< 1 до солунян 5 >

1 А про часи́ та про по́ри, брати, не потрібно писати до вас,
Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni,
2 бо самі ви докладно те знаєте, що при́йде день Господній так, як злодій вночі.
chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku.
3 Бо коли говоритимуть: „Мир і безпечність“, тоді несподівано при́йде заги́біль на них, як му́ка тієї, що носить в утро́бі, — і вони не втечуть!
Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.
4 А ви, браття, не в те́мряві, щоб той день захопи́в вас, як злодій.
Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala.
5 Бо ви всі сини світла й сини дня. Не належимо ми ночі, ні те́мряві.
Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima.
6 Тож не бу́демо спати, як інші, а пильнуймо та будьмо твере́зі!
Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga.
7 Ті бо, що сплять — сплять уночі, а ті, що напиваються — вночі напиваються.
Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku.
8 А ми, що належимо дневі, будьмо тверезі, зодягнувшися в броню́ віри й любови, та в шоло́м надії спасі́ння,
Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa.
9 бо Бог нас не призна́чив на гнів, але щоб спасі́ння оде́ржали Господом нашим Ісусом Христом,
Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
10 що помер був за нас, щоб, чи пильнуємо ми чи спимо́, укупі з Ним ми жили́.
Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi.
11 Утішайте тому́ один о́дного, і збудо́вуйте один о́дного, — як і чините ви!
Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.
12 Благаємо ж, бра́ття, ми вас, — шануйте тих, що працюють між вами, і в вас старшину́ють у Господі, і навчають вас вони,
Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani.
13 і в великій любові їх майте за їхню працю. Між собою заховуйте мир!
Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.
14 Благаємо ж, бра́ття, ми вас: напоумля́йте непорядних, потішайте малодушних, підтримуйте слаби́х, усім довготерпіть!
Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense.
15 Глядіть, щоб ніхто ніко́му не віддавав злом за зло, але за́вжди дбайте про добро один для о́дного й для всіх!
Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.
16 За́вжди радійте!
Kondwerani nthawi zonse.
17 Безперестанку моліться!
Pempherani kosalekeza.
18 Подяку складайте за все, бо така Божа воля про вас у Христі Ісусі.
Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.
19 Духа не вгаша́йте!
Musazimitse moto wa Mzimu Woyera.
20 Не горду́йте пророцтвами!
Musanyoze mawu a uneneri.
21 Усе досліджуючи, тримайтеся доброго!
Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino.
22 Стережіться лихого в усякому ви́гляді!
Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.
23 А Сам Бог миру нехай освя́тить вас цілко́м доскона́ло, а непору́шений дух ваш, і душа, і тіло нехай непорочно збере́жені бу́дуть на при́хід Господа нашого Ісуса Христа!
Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu.
24 Вірний Той, Хто вас кличе, — Він і вчинить оте!
Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.
25 Бра́ття, моліться за нас!
Abale, mutipempherere.
26 Привітайте всю бра́ттю святим поцілунком!
Perekani moni wachikondi kwa onse.
27 Заклинаю вас Господом, — цього листа прочитати перед усіма́ братами!
Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.
28 Благода́ть Господа нашого Ісуса Христа нехай буде з вами. Амі́нь!
Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.

< 1 до солунян 5 >