< 1 Івана 3 >

1 Подивіться, яку любов дав нам Отець, щоб ми були дітьми́ Божими, і ними ми є. Світ нас не знає тому́, що Його не пізнав.
Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye.
2 Улю́блені, — ми тепер Божі діти, але ще не виявилось, що́ ми будемо. Та знаємо, що, коли з'я́виться, то бу́дем подібні до Нього, бо бу́демо бачити Його, як Він є.
Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili.
3 І кожен, хто має на Нього наді́ю оцю, очищає себе так же само, як чистий і Він.
Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.
4 Кожен, хто чинить гріх, чинить і беззако́ння. Бо гріх — то беззако́ння.
Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo.
5 І ви знаєте, що Він був з'явився, щоб гріхи наші взяти, а гріха в Нім нема.
Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo.
6 Кожен, хто в Нім пробува́є, не грішить; усякий, хто грішить, не бачив Його, і не пізнав Його.
Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.
7 Діточки, хай ніхто вас не зво́дить! Хто чинить праведність, той праведний, як праведний Він!
Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama.
8 Хто чинить гріх, той від диявола, бо диявол грішить від поча́тку. Тому́ то з'явився Син Божий, щоб зни́щити справи диявола.
Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi.
9 Кожен, хто родився від Бога, не чинить гріха, бо в нім пробуває насіння Його. І не може грішити, бо від Бога наро́джений він.
Aliyense amene ndi mwana wa Mulungu, sachimwirachimwira, popeza mbewu ya Mulungu ili mwa iye, sangathe kuchimwa, chifukwa ndi mwana wa Mulungu.
10 Цим пізнаю́ться діти Божі та діти дияволові: Кожен, хто нраведности не чинить, той не від Бога, як і той, хто брата свого не любить!
Mmenemu ndi mmene timadziwira ana a Mulungu ndi amene ali ana a mdierekezi. Aliyense amene sachita chilungamo si mwana wa Mulungu; ngakhalenso amene sakonda mʼbale wake.
11 Бо це та звістка, яку від початку ви чули, — щоб любили один о́дного,
Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake.
12 не так, як той Каїн, що був від лукавого, і брата свого́ забив. А за що він забив його? Бо лукаві були його вчинки, а брата його — праведні.
Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama.
13 Не дивуйтеся, бра́ття мої, коли світ вас нена́видить!
Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu.
14 Ми знаємо, що ми перейшли від смертн в життя, бо любимо братів. А хто брата не любить, пробуває той в смерті.
Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa.
15 Кожен, хто нена́видить брата свого, той душогу́б. А ви знаєте, що жоден душогуб не має вічного життя, що в нім перебувало б. (aiōnios g166)
Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha. (aiōnios g166)
16 Ми з того пізнали любов, що ду́шу Свою́ Він покла́в був за нас. І ми мусимо класти ду́ші за братів!
Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu.
17 А хто має достаток на світі, і бачить брата свого в недостачі, та серце своє зачиняє від нього, то як Божа любов пробуває в такому?
Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu?
18 Ді́точки, — любімо не словом, ані язико́м, але ді́лом та правдою!
Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi.
19 Із цього дові́дуємось, що ми з правди, і впокорюєм наші серця́ перед Ним,
Pamenepo tidzadziwa kuti tili pa choonadi ndipo tidzakhala okhazikika mtima pamaso pa Mulungu,
20 бо коли винуватить нас серце, то Бог більший від нашого серця та ві́дає все!
nthawi zonse pamene mtima wathu utitsutsa. Pakuti Mulungu ndi wamkulu kuposa mitima yathu ndipo Iye amadziwa zonse.
21 Улю́блені, — коли не винуватить нас серце, то маємо відвагу до Бога,
Anzanga okondedwa, ngati mitima yathu sikutitsutsa, tili nako kulimbika mtima pamaso pa Mulungu.
22 і чого́ тільки попро́симо, одержимо від Нього, бо виконуємо Його заповіді та чинимо любе для Нього.
Ndipo timalandira chilichonse chimene tichipempha kwa Iye, chifukwa timamvera malamulo ake ndi kuchita zimene zimamukondweretsa.
23 І оце Його заповідь, щоб ми вірували в Ім'я́ Сина Його — Ісуса Христа, і щоб любили один о́дного, як Він нам заповідь дав!
Ndipo lamulo lake ndi ili: kukhulupirira dzina la Mwana wake, Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga Iye anatilamulira.
24 А хто Його заповіді береже́, той у Нім пробуває, а Він у ньому. А що в нас пробуває, пізнає́мо це з того Духа, що Він нам Його дав.
Iwo amene amamvera malamulo ake amakhala mwa Iye, ndipo Iye amakhala mwa iwo. Ndipo mmenemu ndi momwe timadziwira kuti Iye akukhala mwa ife. Timadziwa mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa.

< 1 Івана 3 >