakhale nditadzitama momasuka za ulamuliro umene Ambuye anatipatsa woti tikukuzeni osati kukuwonongani, ndithu sindidzachita manyazi.
9 Та щоб не здавалось, ніби хочу лякати вас листами.
Ine sindikufuna kuoneka ngati ndikukuopsezani ndi makalata anga.
10 „Бо листи його — кажуть — важкі́ та міцні́, але особисто присутній — слабий, а мова його незначна́“,
Pakuti ena amati, “Makalata ake ndi awukali ndi amphamvu koma maonekedwe a thupi lake ndi wosagwira mtima ndipo mayankhulidwe ake ndi achabechabe.”
11 такий нехай знає оце, що які ми на слові в листах, неприсутніми бувши, такі ми й на ді́лі, присутніми бувши.
Anthu oterewa ayenera kuzindikira kuti zomwe timalemba mʼmakalata tili kutali ndi zomwe tidzakhale tili komweko.
12 Бо не сміємо вважати себе чи рівняти до інших, що самі себе хвалять, — вони нерозумно самі себе міряють собою, і рівняють з собою себе.
Sitikudziyika kapena kudzifananiza tokha ndi anthu ena amene amadziyenereza okha. Pamene akudzifanizira okha podziyerekeza ndi anzawo a mʼgulu lawo lomwe, ndi opanda nzeru.
13 Ми ж не будем хвалитись над міру, а в міру міри́ла, що його Бог призна́чив на міру для нас, щоб і до нас досягти́.
Komabe, ifeyo sitidzitama modutsa malire ake enieni, koma kudzitama kwathu kudzalekeza mʼmalire amene Mulungu anatiyikira, malire ake ndi mpaka kwa inu.
14 Бо ми не розтягуємося над міру, ніби не досягли́ ми до вас, бо ми досягли́ аж до вас із Єва́нгелією Христовою.
Pakuti sitikudzitama modutsa malire ngati kuti sitinafike kwa inu, popeza tinali oyamba kufika kwa inu ndi Uthenga Wabwino wa Khristu.
15 Ми не хвалимось над міру у чужих працях, але маємо надію, що як буде рости ваша віра, то за нашим міри́лом сильно звели́чимося ми між вами,
Choncho sitinyadiranso ntchito imene ena anayigwira. Chiyembekezo chathu nʼchakuti, pamene chikhulupiriro chanu chikukulirakulira, dera lathu la ntchito pakati panu lidzakulanso kwambiri,
16 щоб і в дальших за вами країнах звіщати Єва́нгелію, а не хвалитись готовим, як це чужі тве́рдять.
kuti tikalalikire Uthenga Wabwino mu zigawo zina kupitirira kwanuko. Pakuti sitikufuna kudzitama pa ntchito yogwira ena kale mʼdera la munthu wina.
17 А „хто хва́литься, нехай хва́литься в Господі!“
Koma, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
18 Бо достойний не той, хто сам себе хва́лить, але кого хвалить Госпо́дь!
Pakuti munthu amene amavomerezedwa, si amene amadziyenereza yekha, koma munthu amene Ambuye amuyenereza.

< 2 до коринтян 10 >