< 2 до коринтян 10 >

1 Я, Павло, особисто закликаю вас із лагідністю і добротою Христа, – я, той хто «покірний, коли присутній» між вами, «а коли відсутній, то сміливий» стосовно вас.
Mwa kufatsa ndi kuleza mtima kwa Khristu, ndikukupemphani, ine Paulo amene anthu ena amati ndimachita manyazi tikaonana maso ndi maso ndi inu, koma wosaopa pamene ndili kutali nanu!
2 Прошу вас: коли я прийду, не змушуйте мене вдаватися до сміливості, яку я рішуче розраховую проявити щодо тих, хто вважає, що ми живемо по-тілесному.
Ndikukupemphani kuti ndikadzafika kumeneko ndisadzachite kuyankhula mwamphamvu monga mmene ndimayembekezera kudzachita kwa anthu ena amene amaganiza kuti machitidwe athu ndi ofanana ndi anthu a dziko lapansi.
3 Адже, живучи в тілі, воюємо не по-тілесному.
Ngakhale ife timakhala mʼdziko lapansi, sitimenya nkhondo monga mmene dziko lapansi limachitira.
4 І зброя нашої боротьби не тілесна, а сильна Богом для руйнування фортець. Ми руйнуємо задуми
Pakuti zida zathu zankhondo si zida za dziko lapansi. Koma ndi mphamvu zochokera kwa Mulungu zotha kugwetsa malinga.
5 та кожну зарозумілість, яка противиться пізнанню Бога, а також беремо в полон кожну думку на послух Христу.
Timagonjetsa maganizo onse onyenga ndiponso kudzikuza kulikonse kolimbana ndi anthu kuti asadziwe Mulungu. Ndipo timagonjetsa ganizo lililonse kuti limvere Khristu.
6 І ми готові покарати будь-яку непокору, як тільки ваш послух стане довершеним.
Ndipo ife tidzakhala okonzeka kulanga aliyense wosamvera ngati inuyo mutakhala omvera kwenikweni.
7 Ви дивитеся на зовнішність. Але коли хтось впевнений, що він належить Христу, то нехай візьме до уваги, що ми, як і він, Христові.
Inu mukuweruza potengera zimene maso anu akuona. Ngati wina akutsimikiza kuti ndi wake wa Khristu, iye aganizenso kuti ifenso ndife a Khristu monga iye.
8 І навіть якщо я ще більше вихваляюся нашою владою, яку нам дав Господь для вашого збудування, а не для руйнування, то я за це не буду осоромлений.
Tsono ngakhale nditadzitama momasuka za ulamuliro umene Ambuye anatipatsa woti tikukuzeni osati kukuwonongani, ndithu sindidzachita manyazi.
9 Хай вам не здається, що я хочу залякати вас [своїми] листами.
Ine sindikufuna kuoneka ngati ndikukuopsezani ndi makalata anga.
10 Адже [дехто] каже: «Його листи вагомі та сильні, але коли приходить особисто, то він слабкий і слова його незначні».
Pakuti ena amati, “Makalata ake ndi awukali ndi amphamvu koma maonekedwe a thupi lake ndi wosagwira mtima ndipo mayankhulidwe ake ndi achabechabe.”
11 Така людина нехай врахує те, що якими ми є на слові в листах, коли відсутні, такими ж є і на ділі, коли присутні.
Anthu oterewa ayenera kuzindikira kuti zomwe timalemba mʼmakalata tili kutali ndi zomwe tidzakhale tili komweko.
12 Ми не сміємо судити або прирівнювати себе до тих, що самі себе рекомендують. Вони, вимірюючи себе собою та порівнюючи себе із собою, не є розумними.
Sitikudziyika kapena kudzifananiza tokha ndi anthu ena amene amadziyenereza okha. Pamene akudzifanizira okha podziyerekeza ndi anzawo a mʼgulu lawo lomwe, ndi opanda nzeru.
13 Ми ж не будемо хвалитися безмірно, а лише в межах служіння, яке нам визначив Бог, щоб досягнути й вас.
Komabe, ifeyo sitidzitama modutsa malire ake enieni, koma kudzitama kwathu kudzalekeza mʼmalire amene Mulungu anatiyikira, malire ake ndi mpaka kwa inu.
14 Бо ми не виходимо за ці межі, ніби не досягнули вас, адже ми досягнули і вас Доброю Звісткою Христа.
Pakuti sitikudzitama modutsa malire ngati kuti sitinafike kwa inu, popeza tinali oyamba kufika kwa inu ndi Uthenga Wabwino wa Khristu.
15 Ми не хвалимося надмірно чужою працею, а сподіваємося, що, у міру того, як ваша віра зростатиме, зростатимуть і межі нашого служіння серед вас,
Choncho sitinyadiranso ntchito imene ena anayigwira. Chiyembekezo chathu nʼchakuti, pamene chikhulupiriro chanu chikukulirakulira, dera lathu la ntchito pakati panu lidzakulanso kwambiri,
16 щоби звіщати Добру Звістку поза вашими [околицями], а не хвалитися зробленим на чужому полі.
kuti tikalalikire Uthenga Wabwino mu zigawo zina kupitirira kwanuko. Pakuti sitikufuna kudzitama pa ntchito yogwira ena kale mʼdera la munthu wina.
17 «А хто вихваляється, нехай вихваляється в Господі».
Koma, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
18 Адже схвалений не той, хто сам себе рекомендує, а той, кого рекомендує Господь.
Pakuti munthu amene amavomerezedwa, si amene amadziyenereza yekha, koma munthu amene Ambuye amuyenereza.

< 2 до коринтян 10 >