< 1 Тимофію 3 >

1 Вірне це слово: коли хто єпи́скопства хоче, — доброго діла він пра́гне.
Mawu woona ndi awa: Ngati munthu akufunitsitsa atakhala woyangʼanira, ndiye kuti akufuna ntchito yabwino.
2 А єпи́скоп має бути бездога́нний, муж однієї дружи́ни, тверезий, невинний, че́сний, гостинний до при́ходнів, здібний навчати,
Tsono woyangʼanira ayenera kukhala munthu wopanda chotsutsika nacho, mwamuna wa mkazi mmodzi yekha, woganiza bwino, wodziretsa, waulemu, wosamala bwino alendo, wodziwa kuphunzitsa.
3 не п'яни́ця, не заводія́ка, але тихий, несварли́вий, не сріблолюбець,
Asakhale chidakwa, asakhale wandewu, koma wofatsa, asakhale wokonda mikangano, kapena wokonda ndalama.
4 щоб добре ряди́в власним домом, що має дітей у слухня́ності з повною чесністю, —
Akhale wodziwa kusamala bwino banja lake ndi kulera ana ake bwino, kuti akhale omvera ndi aulemu weniweni.
5 бо хто власним домом ряди́ти не вміє, я́к він зможе пильнува́ти про Божу Церкву? —
(Ngati munthu sadziwa kusamala banja lake lomwe, angathe bwanji kusamala mpingo wa Mulungu?)
6 не новонаве́рнений, щоб він не запишався, і не впав у ворожий о́суд.
Asakhale wongotembenuka mtima kumene kuopa kuti angadzitukumule napezeka pa chilango monga Satana.
7 Треба, щоб мав він і добре засві́дчення від чужи́нців, щоб не впасти в догану та в сітку диявольську.
Ayeneranso kukhala munthu wambiri yabwino ndi akunja, kuti anthu asamutonze nagwa mu msampha wa Satana.
8 Так само диякони́ мають бути поважні, не двомовці, не багато відда́ні вину, не соромнозахла́нні,
Momwemonso atumiki, akhale anthu oyenera ulemu, woona mtima, osakhala okonda zoledzeretsa, osakonda kupeza zinthu mwachinyengo.
9 такі, що мають таємни́цю віри при чистім сумлінні.
Ayenera kugwiritsa mozama choonadi cha chikhulupiriro ndi kukhala ndi chikumbumtima chabwino.
10 Отже, і вони нехай перш випробо́вуються, а потому хай служать, якщо бу́дуть бездога́нні.
Ayambe ayesedwa kaye, ndipo ngati palibe kanthu kowatsutsa, aloleni akhale atumiki.
11 Так само жінки́ нехай будуть поважні, не обмовли́ві, тверезі та вірні в усьому.
Momwemonso, akazi akhale olemekezeka, osasinjirira koma oganiza bwino ndi odalirika pa chilichonse.
12 Диякони́ мусять бути мужі однієї дружи́ни, що добре рядя́ть дітьми́ й своїми домами.
Mtumiki akhale wokhulupirika kwa mkazi wake ndipo ayenera kukhala wosamalira bwino ana ake ndi onse a pa khomo pake.
13 Бо хто добре виконує службу, той до́брий ступі́нь набуває собі та велику відвагу в вірі через Христа Ісуса.
Iwo amene atumikira bwino amakhala ndi mbiri yabwino ndipo amakhala chitsimikizo chachikulu cha chikhulupiriro chawo mwa Khristu Yesu.
14 Це пишу́ я тобі, і сподіваюсь до тебе прийти незаба́ром.
Ngakhale ndili ndi chiyembekezo choti ndifika komweko posachedwapa, ndikukulemberani malangizo awa.
15 А коли я спізнюся, то щоб знав ти, як треба пово́дитися в Божому домі, що ним є Церква Бога Живого, стовп і підвалина пра́вди.
Ine zina zikandichedwetsa kubwera, mudziwe za mmene anthu ayenera kukhalira mʼNyumba ya Mulungu, imene ndi mpingo wa Mulungu wamoyo, mzati ndi maziko achoonadi.
16 Безсумнівно, велика це таємни́ця благоче́стя: Хто в тілі з'яви́вся, Той оправданий Духом, а́нгола́м показався, проповіданий був між наро́дами, увірувано в Нього в світі, Він у славі вознісся!
Mosakayikira, chinsinsi cha chikhulupiriro chathu chachikulu: Khristu anaonekera ali ndi thupi la munthu, Mzimu anamuchitira umboni, angelo anamuona, analalikidwa pakati pa mitundu yonse, dziko lapansi linamukhulupirira, anatengedwa kupita kumwamba mwa ulemerero.

< 1 Тимофію 3 >