< 1 до коринтян 5 >

1 Всюди чути, що між вами пере́люб, і то такий пере́люб, який і між поганами незна́ний, — що хтось має за дружи́ну собі дружину ба́тькову.
Mbiri yamveka kuti pakati panu pakuchitika chigololo. Ndipo chigololo cha mtunduwu ngakhale pakati pa akunja sichingapezeke; munthu akumagonana ndi mkazi wa abambo ake.
2 І ви завелича́лися, а не засмутились радніш, щоб був вилучений з-поміж вас, хто цей учинок зробив.
Ndipo inu mukudzitukumulabe. Kodi simukanayenera kudzazidwa ndi chisoni ndipo mukanamuchotsa pa chiyanjano chanu munthu wochita zimenezi?
3 Отож я, відсутній тілом, та присутній духом, уже розсудив, як присутній між вами: того, хто так учинив це,
Ngakhale sindili nanu mʼthupi, ndili nanu mu mzimu. Ndipo ineyo ndapereka kale chiweruzo pa munthu amene amachita zotere, ngati kuti ndili komweko.
4 у Ім'я́ Господа Ісуса, як зберетеся ви та мій дух, із силою Господа нашого Ісуса, —
Mukasonkhana mu dzina la Ambuye athu Yesu, ine ndili nanu mu mzimu, ndipo mphamvu ya Ambuye athu Yesu ili pomwepo,
5 віддати такого сатані на погибіль тіла, щоб дух спасся Господнього дня!
mumupereke munthuyu kwa Satana, kuti chikhalidwe chake cha uchimo chiwonongedwe ndikuti mzimu wake udzapulumuke pa tsiku la Ambuye.
6 Велича́ння ваше не добре. Хіба ви не знаєте, що мала ро́зчина все тісто заква́шує?
Kudziwa kwanu si kwabwino. Kodi simukudziwa kuti yisiti wochepa amafufumitsa mphumphu yaufa wonse wa tirigu?
7 Отож, очистьте стару́ ро́зчину, щоб стати вам нови́м тістом, бо ви прісні́, бо наша Пасха, Христос, за нас у жертву прине́сений.
Chotsani yisiti wakale kuti mukhale ndi mphumphu yopanda yisiti, monga inu muli. Pakuti Khristu, Mwana Wankhosa wa Paska wathu, anaperekedwa nsembe.
8 Тому́ святкуймо не в давній ро́зчині, ані в ро́зчині злоби́ й лука́вства, але в опрі́сноках чистости та правди!
Choncho, tiyeni tisunge chikondwererochi, osati ndi yisiti wakale, wowononga ndi woyipa, koma ndi buledi wopanda yisiti, buledi woona mtima ndi choonadi.
9 Я писав вам у листі не єдна́тися з перелю́бниками, —
Ndakulemberani mʼkalata yanga kuti musayanjane nawo anthu achigololo.
10 але не взагалі з цьогосвітніми перелю́бниками, чи з користолю́бцями, чи з хижака́ми, чи з ідоля́нами, бо ви мусіли були б відійти від світу.
Pamenepatu sindikutanthauzatu anthu a dziko lapansi lino amene ndi achigololo, kapena aumbombo, kapena opeza ndalama mwachinyengo, kapena opembedza mafano. Kukanatero mukanangochoka mʼdziko lapansi lino.
11 А тепер я писав вам не єднатися з тим, хто зветься братом, та є перелю́бник, чи користолю́бець, чи ідоля́нин, чи злоріка, чи п'яни́ця, чи хижа́к, — із такими навіть не їсти!
Koma tsopano ndikukulemberani kuti musayanjane ndi aliyense amene adzitcha mʼbale koma ndi wachigololo, kapena waumbombo, kapena wopembedza mafano, kapena wonamizira anzake, woledzera kapena wopeza ndalama mwachinyengo. Munthu wotere ngakhale kudya, osadya naye pamodzi.
12 Бо що ж мені судити й чужих? Чи ви не судите своїх?
Kodi ndipindulanji kuti ndiweruze anthu amene si a mu mpingo? Kodi simuyenera kuweruza iwo amene ali mu mpingo?
13 А чужих судить Бог. Тож ви́лучіть лукавого з-поміж себе сами́х!
Mulungu adzaweruza akunja. “Chotsani woyipayo pakati panu.”

< 1 до коринтян 5 >